Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/08 tsamba 1
  • Akonzekeretseni Atsopano Kupirira Chitsutso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Akonzekeretseni Atsopano Kupirira Chitsutso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Pitirizanibe Kukhala M’gulu la Yehova
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • “Mulole Kuti Kupirira Kumalize Kugwira Ntchito Yake”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • N’zotheka Kupirira Ena Akamakuzunzani
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Chipiriro—Nchofunika kwa Akristu
    Nsanja ya Olonda—1993
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
km 11/08 tsamba 1

Akonzekeretseni Atsopano Kupirira Chitsutso

1 Anthu akayamba kuphunzira Baibulo ndi ‘kufuna kukhala ndi moyo wodzipereka kwa Mulungu,’ Satana amawalondalonda kuti aziwatsutsa. (2 Tim. 3:12) Iwo angatsutsidwe ndi anzawo akuntchito, akusukulu, kapena anthu oyandikana nawo. Nthawi zambiri zimakhala zovuta ngati amene akutsutsa atsopanowo ndi achibale awo, amene pochita zimenezo, amaona ngati akufuna kuwathandiza.—Mat. 10:21; Maliko 3:21.

2 Ananeneratu Kuti Tidzatsutsidwa: Atsopano ayenera kudziwa kuti adzazunzidwa, ndipo zimenezi zimasonyeza kuti iwo tsopano ndi ophunzira enieni a Khristu. (Yoh. 15:20) Nthawi zina, anthu angawatsutse chifukwa cha maganizo olakwika amene anthuwo amakhala nawo ponena za Mboni za Yehova. Musaiwale kuti munthu akamachitiridwa chipongwe chifukwa chokhala wotsatira Yesu ndiponso kumvera Mulungu, amakhala wosangalala kwambiri. (Mac. 5:27-29, 40, 41) Atsimikizireni atsopanowo kuti, Yehova amawakonda ndipo adzawathandiza. (Sal. 27:10; Maliko 10:29, 30) Choncho, ngati iwo apitirizabe kusunga umphumphu wawo, amakhala kumbali ya Yehova pankhani ya ulamuliro wa m’chilengedwe chonse.—Miy. 27:11.

3 Ubwino Wodziwa Zinthu Molondola: Athandizeni ophunzira Baibulo kuona kuti afunika kusasiya kuphunzira kuti adziwe zinthu molondola, ngakhale angakumane ndi mavuto otani. Satana amagwiritsa ntchito chitsutso pofuna kuletsa zimene iwo akuphunzira kuti zisazike mizu m’mitima yawo yophiphiritsa. (Miy. 4:23; Luka 8:13) Afunika kusasiya kuphunzira kuti adziwe molondola Mawu a Mulungu, chifukwa zimenezi zidzawathandiza kukhala okhazikika m’chikhulupiriro.—Sal. 1:2, 3; Akol. 2:6, 7.

4 Kupirira N’kofunika: Panthawi ya mavuto, kupirira n’kofunika kwambiri ndipo kungabale zipatso zabwino. (Luka 21:16-19) Atsopano akamapirira chitsutso, amapindula ndiponso amapindulitsa ena. Iwo amaona mphamvu ya Yehova polandira madalitso ochuluka amene iye amapereka kwa anthu omwe amapirira mokhulupirika.—Yak. 1:12.

5 Mtumwi Paulo anasangalala kwambiri ataona mmene abale a ku Tesalonika anapitira patsogolo mwauzimu. Anathokoza Mulungu chifukwa cha iwo, popeza iyeyo anali atathandiza ambiri a iwo kuphunzira choonadi. (2 Ates. 1:3-5) Ifenso, tingasangalale ngati tikonzekeretsa ophunzira Baibulo kuti azipirira chitsutso.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena