Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Miliri ya Yehova pa Matchalitchi Achikhristu
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
    • 29. Kodi “nyenyezi yaikulu yoyaka ngati nyale” ikuimira chiyani, ndipo n’chifukwa chiyani tikutero?

      29 M’mitu ya m’mbuyomu, taona kale zimene nyenyezi imaimira m’mauthenga a Yesu opita kumipingo 7. M’mauthenga amenewa, nyenyezi 7 zimaimira akulu a m’mipingo.b (Chivumbulutso 1:20) “Nyenyezi,” kapena kuti akulu odzozedwa pamodzi ndi Akhristu onse odzozedwa, mwauzimu amakhala m’malo awo a kumwamba kuyambira pa nthawi imene anadindidwa chidindo ndi mzimu woyera ngati chikole chotsimikizira kuti adzalandira cholowa chawo kumwamba. (Aefeso 2:6, 7) Komabe, mtumwi Paulo anachenjeza kuti pakati pa anthu okhala ngati nyenyezi amenewa padzatuluka anthu a mpatuko ndiponso oyambitsa magawano, amene adzasocheretsa nkhosa. (Machitidwe 20:29, 30) Akulu osakhulupirikawo adzachititsa kuti pakhale mpatuko waukulu, ndipo iwo adzakhala “munthu wosamvera malamulo,” yemwe adzadzikweze kuti afanane ndi Mulungu pakati pa anthu. (2 Atesalonika 2:3, 4) Zimene Paulo anachenjezazi zinayamba kuchitika pamene atsogoleri a Matchalitchi Achikhristu anayamba kuonekera. M’pake kuti gulu la atsogoleri limeneli likuimiridwa ndi “nyenyezi yaikulu yoyaka ngati nyale.”

  • Miliri ya Yehova pa Matchalitchi Achikhristu
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
    • b Ngakhale kuti nyenyezi 7 zimene zili m’dzanja lamanja la Yesu zikuimira oyang’anira odzozedwa a mumpingo wachikhristu, akulu ambiri m’mipingo yoposa 100,000 padziko lonse ali m’gulu la khamu lalikulu. (Chivumbulutso 1:16; 7:9) Kodi iwo ali ndi udindo wotani? Akuluwa amaikidwa ndi mzimu woyera kudzera mwa Akhristu odzozedwa, omwe ndi kapolo wokhulupirika ndi wanzeru. Motero, tinganene kuti akuluwa akutsogoleredwa ndi dzanja lamanja la Yesu chifukwa iwonso ndi abusa ake aang’ono. (Yesaya 61:5, 6; Machitidwe 20:28) Iwo amathandiza “nyenyezi 7” chifukwa amatumikira kumene kulibe abale odzozedwa oyenerera.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena