-
‘Ndani Ali Woyenera Kutsegula Mpukutu?’Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
14. (a) Kodi zamoyo zinayi pamodzi ndi akulu 24 anachita chiyani Yesu atalandira mpukutu? (b) Kodi zimene Yohane anaona zokhudza akulu 24 aja zikutithandiza bwanji kuwazindikira bwino komanso kuzindikira udindo wawo?
14 Kodi zamoyo zinayi pamodzi ndi akulu 24 amene anazungulira mpando wachifumu wa Yehova, anachita chiyani? “Atatenga mpukutuwo, zamoyo zinayi ndi akulu 24 aja anagwada ndi kuwerama pamaso pa Mwanawankhosa. Aliyense wa iwo anali ndi zeze woimbira ndi mbale yagolide yodzaza ndi zofukiza. Zofukizazo zikuimira mapemphero a oyera.” (Chivumbulutso 5:8) Mofanana ndi zamoyo zinayi zomwe zinazungulira mpando wachifumu wa Mulungu, zomwe ndi akerubi, akulu 24 anagwada ndi kuweramira Yesu. Iwo anachita zimenezi posonyeza kuti akuzindikira udindo wake. Koma akulu okhawa ndi amene anali ndi azeze oimbira ndiponso mbale za zofukiza.a Ndipo iwo okha ndi amene ankaimba nyimbo yatsopano. (Chivumbulutso 5:9) Choncho, iwo akufanana ndi a 144,000 amene ndi “Isiraeli [wopatulika] wa Mulungu,” amenenso ali ndi azeze oimbira ndipo akuimba nyimbo yatsopano. (Agalatiya 6:16; Akolose 1:12; Chivumbulutso 7:3-8; 14:1-4) Komanso, akulu 24 akuoneka m’masomphenyawa akukwaniritsa udindo wawo wokhala ansembe kumwamba, umene unkachitiridwa chithunzi ndi ansembe akale ku Isiraeli omwe ankapereka nsembe ya zofukiza kwa Yehova kuchihema. Nsembe zimenezi zinatha padziko lapansi pamene Mulungu anachotsa Chilamulo cha Mose pochikhoma pamtengo wozunzikirapo wa Yesu. (Akolose 2:14) Kodi tikupezapo mfundo yotani pa zonsezi? Tikupeza mfundo yakuti masomphenya amenewa akusonyeza Akhristu odzozedwa opambana pa nkhondo akuchita utumiki wawo monga ‘ansembe a Mulungu ndi a Khristu, ndipo akulamulira monga mafumu limodzi naye zaka 1,000.’—Chivumbulutso 20:6.
-
-
‘Ndani Ali Woyenera Kutsegula Mpukutu?’Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
Nyimbo Yatsopano
17. (a) Kodi akulu 24 ankaimba nyimbo yatsopano yotani? (b) Kodi kawirikawiri mawu akuti “nyimbo yatsopano” amagwiritsidwa ntchito bwanji m’Baibulo?
17 Tsopano kunamveka nyimbo yokoma. Nyimboyi ankaimbira Mwanawankhosa ndipo amene ankaimba ndi ansembe anzake, omwe ndi akulu 24 aja. “Iwo anali kuimba nyimbo yatsopano, yakuti: ‘Inu ndinu woyenera kutenga mpukutuwo ndi kumatula zidindo zake zomatira, chifukwa munaphedwa, ndipo ndi magazi anu, munagula anthu kuti atumikire Mulungu. Anthu ochokera mu fuko lililonse, chinenero chilichonse, mtundu uliwonse, ndi dziko lililonse.’” (Chivumbulutso 5:9) Mawu akuti “nyimbo yatsopano” amapezeka nthawi zingapo m’Baibulo ndipo kawirikawiri amatanthauza nyimbo yotamanda Yehova chifukwa cha mphamvu zimene wasonyeza populumutsa anthu. (Salimo 96:1; 98:1; 144:9) Choncho nyimboyo imakhala yatsopano chifukwa chakuti woimbayo ali ndi zifukwa zatsopano zotamandira Yehova poona ntchito zake zina zodabwitsa ndiponso chifukwa chakuti ali ndi zifukwa zina zotamandira dzina la Yehova laulemerero.
18. Kodi n’chifukwa chiyani akulu 24 aja ankatamanda Yesu ndi nyimbo yawo yatsopano?
18 Koma apa akulu 24 ankaimbira Yesu nyimbo yatsopano, osati Yehova. Komabe mfundo yake ndi yofanana. Iwo ankatamanda Yesu chifukwa cha zinthu zatsopano zimene iye, monga Mwana wa Mulungu, anawachitira. Kudzera m’magazi ake, iye anakhala mkhalapakati wa pangano latsopano, limene linathandiza kuti pakhale mtundu watsopano, umene ndi chuma chapadera cha Yehova. (Aroma 2:28, 29; 1 Akorinto 11:25; Aheberi 7:18-25) Anthu a mumtundu watsopano wauzimu umenewu anachokera m’mitundu yosiyanasiyana, koma Yesu anawagwirizanitsa kuti akhale mumpingo umodzi ngati mtundu umodzi.—Yesaya 26:2; 1 Petulo 2:9, 10.
19. (a) Kodi mtundu wa Isiraeli unalephera kulandira madalitso otani chifukwa cha kusakhulupirika kwake? (b) Kodi mtundu watsopano wa Yehova udzasangalala ndi madalitso otani?
19 Pamene Yehova ankathandiza Aisiraeli kuti akhale mtundu m’masiku a Mose, anachita nawo pangano ndipo anawalonjeza kuti ngati iwo angakhalebe okhulupirika ku panganolo, adzakhala ufumu wake wa ansembe. (Ekisodo 19:5, 6) Koma Aisiraeli anakhala osakhulupirika ndipo sanalandire madalitso amene Yehova anawalonjeza. Koma mtundu watsopano wakhalabe wokhulupirika. Mtunduwu unakhazikitsidwa chifukwa cha pangano latsopano limene mkhalapakati wake ndi Yesu. Choncho, anthu a mumtundu watsopanowu adzalamulira dziko lapansi monga mafumu ndiponso adzagwira ntchito ngati ansembe, pothandiza anthu olungama kuti agwirizanenso ndi Yehova. (Akolose 1:20) Zimenezi zikugwirizana ndi mawu a m’nyimbo yatsopanoyo, akuti: “Ndipo munawasandutsa mafumu ndi ansembe a Mulungu wathu, moti adzakhala mafumu olamulira dziko lapansi.” (Chivumbulutso 5:10) Akulu 24 amenewa amasangalala kwambiri akamaimba nyimbo yatsopano imeneyi, yotamanda Yesu amene ali mu ulemerero wake.
-