Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • fy mutu 15 tsamba 173-182
  • Kulemekeza Makolo Athu Okalamba

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulemekeza Makolo Athu Okalamba
  • Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • KUZINDIKIRA ZOKHUMBA MTIMA WAWO
  • KUTHANDIZA NDI ZOSOŴA ZAKUTHUPI
  • CHIKONDI NDI KUDZIMANA
  • KHALANI WACHIFUNDO NDI WOMVETSETSA
  • KHALANI NDI MAGANIZO ABWINO
  • OSAMALIRA NAWONSO AMAFUNA KUSAMALIRIDWA
  • NYONGA YOPOSA YACHIBADWA
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani Yosamalira Makolo Achikulire?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Achikulire Tingawasamalire Bwanji?
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Kusamalira Okalamba—Vuto Lomakulakulabe
    Galamukani!—1991
  • Muzilemekeza Anthu Achikulire
    Nsanja ya Olonda—2014
Onani Zambiri
Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
fy mutu 15 tsamba 173-182

Mutu 15

Kulemekeza Makolo Athu Okalamba

1. Kodi tili ndi mangawa otani kwa makolo athu, motero tiyenera kuwaona motani ndi kuwachitira motani?

“TAMVERA atate wako anakubala, usapeputse amako atakalamba,” anatero mwamuna wanzeru wakale. (Miyambo 23:22) ‘Sindingayese kuchita zimenezo!’ inuyo mungatero. M’malo mwa kupeputsa amayi athu—kapena atate athu—ambirife timawakonda kwambiri. Timadziŵa kuti tili ndi mangawa aakulu kwa iwo. Choyamba, makolo athu anatipatsa moyo. Pamene kuli kwakuti Yehova ndiye Kasupe wa moyo, popanda makolo athu sitikanakhalapo. Palibe chinthu chimene tingapatse makolo athu cha mtengo wapatali wofanana ndi moyo. Pamenepo, tangolingalirani za kudzimana, nkhaŵa ya kusamalira, ndalama zotayidwa, ndi chisamaliro chachikondi chimene kukulitsa mwana kumafuna. Chotero, nkoyenera chotani nanga, pamene Mawu a Mulungu amatilangiza kuti: “Lemekeza atate wako ndi amako . . . kuti kukhale bwino ndi iwe, ndi kuti ukhale wa nthaŵi yaikulu padziko”!—Aefeso 6:2, 3.

KUZINDIKIRA ZOKHUMBA MTIMA WAWO

2. Kodi ana aakulu ‘angabwezere’ motani makolo awo?

2 Mtumwi Paulo analembera Akristu kuti: “Ana kapena adzukulu, ayambe aphunzire iwo kuchitira ulemu a m’banja lawo, ndi kubwezera akuwabala [ndi agogo awo, NW]; pakuti ichi ncholandirika pamaso pa Mulungu.” (1 Timoteo 5:4) Ana aakulu ‘amabwezera’ mwa kusonyeza chiyamikiro kaamba ka zaka zambiri za chikondi chawo, ntchito, ndi chisamaliro zimene makolo awo ndi agogo awo anapereka pa iwo. Njira imodzi imene ana angachitire zimenezi ndiyo mwa kuzindikira kuti mofanana ndi munthu wina aliyense, okalamba amafuna kukondedwa ndi kulimbikitsidwa—kaŵirikaŵiri amazilakalaka kwambiri zimenezo. Mofanana ndi tonsefe, iwo amafuna kuona kuti akuŵerengeredwa. Amafuna kuona kuti moyo wawo uli wofunika.

3. Kodi tingalemekeze motani makolo ndi agogo athu?

3 Motero, tingalemekeze makolo athu ndi agogo athu mwa kuwachititsa kudziŵa kuti timawakonda. (1 Akorinto 16:14) Ngati makolo athu sakukhala nafe, tiyenera kukumbukira kuti pamene iwo alandira mawu kuchokera kwa ife, amalimbikitsidwa kwambiri. Kalata yabwino, foni, kapena kuwachezera zingawapatse chimwemwe chachikulu. Miyo, amene akukhala ku Japan, pamene anali ndi zaka 82 zakubadwa analemba kuti: “Mwana wanga wamkazi [amene mwamuna wake ndi mtumiki woyendayenda] amandiuza kuti: ‘Mayi, chonde “yendani” nafe paulendo.’ Amanditumizira ndandanda ya kucheza kwawo ndi nambala ya foni mlungu uliwonse. Ndimatsegula mapu anga ndi kunena kuti: ‘Eya. Tsopano ali apa!’ Ndimayamikira Yehova nthaŵi zonse pondidalitsa ndi mwana wotere.”

KUTHANDIZA NDI ZOSOŴA ZAKUTHUPI

4. Kodi mwambo wachipembedzo chachiyuda unaphunzitsa motani anthu kuumira mtima makolo awo okalamba?

4 Kodi kulemekeza makolo kungaphatikizeponso kusamalira zosoŵa zawo zakuthupi? Inde. Kaŵirikaŵiri kumatero. M’tsiku la Yesu atsogoleri achipembedzo achiyuda anali ndi mwambo wakuti ngati munthu walengeza kuti ndalama zake kapena katundu wake anali “choperekedwa kwa Mulungu,” iye anali womasuka pa thayo la kuchigwiritsira ntchito kusamalira makolo ake. (Mateyu 15:3-6) Nkuuma mtima kotani nanga! Kwenikweni, atsogoleri achipembedzo amenewo anali kulimbikitsa anthu kusalemekeza makolo awo koma kuwapeputsa mwa kuwamana zosoŵa zawo mwadyera. Sitikufuna konse kuchita zimenezo!—Deuteronomo 27:16.

5. Mosasamala kanthu za thandizo loperekedwa ndi boma m’maiko ena, kodi nchifukwa ninji kulemekeza makolo nthaŵi zina kumaphatikizapo thandizo la ndalama?

5 M’maiko ambiri lerolino, maprogramu ochirikizidwa ndi boma amapereka thandizo la zinthu zina zakuthupi kwa okalamba, monga chakudya, zovala, ndi nyumba. Kuwonjezera pa zimenezo, okalamba angakhale atasungiratu chuma chowathandiza paukalamba wawo. Koma ngati chumacho chitha kapena ngati chichepa, ana amalemekeza makolo awo mwa kuchita zimene angathe kuti apezere makolo zosoŵa zawo. Kwenikweni, kusamalira makolo okalamba kuli umboni wa kudzipereka kwaumulungu, ndiko kuti, kudzipereka kwa munthu kwa Yehova Mulungu, Woyambitsa kakonzedwe ka banja.

CHIKONDI NDI KUDZIMANA

6. Kodi ena apanga makonzedwe otani a kakhalidwe kotero kuti asamalire zosoŵa za makolo awo?

6 Ana aakulu ambiri athandiza pa zosoŵa za makolo awo okalamba mwa chikondi ndi kudzimana. Ena atenga makolo awo ndi kukhala nawo panyumba pawo kapena kusamuka kukakhala pafupi nawo. Ena asamuka kukakhala pamodzi ndi makolo awo. Kaŵirikaŵiri, makonzedwe oterowo akhala dalitso kwa makolo ndi ana omwe.

7. Kodi nchifukwa ninji kuli kofunika kusachita mofulumira popanga zosankha zokhudza makolo okalamba?

7 Komabe, nthaŵi zina zimenezo sizimayenda bwino. Chifukwa ninji? Mwinamwake chifukwa chakuti zosankha zapangidwa mofulumira kapena zangosonkhezeredwa ndi kukhudzidwa mtima. “Wochenjera asamalira mayendedwe ake,” limachenjeza mwanzeru Baibulo. (Miyambo 14:15) Mwachitsanzo, tinene kuti amayi anu okalamba akupeza vuto kukhala okha ndipo muganiza kuti kungakhale kothandiza kudzakhala nawo. Posamalira mayendedwe anu mochenjera, mungapende mfundo izi: Kodi zosoŵa zawo zenizeni nzotani? Kodi pali makonzedwe alionse a anthu kapena aboma amene angakhale njira ina yoperekera chithandizo? Kodi iwo akufuna kusamuka? Ngati akutero, kodi moyo wawo udzakhudzidwa motani? Kodi adzasiya mabwenzi? Kodi zimenezi zidzakhudza motani maganizo awo? Kodi mwakambitsirana nawo zinthu zimenezi? Kodi kuchita zimenezo kungayambukire motani inuyo, mnzanu wa muukwati, kapena ana anu? Ngati amayi anu amafunikira chisamaliro, kodi adzachipereka ndani? Kodi mungagaŵane thayo limenelo? Kodi mwakambitsirana nkhaniyo mwachindunji ndi ena oloŵetsedwamo?

8. Kodi mungafunsire kwa yani pamene mufuna kudziŵa mmene mungathandizire makolo anu okalamba?

8 Popeza kuti thayo la kusamalira makolo lili pa ana onse m’banja, kungakhale kwanzeru kukhala ndi msonkhano wa banja kotero kuti onse akhale ndi mbali pakupanga zosankha. Kukambitsirana ndi akulu mumpingo wachikristu kapena ndi mabwenzi amene anakumanapo ndi vuto limenelo kungakhalenso kothandiza. “Zolingalira zizimidwa popanda upo,” limachenjeza motero Baibulo, “koma pochuluka aphungu zikhazikika.”—Miyambo 15:22.

KHALANI WACHIFUNDO NDI WOMVETSETSA

Chithunzi patsamba 179

Si bwino kupangira kholo chosankha popanda kulankhula nalo choyamba

9, 10. (a) Mosasamala kanthu za ukalamba wawo, kodi tiyenera kukumbukiranji za iwo? (b) Mosasamala kanthu za zimene mwana angachitire makolo ake, kodi ayenera kuwapatsanji nthaŵi zonse?

9 Kulemekeza makolo athu okalamba kumafuna chifundo ndi kuwamvetsetsa. Pamene achikulire afika m’zaka zaukalamba weniweni, angayambe kupeza vuto kwambiri pakuyenda, kudya, ndi kukumbukira zinthu. Angafunikire chithandizo. Kaŵirikaŵiri, ana amafuna kuwatetezera ndipo amayesa kupereka chithandizo. Koma okalambawo ali achikulire okhala ndi nzeru za zaka zambiri ndi chidziŵitso, adzisamalira okha kwa zaka zonsezo ndipo akhala akupanga zosankha zawo. Iwo akhala odziŵika ndipo apeza ulemu chifukwa cha ukholo wawo ndi uchikulire wawo. Makolo amene aona kuti tsopano thayo la kusamalira moyo wawo likutengedwa ndi ana awo angapsinjike maganizo ndi kukhala okwiya. Ena amaipidwa ndi kukana zoyesayesa zimene angaone kuti zikuwalanda ufulu wawo.

10 Palibe njira zofeŵa zothetsera mavuto oterowo, koma kumakhala kukoma mtima ngati tilola makolo okalamba kudzisamalira okha ndi kupanga zosankha zawo zimene angakhoze. Kuli kwanzeru kusasankhira zinthu makolo anu popanda kulankhula nawo choyamba. Ukalamba wawalanda zambiri. Athandizeni kusunga zimene akali nazo. Mungapeze kuti pamene simukulamulira kwambiri moyo wa makolo anu, mpamenenso unansi wanu umakhala bwino kwambiri. Adzakhala achimwemwe mokulirapo, inunso mudzatero. Ngakhale ngati kuli kofunika kuumirira pa zinthu zina kaamba ka ubwino wawo, kulemekeza makolo anu kumafuna kuti muwaope ndi kuwapatsa ulemu wowayenera. Mawu a Mulungu amalangiza kuti: “Pali aimvi uziwagwadira, nuchitire ulemu munthu wokalamba.”—Levitiko 19:32.

KHALANI NDI MAGANIZO ABWINO

11-13. Ngati unansi wa mwana wachikulire ndi makolo ake sunali bwino kumbuyoku, kodi mwanayo angachitebe motani ntchito yowasamalira m’zaka zawo zaukalamba?

11 Nthaŵi zina vuto limene ana aakulu amakumana nalo pakulemekeza makolo awo okalamba limaphatikizapo unansi umene anali nawo ndi makolo awo nthaŵi zakumbuyo. Mwinamwake atate anu analibe chifundo ndi chikondi, amayi anu mwina anali olamulira ndi aukali. Mwina mukali wokhumudwa, wokwiya, kapena wopwetekedwa mtima chifukwa sanakhale makolo amene munafuna kuti akhale. Kodi mungagonjetse maganizo otero?a

12 Basse, amene anakulira ku Finland, akusimba kuti: “Atate anga opeza anali aofesala a SS m’Germany wa Nazi. Iwo anali kutaya mtima mwamsanga, ndipo anali owopsa. Anali kumenya amayi nthaŵi zambiri pamaso panga. Tsiku lina pamene anakwiya nane, anandikwapula ndi lamba lawo ndipo chitsulo chake chinandikantha kunkhope. Chinandikantha kwambiri kwakuti ndinagwera pa mbedi.”

13 Komabe, analinso ndi mkhalidwe wina. Basse akuwonjezera kuti: “Ngakhale ndi choncho, iwo anagwira ntchito zolimba ndipo sanaleke kusamalira zofunika za banja. Sanandisonyeze chikondi cha tate, koma ndinadziŵa kuti anali osweka mtima. Amayi awo anawapitikitsa panyumba pamene anali mnyamata wamng’ono. Kukula kwawo kunali komenyana ndi anthu nthaŵi zonse, ndipo anapita kunkhondo akali achichepere. Pamlingo wina wake ndinadziŵa chifukwa chake ndipo sindinawapatse mlandu. Pamene ndinakula, ndinafuna kuwathandiza kwambiri kufikira imfa yawo. Zinali zovuta, koma ndinachita zimene ndinakhoza. Ndinayesa kukhala mwana wabwino kufikira imfa yawo, ndipo ndikhulupirira kuti anakhutira kuti ndinali wotero.”

14. Kodi ndi lemba liti limene limagwira ntchito m’mikhalidwe yonse, kuphatikizapo imene imabuka posamalira makolo okalamba?

14 M’mikhalidwe ya banja, mofanana ndi m’nkhani zina, uphungu wa Baibulo umagwira ntchito: “Valani, . . . mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, kuleza mtima; kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali nacho chifukwa pa mnzake; monganso [Yehova, NW] anakhululukira inu, teroni inunso.”—Akolose 3:12, 13.

OSAMALIRA NAWONSO AMAFUNA KUSAMALIRIDWA

15. Kodi nchifukwa ninji kusamalira makolo nthaŵi zina kumakhala kosautsa maganizo?

15 Kusamalira kholo lokalamba ndi ntchito yaikulu, yoloŵetsamo zochita zambiri, thayo lalikulu, ndi maola ochuluka. Koma mbali yovuta kwambiri ndiyo yokhudza maganizo. Kumavutitsa maganizo kuona makolo anu akutaya thanzi lawo, kuiŵala, ndi kulephera kudziimira paokha. Sandy, wa ku Puerto Rico, akusimba kuti: “Amayi anga ndiwo anali nkhaŵa yaikulu pabanja. Kunali kopweteka kwambiri kumawasamalira. Anayamba ndi kutsimphina, kenako anafunikira ndodo, walker [chothandiza kuyenda] ndiyeno mpando wa magudumu. Pambuyo pake, matenda anakulirakulira kufikira anamwalira. Anadwala kansa ya m’mafupa ndipo anafunikira chisamaliro cha nthaŵi zonse—usana ndi usiku. Tinawasambitsa ndi kuwadyetsa ndi kuwaŵerengera. Zinali zovuta kwambiri—makamaka m’maganizo. Pamene ndinaona kuti amayi anali kumwalira, ndinalira chifukwa ndinawakonda kwambiri.”

16, 17. Kodi ndi uphungu wotani umene ungathandize wopereka chisamaliro kukhala ndi kaonedwe kabwino ka zinthu?

16 Ngati mukhala mumkhalidwe umodzimodziwo, kodi mungachitenji kuti mulimbane nazo? Kumvetsera Yehova mwa kuŵerenga Baibulo ndi kulankhula naye m’pemphero kungakuthandizeni kwambiri. (Afilipi 4:6, 7) Mwa njira yothandiza, yesani kudya zakudya zopatsa thanzi ndi kupeza tulo tokwanira. Mwa kuchita zimenezi, mudzakhala mumkhalidwe wabwino, ponse paŵiri m’maganizo ndi kuthupi, kuti musamalire wokondedwa wanu. Mwinamwake mungapange makonzedwe a kupumulako pa umoyo wa masiku onse. Ngakhale ngati kutenga tchuthi nkosatheka, kumakhalabe kwanzeru kupatula nthaŵi ya kupumula. Kuti mupezeko nthaŵi, mungamvane ndi wina kuti akhaleko ndi kholo lanu lodwalalo.

17 Sikwachilendo kwa opereka chisamaliro achikulire kuona monga zimene akuchita sizokwanira. Koma musadzimve waliwongo posachita zimene simungathe. M’mikhalidwe ina mungafunikire kupereka wokondedwa wanuyo kunyumba yosamalira okalamba. Ngati ndinu wopereka chisamaliro, ikani zonulirapo zotheka. Muyenera kulingalira bwino zofunika, osati za makolo anu zokha, komanso za ana anu, za mnzanu wa muukwati, ndi zanu.

NYONGA YOPOSA YACHIBADWA

18, 19. Kodi Yehova wapereka lonjezo lotani la chichirikizo, ndipo nchochitika chiti chimene chimasonyeza kuti amasunga lonjezo limeneli?

18 Kupyolera m’Mawu ake Baibulo, Yehova wapereka mwachikondi chitsogozo chimene chingathandize kwambiri munthu wosamalira makolo okalamba, koma chimenecho sindicho chithandizo chokha chimene amapereka. “Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa iye,” analemba motero wamasalmo mwa kuuziridwa. “Nadzamva kufuula kwawo, nadzawapulumutsa.” Yehova adzapulumutsa, kapena kulanditsa, okhulupirika ake ngakhale m’mikhalidwe yovuta kwenikweni.—Salmo 145:18, 19.

19 Myrna, ku Philippines, anadziŵa zimenezi pamene anali kusamalira amake, amene anapuŵala ndi stroko. “Palibe chinthu chovutitsa maganizo kwambiri monga kuona wokondedwa wako akuvutika, wosakhoza kukuuzani chimene chikupweteka,” analemba motero Myrna. “Zinali monga kuwaona akumira pang’onopang’ono, popanda zimene ndikanachita. Nthaŵi zambiri ndinkagwada ndi kupemphera kwa Yehova ponena za kutopa nazo kwanga. Ndinalira monga Davide, amene anachonderera Yehova kuti asunge misozi yake m’nsupa ndi kumkumbukira. [Salmo 56:8] Ndipo monga momwe Yehova analonjezera, anandipatsa nyonga imene ndinafunikira. ‘Yehova anali mchirikizo wanga.’”—Salmo 18:18.

20. Kodi ndi malonjezo a Baibulo otani amene amathandiza awo opereka chisamaliro kukhala achidaliro, ngakhale ngati uyo amene akumsamalira amwalira?

20 Ena amati kusamalira makolo okalamba kuli monga “nkhani ya mapeto achisoni.” Mosasamala kanthu za kuyesayesa kuwasamalira mwakhama, okalamba amamwalirabe, monga momwe anachitira amake Myrna. Koma awo okhulupirira Yehova amadziŵa kuti imfa sindiyo mapeto a nkhani. Mtumwi Paulo ananena kuti: “Ndikukhala nacho chiyembekezo cha kwa Mulungu . . . kuti kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama.” (Machitidwe 24:15) Awo amene ataya makolo awo okalamba mu imfa amapeza chitonthozo m’chiyembekezo cha chiukiriro limodzi ndi lonjezo la dziko latsopano losangalatsa lopangidwa ndi Mulungu mmene ‘simudzakhalanso imfa.’—Chivumbulutso 21:4.

21. Kodi kulemekeza okalamba kumakhala ndi zotulukapo zabwino zotani?

21 Atumiki a Mulungu amalemekeza kwambiri makolo awo, ngakhale kuti iwoŵa angakhale atakalamba. (Miyambo 23:22-24) Amawapatsa ulemu. Mwa kutero, amaona zimene mwambi wouziridwa umanena kuti: “Atate wako ndi amako akondwere, amako wakukubala asekere.” (Miyambo 23:25) Ndipo choposa zonse, awo amene amalemekeza makolo awo okalamba amakodweretsa ndi kulemekezanso Yehova Mulungu.

a Pano sitikunena za makolo amene anachitira nkhanza ana awo zimene zinachititsa anawo kutaya chidaliro chawo mwa iwo, zimene zingaonedwe kukhala mlandu.

KODI MAPULINSIPULO A BAIBULO AŴA ANGATITHANDIZE MOTANI . . . KULEMEKEZA MAKOLO ATHU OKALAMBA?

Tiyenera kubwezera makolo ndi agogo athu.—1 Timoteo 5:4.

Zinthu zathu zonse ziyenera kuchitika mwa chikondi.—1 Akorinto 16:14.

Zosankha zazikulu siziyenera kupangidwa mofulumira.—Miyambo 14:15.

Ngakhale ngati makolo okalamba angakhale odwalira ndi ofooka, ayenera kulemekezedwa.—Levitiko 19:32.

Chiyembekezo cha kukalamba ndi kumwalira sitidzakhala nacho kwamuyaya.—Chivumbulutso 21:4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena