-
Tiyesetse Kuti Tipambane pa NkhondoMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
3. (a) Kodi Yesu analimbikitsa bwanji Akhristu a mpingo wa ku Simuna? (b) Ngakhale kuti Akhristu a ku Simuna anali osauka, n’chifukwa chiyani Yesu ananena kuti iwo anali “olemera”?
3 Iye anati: “Ndikudziwa masautso ako ndi umphawi wako, koma ndiwe wolemera. Ndikudziwanso za kutonza kwa odzitcha Ayudawo, pamene si Ayuda, koma ndiwo sunagoge wa Satana.” (Chivumbulutso 2:9) Yesu sanadzudzule abale ake a mumpingo wa ku Simuna, koma anangowayamikira. Iwo anazunzidwa kwambiri chifukwa cha chikhulupiriro chawo. Akhristuwo anali osauka, mwina chifukwa chakuti anali okhulupirika. (Aheberi 10:34) Koma chinthu chofunika kwambiri pa moyo wawo chinali zinthu zauzimu, ndipo anasunga chuma kumwamba monga mmene Yesu anawalangizira. (Mateyu 6:19, 20) Motero Yesu, yemwe ndi M’busa Wamkulu, ankawaona kuti ndi “olemera.”—Yerekezerani ndi Yakobo 2:5.
4. Kodi ndani amene ankazunza kwambiri Akhristu a ku Simuna ndipo Yesu ankawaona bwanji anthu ozunzawo?
4 Yesu anayamikira Akhristu a mpingo wa ku Simuna makamaka chifukwa choti anapirira potsutsidwa kwambiri ndi Ayuda. Chikhristu chitangoyamba kumene, anthu ambiri a m’chipembedzo cha Chiyuda ankatsutsa kwambiri Akhristuwo n’cholinga choti Chikhristu chisafalikire. (Machitidwe 13:44, 45; 14:19) Tsopano patangopita zaka zowerengeka mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, Ayuda a ku Simuna nawonso ankasonyeza mtima wa Satana umenewo. N’chifukwa chake Yesu ankawaona kuti iwo ndi “sunagoge wa Satana.”a
-
-
Tiyesetse Kuti Tipambane pa NkhondoMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
a Patapita zaka pafupifupi 60 Yohane atamwalira, munthu wina wa zaka 86 dzina lake Polycarp, anaphedwa mumzinda wa Simuna powotchedwa chifukwa chokana kusiya kukhulupirira Yesu. Buku linalake lofotokoza za kuphedwa kwa Polycarp, lomwe anthu amakhulupirira kuti linalembedwa m’nthawi imene iye anaphedwa, linanena kuti pamene anthu ankasonkhanitsa nkhuni zomuwotchera, “monga mwa chizolowezi chawo, Ayuda anajijirika kwambiri pothandizira pa ntchitoyi.” Iwo anachita zimenezi ngakhale kuti limeneli linali “tsiku la Sabata lapadera.”—The Martyrdom of Polycarp.
-