-
Yehova Amayamikira Utumiki Wanu wa Mtima WonseNsanja ya Olonda—1997 | October 15
-
-
5. Kodi chitsanzo cha atumwi chimasonyeza motani kuti onse sangachite mofanana mu utumiki?
5 Kodi kutumikira ndi mtima wonse kumatanthauza kuti tiyenera kutero pamlingo wofanana? Zimenezo sizingatheke nkomwe, popeza kuti mikhalidwe ndi kukhoza zimasiyanasiyana pakati pa wina ndi mnzake. Talingalirani za atumwi okhulupirika a Yesu. Iwo sanali kuchita zofanana. Mwachitsanzo, timadziŵa zochepa kwambiri ponena za atumwi ena, monga Simoni Mkanani ndi Yakobo mwana wa Alifeyo. Mwinamwake anali kuchita zochepa m’ntchito zawo monga atumwi. (Mateyu 10:2-4) Mosiyana ndi zimenezo, Petro anavomereza maudindo ambiri ovuta—inde, mpaka Yesu anampatsa “mafungulo a Ufumu”! (Mateyu 16:19) Komabe, Petro sanaikidwe monga wamkulu kuposa anzakewo. Pamene Yohane anaona masomphenya a Yerusalemu Watsopano m’Chivumbulutso (cha m’ma 96 C.E.), iye anaona maziko 12 pamene panalembedwa “maina khumi ndi aŵiri a atumwi khumi ndi aŵiri.”a (Chivumbulutso 21:14) Yehova anayamikira utumiki wa atumwi onse, ngakhale kuti mwachionekere ena anachita zambiri kuposa anzawo.
-
-
Yehova Amayamikira Utumiki Wanu wa Mtima WonseNsanja ya Olonda—1997 | October 15
-
-
a Popeza kuti Matiya analoŵa m’malo mwa Yudase monga mtumwi, dzina lake—osati la Paulo—liyenera kuti linaonekera pakati pa maziko 12 amenewo. Ngakhale kuti Paulo anali mtumwi, iye sanali mmodzi wa 12 amenewo.
-