-
Kuteteza Dzina Lathu Monga AkristuNsanja ya Olonda—2005 | February 15
-
-
4. Kodi Yesu anatsindika motani kuti tikufunika kuteteza dzina lathu monga Akristu?
4 Komabe, monga atumiki odzipatulira kwa Yehova, tikudziwa kuti zingakhale zoopsa kwambiri ngati winawake, kaya wachinyamata kapena wachikulire, atachita zinthu zomwe zingaipitse dzina lake monga Mkristu. Munthu angadziwike ndi dzina labwino monga Mkristu, ngati akutsatira miyezo ya Yehova ndi kuchita zimene Iye amayembekezera kwa ife. Izitu n’zoyenera chifukwa tinalengedwa m’chifaniziro chake. (Genesis 1:26; Mika 6:8) Baibulo limayerekezera dzina lathu labwino monga Akristu, ndi chovala chimene timavala mwakuti aliyense angathe kuchiona. Pochenjeza za nthawi yathu ino, Yesu anati: “Taonani, ndidza ngati mbala. Wodala iye amene adikira, nasunga zovala zake, kuti angayende wausiwa, nangapenye anthu usiwa wake.”a (Chivumbulutso 16:15) Sitiyenera kuvula makhalidwe ndi miyezo yathu yachikristu n’kulola kutengera makhalidwe a dziko la Satanali. Ngati zoterezi zitatichitikira, ndiye kuti talephera kusunga “zovala” zimenezi. Izitu zingakhale zomvetsa chisoni ndi zochititsa manyazi.
-
-
Kuteteza Dzina Lathu Monga AkristuNsanja ya Olonda—2005 | February 15
-
-
a N’kutheka kuti mawu amenewa akunena zimene woyang’anira malo ozungulira kachisi ku Yerusalemu ankachita. M’kati mwa usiku, iye ankayendera kachisiyo kuti aone ngati alonda achilevi, amene ankalondera malo osiyanasiyana pakachisiyo ali m’maso kapena ngati akugona. Mlonda aliyense wopezeka akugona ankamumenya ndi ndodo, ndipo zovala zake ankatha kuzitentha. Ichi chinali chilango chochititsa manyazi.
-