-
Miliri ya Yehova pa Matchalitchi AchikhristuMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
29. Kodi “nyenyezi yaikulu yoyaka ngati nyale” ikuimira chiyani, ndipo n’chifukwa chiyani tikutero?
29 M’mitu ya m’mbuyomu, taona kale zimene nyenyezi imaimira m’mauthenga a Yesu opita kumipingo 7. M’mauthenga amenewa, nyenyezi 7 zimaimira akulu a m’mipingo.b (Chivumbulutso 1:20) “Nyenyezi,” kapena kuti akulu odzozedwa pamodzi ndi Akhristu onse odzozedwa, mwauzimu amakhala m’malo awo a kumwamba kuyambira pa nthawi imene anadindidwa chidindo ndi mzimu woyera ngati chikole chotsimikizira kuti adzalandira cholowa chawo kumwamba. (Aefeso 2:6, 7) Komabe, mtumwi Paulo anachenjeza kuti pakati pa anthu okhala ngati nyenyezi amenewa padzatuluka anthu a mpatuko ndiponso oyambitsa magawano, amene adzasocheretsa nkhosa. (Machitidwe 20:29, 30) Akulu osakhulupirikawo adzachititsa kuti pakhale mpatuko waukulu, ndipo iwo adzakhala “munthu wosamvera malamulo,” yemwe adzadzikweze kuti afanane ndi Mulungu pakati pa anthu. (2 Atesalonika 2:3, 4) Zimene Paulo anachenjezazi zinayamba kuchitika pamene atsogoleri a Matchalitchi Achikhristu anayamba kuonekera. M’pake kuti gulu la atsogoleri limeneli likuimiridwa ndi “nyenyezi yaikulu yoyaka ngati nyale.”
-
-
Miliri ya Yehova pa Matchalitchi AchikhristuMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
31. (a) Kodi atsogoleri a Matchalitchi Achikhristu anagwa liti kuchokera m’malo awo “akumwamba”? (b) Kodi n’chifukwa chiyani madzi amene atsogoleri a zipembedzo amapereka ali ngati “chitsamba chowawa,” ndipo anthu ambiri amene alandira madzi amenewa chawachitikira n’chiyani?
31 Anthu ena atachoka m’Chikhristu choona n’kukhala atsogoleri a Matchalitchi Achikhristu, anagwa kuchokera m’malo awo okwezeka “akumwamba” amene anatchulidwa ndi Paulo pa Aefeso 2:6, 7. M’malo mopereka madzi abwino a choonadi kwa anthu awo, iwo anapereka “chitsamba chowawa,” chomwe ndi ziphunzitso zabodza. Zina mwa ziphunzitso zimenezi ndi zakuti anthu oipa amakapsa kumoto, zoti kuli malo otchedwa puligatoliyo, zoti pali milungu itatu mwa Mulungu mmodzi, ndiponso zoti Mulungu analemberatu zilizonse zimene zimachitika pa moyo wa munthu. Komanso iwo anachititsa kuti anthu azimenya nkhondo m’malo mowalimbikitsa kuti akhale atumiki a Mulungu amakhalidwe abwino. Kodi zotsatira zake zinali zotani? Anthu amene anakhulupirira mabodza amenewa anadyetsedwa poizoni wauzimu. Zimene zinawachitikira n’zofanana ndi zimene zinachitikira Aisiraeli osakhulupirika a m’nthawi ya Yeremiya. Ponena za Aisiraeli amenewa, Yehova anati: “Ndiwadyetsa chitsamba chowawa ndipo ndiwamwetsa madzi apoizoni. Chifukwa kuchokera mwa aneneri a ku Yerusalemu mpatuko wafalikira m’dziko lonse.”—Yeremiya 9:15; 23:15.
-