Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 49
  • Kodi Mdyerekezi Amakhala Kuti?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mdyerekezi Amakhala Kuti?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Mdani wa Moyo Wosatha
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Satana
    Galamukani!—2013
  • “Tsutsani Mdyerekezi” Monga Anachitira Yesu
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Olamulira Okhala m’Malo a Mizimu
    Nsanja ya Olonda—1995
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 49

Kodi Mdyerekezi Amakhala Kuti?

Yankho la m’Baibulo

Mdyerekezi amakhala kumalo osaoneka chifukwa ndi cholengedwa chauzimu. Koma sikuti malo amenewa ndi ku Gehena woyaka moto kumene anthu ena amati anthu oipa amakazunzikako ngati mmene chithunzi cha m’nkhaniyi chikusonyezera.

“Nkhondo kumwamba”

Nthawi ina Satana ankatha kuyendayenda kumwamba komanso kupita kumene kunali Mulungu ndi angelo okhulupirika. (Yobu 1:6) Koma Baibulo linalosera kuti kudzakhala “nkhondo kumwamba.” Nkhondo imeneyi inachititsa kuti Satana adzachotsedweko “n’kuponyedwa kudziko lapansi.” (Chivumbulutso 12:7-9) Nkhani zimene zinalembedwa m’Baibulo komanso zinthu zimene zikuchitika padzikoli zikusonyeza kuti nkhondo imeneyi inachitika kale. Mdyerekezi panopa ali padziko lapansili.

Kodi zimenezi zikutanthauza kuti pali malo enieni padziko lapansi pano kumene kumakhala Mdyerekezi? Mwachitsanzo mzinda wakale wa Pegamo unatchulidwa kuti ndi malo “kumene kuli mpando wachifumu wa Satana” komanso ‘n’kumene Satana akukhala.’ (Chivumbulutso 2:13) Mawu amenewa akungotanthauza kuti anthu ambiri mumzindawu ankakonda kulambira Satana. Baibulo limanena kuti Mdyerekezi amalamulira “maufumu onse a padziko lapansi,” choncho sakhala malo amodzi padzikoli koma ali padziko lapansi.—Luka 4:5, 6.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena