-
“Mulimbanetu Chifukwa cha Chikhulupiriro”!Nsanja ya Olonda—1998 | June 1
-
-
5. Kodi Yuda akugwira mawu mneneri wakale uti, ndipo kodi ulosi umenewo unasonyeza motani kuti udzakwaniritsidwadi?
5 Kenako, Yuda akutchula chiweruzo chachikulu kwambiri. Akugwira mawu ulosi wa Enoke—nkhani yopezeka pano pokha m’Malemba onse ouziridwa.a (Yuda 14, 15) Enoke analosera nthaŵi pamene Yehova adzaweruza anthu onse osaopa Mulungu pamodzi ndi zochita zawo zopanda umulungu. Komano, Enoke analankhula monga kuti zinachitika kale, popeza kuti ziweruzo za Mulungu zinali zotsimikizirika zedi monga kuti zinachitika kale. Anthu ayenera kuti ananyoza Enoke ndipo kenako Nowa, koma onyoza onse ameneŵo anafa ndi madzi pa Chigumula cha dziko lonse.
-
-
“Mulimbanetu Chifukwa cha Chikhulupiriro”!Nsanja ya Olonda—1998 | June 1
-
-
a Ofufuza ena amanena kuti Yuda anali kugwira mawu buku lopanda umboni lotchedwa kuti Buku la Enoke. Komabe, R. C. H. Lenski akuti: “Tikufunsa kuti: ‘Kodi buku lankhani zosiyanasiyana limeneli, Buku la Enoke, linachokera kuti?’ Buku limeneli linangosonkhanitsa nkhani zosiyanasiyana, ndipo palibe amene angatsimikizire za madeti a zigawo zake zosiyanasiyana . . . ; palibe amene ali ndi umboni wakuti mawu ake ena sanatengedwe kwa Yuda iye mwini.”
-