-
Aneneri OnyengaKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Kapena munganene kuti: ‘Ndiri wotsimikizira kuti mudzavomereza kuti umboni weniweni uyenera kuchirikiza chinenezo chachikulu choterocho. Kodi minisitala wanu anatchula zitsanzo zenizeni zirizonse? (Ngati mwininyumba atchula “zonenedweratu” zina zimene sizinachitike, gwiritsirani ntchito mawu a patsamba 33, ndi pa tsamba 35 mpaka pamwamba pa 36.)’
Kuthekera kwina: ‘Ndiri wotsimikizira kuti ngati munthu wina anakuimbani mlandu wofananawo, mukanalola mwaŵi wooti mufotokoze ganizo lanu kapena lingaliro, kodi sichoncho? . . . Chotero kodi ndingakusonyezeni kuchokera m’Baibulo . . . ?’
-
-
ArmagedoKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Armagedo
Tanthauzo: Liwu Lachigiriki Har Ma·ge·donʹ, lotengedwa ku Chihebri ndi kutembenuzidwa kukhala “Armagedo” ndi otembenuza ambiri, limatathauza “Phiri la Megido,” kapena “Phiri la Msonkhano wa Magulu Ankhondo.” Baibulo limagwirizanitsa dzinali, osati ndi chipiyoyo cha nyukliya koma ndi “nkhondo ya tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuyonse” irinkudza ya chilengedwe chonse. (Chiv. 16:14, 16) Dzinali likugwiritsiridwa ntchito mwachindunji kusonya “malo [Chigiriki toʹpon; ndiko kuti, khalidwe kapena mkhalidwe]” amene olamulira andale zadziko a dziko lapansi akusonkhanitsidwirako motsutsana ndi Yehova ndi Ufumu wake wokhala mmanja mwa Yesu Kristu. Chitsutso chotero chidzasonyezedwa mwa chochitika cha dziko lonse chotsutsana ndi atumiki a Yehova padziko lapansi, oimira owoneka a Ufumu wa Mulungu.
Kodi anthu adzaloledwa ndi Mulungu kuwononga dziko lapansi ndi chimene ena amatcha “Armagedo yamoto wanyukliya”?
Sal. 96:10, NW: “Yehova iyemwiniyo wakhala mfumu. Dziko lobala zipatso [Chihebri, te·velʹ; dziko lapansi, monga lachonde ndi lokhalidwa ndi anthu, mbali yadziko lapansi yokhoza kukhalidwa ndi anthu] nalonso lafikira kukhala lokhazikitsidwa zolimba kotero kuti silingachititsidwe kugwedezeka.”
Sal. 37:29: “Olungama adzalandira dziko lapansi, nadzakhala momwemo kosatha.”
Chiv. 11:18, NW: “Mitundu inakwiya, ndipo mkwiyo wanu [wa Yehova] unafika, ndi nthaŵi yoikidwiratu . . . ya kuwononga awo owononga dziko lapansi.”
Kodi Armagedo nchiyani, monga momwe ikutchulidwira m’Baibulo?
Chiv. 16:14, 16, NW: “Iwo, kunena zowona, ali mawu ouziridwa ndi ziwanda ndipo amachita zizindikiro, ndipo iwo amapita kwa mafumu a dziko lonse lapansi lokhalidwa ndi anthu kuwasonkhanitsira pamodzi ku nkhondo ya tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuyonse. Ndipo anawasonkhanitsira pamodzi ku malo amene akutchedwa m’Chihebri Har–Magedo [Armagedo].”
Kodi Armagedo idzamenyedwera ku Middle East kokha?
Olamulira ndi magulu ankhondo amitundu yonse adzasonkhanitsidwa kumenyana ndi Mulungu
Chiv. 16:14, NW: “Amapita kwa mafumu a dziko lonse lapansi lokhalidwa ndi anthu, kuwasonkhanitsira pamodzi ku nkhondo ya tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuyonse.”
Chiv. 19:19, NW: “Ndinawona chirombo [ulamuliro wandale zadziko waumunthu] ndi mafumu a dziko lapansi ndi magulu awo ankhondo atasonkhana kuchita nkhondo ndi wokwera pakavalo limodzi ndi gulu lake lankhondo.”
Yer. 25:33: “Akuphedwa a Yehova adzakhala tsiku lomwelo kuchokera kumalekezero ena a dziko lapansi kumka kumalekezero a dziko lapansi.”
Kugwiritsiridwa ntchito kwa dzina lakuti Armagedo (Har–Magedo) sikungatathauze kuti nkhondoyo idzamenyedwera ku Phiri lenileni la Megido
Kulibe Phiri lenileni la Megido; kuli kokha mulu wa pafupifupi mapazi 70 (21 m) kumene mabwinja a Megido wakale akupezeka.
Mafumu ndi magulu ankhondo a “dziko lonse lapansi lokhalidwa ndi anthu” sakakwana m’Chigwa chenichenicho cha Esdraelon, mtsinde mwa Megido. Chigwacho nchangondya zitatu, chamamailo 20 okha (32 km) m’litali ndi mamailo 18 (29 km) m’bwambi kumalekezero akummaŵa.—The Geography of the Bible (New York, 1957), Denis Baly, p. 148.
Dzinalo nloyenerera chifukwa cha mbali ya Megido m’mbiri; chigwa chokhala mtsinde mwa Megidocho chinali malo ankhondo zotha makani
Kumeneko Yehova anachititsa kugonjetsedwa kwa Sisera, kazembe wankhondo wa gulu la nkhondo la Akanani, pamaso pa Woweruza Baraki.—Ower. 5:19, 20; 4:12-24.
Thutmose III, farao wa Igupto, anati: “Kulandidwa kwa Megido ndiko kulandidwa kwa matauni chikwi!”—Ancient Near Eastern Texts Relating to the Old Testament (Princeton, N.J.; 1969), lolembedwa ndi James Pritchard, p. 237.
Dzina lakuti Megido (kutanthauza “Msonkhano wa Magulu Ankhondo”) nloyenerera chifukwa chakuti Armagedo uli mkhalidwe wa padziko lonse mu umene magulu ankhondo ndi ochirikiza ena a olamulira amitundu yonse adzaloŵetsedwamo.
Kodi ndani kapena nchiyani chimene chidzawonongedwa pa Armagedo?
Dan. 2:44, NW: “Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu . . . Udzaphwanya ndi kutha maufumu onse amenewa, ndipo uwo wokha udzakhala kosatha.”
Chiv. 19:17, 18, NW: “Ndinawonanso mngelo ataima m’dzuŵa, ndipo anafuula ndi mawu aakulu ndi kunena kwa mbalame zonse zimene zimauluka m’mlengalenga: ‘Idzani kuno, sonkhanani ku chakudya chamadzulo chachikulu cha Mulungu, kuti mudzadye minofu ya mafumu ndi minofu ya atsogoleri ankhondo ndi minofu ya anthu amphamvu ndi minofu ya akavalo ndi ya owakwera, ndi minofu ya onse, ya mfulu kudzanso ya akapolo ndi ya aang’ono ndi akulu.’”
1 Yoh. 2:16, 17, NW: “Chirichonse m’dziko—chikhumbo chathupi ndi chikhumbo chamaso ndi kuwonetsera chuma chomwe uli nacho—sizimachokera kwa Atate, koma zimachokera ku dziko. Ndiponso, dziko likupita ndipo chomwechonso chikhumbo chake, koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kosatha.”
Chiv. 21:8: “Koma amantha, ndi osakhulupirira, ndi onyansa, ndi ambanda, ndi achigololo, ndi olambira mafano, ndi onse amabodza, cholandira chawo chidzakhala m’nyanja yotentha ndi moto ndi sulfure; ndiyo imfa yachiŵiri.”
-