-
“Mulungu Akonda Wopereka Mokondwera”Nsanja ya Olonda—1998 | November 1
-
-
Paulo anapempha thandizo kumipingo yakutali monga ku Makedoniya, ndipo analinganiza kuti pakhale zopereka zokathandizira Akristu okanthidwa ndi njala ku Yudeya. Kwa Akorinto, Paulo analemba kuti: “Monga ndinalangiza Mipingo ya ku Galatiya, motero chitani inunso. Tsiku loyamba la sabata yense wa inu asunge yekha, monga momwe anapindula.”a—1 Akorinto 16:1, 2.
-
-
“Mulungu Akonda Wopereka Mokondwera”Nsanja ya Olonda—1998 | November 1
-
-
a Ngakhale kuti Paulo ‘analangiza,’ sizikutanthauza kuti anaika malamulo ake oti aliyense adziwatsatira. M’malo mwake, Paulo anali kungoyang’anira zoperekazo, zochokera kumipingo ingapo. Ndiponso, Paulo ananena kuti aliyense ‘payekha’ anafunikira kupereka “monga momwe anapindula.” M’mawu ena, chopereka chilichonse chinayenera kuperekedwa ndi munthu kwayekha ndiponso modzifunira. Palibe amene anakakamizidwa.
-