Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yehova Amayamikira Utumiki Wanu wa Mtima Wonse
    Nsanja ya Olonda—1997 | October 15
    • 5. Kodi chitsanzo cha atumwi chimasonyeza motani kuti onse sangachite mofanana mu utumiki?

      5 Kodi kutumikira ndi mtima wonse kumatanthauza kuti tiyenera kutero pamlingo wofanana? Zimenezo sizingatheke nkomwe, popeza kuti mikhalidwe ndi kukhoza zimasiyanasiyana pakati pa wina ndi mnzake. Talingalirani za atumwi okhulupirika a Yesu. Iwo sanali kuchita zofanana. Mwachitsanzo, timadziŵa zochepa kwambiri ponena za atumwi ena, monga Simoni Mkanani ndi Yakobo mwana wa Alifeyo. Mwinamwake anali kuchita zochepa m’ntchito zawo monga atumwi. (Mateyu 10:2-4) Mosiyana ndi zimenezo, Petro anavomereza maudindo ambiri ovuta​—inde, mpaka Yesu anampatsa “mafungulo a Ufumu”! (Mateyu 16:19) Komabe, Petro sanaikidwe monga wamkulu kuposa anzakewo. Pamene Yohane anaona masomphenya a Yerusalemu Watsopano m’Chivumbulutso (cha m’ma 96 C.E.), iye anaona maziko 12 pamene panalembedwa “maina khumi ndi aŵiri a atumwi khumi ndi aŵiri.”a (Chivumbulutso 21:14) Yehova anayamikira utumiki wa atumwi onse, ngakhale kuti mwachionekere ena anachita zambiri kuposa anzawo.

  • Yehova Amayamikira Utumiki Wanu wa Mtima Wonse
    Nsanja ya Olonda—1997 | October 15
    • a Popeza kuti Matiya analoŵa m’malo mwa Yudase monga mtumwi, dzina lake​—osati la Paulo​—liyenera kuti linaonekera pakati pa maziko 12 amenewo. Ngakhale kuti Paulo anali mtumwi, iye sanali mmodzi wa 12 amenewo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena