Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • bt mutu 19 tsamba 148-155
  • ‘Pitiriza Kulankhula, Usakhale Chete’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Pitiriza Kulankhula, Usakhale Chete’
  • ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • “Anali Opanga Matenti” (Machitidwe 18:1-4)
  • “Anthu Ambiri a ku Korinto . . . Anayamba Kukhulupirira” (Machitidwe 18:5-8)
  • “Ndili ndi Anthu Ambiri Mumzindawu” (Machitidwe 18:9-17)
  • “Yehova Akalola” (Machitidwe 18:18-22)
  • Akula ndi Priskila—Banja Lopereka Chitsanzo Chabwino
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Mawu a Yehova Afalikira!
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • “Ndilibe Mlandu wa Magazi a Anthu Onse”
    ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Machitidwe
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
bt mutu 19 tsamba 148-155

MUTU 19

‘Pitiriza Kulankhula, Usakhale Chete’

Paulo ankapeza yekha zinthu zofunika pa moyo wake, komabe ankaika utumiki wake patsogolo

Nkhaniyi yachokera pa Machitidwe 18:1-22

1-3. N’chifukwa chiyani mtumwi Paulo anapita ku Korinto, nanga ndi zinthu ziti zimene ziyenera kuti zinkamudetsa nkhawa?

CHAKUMAPETO kwa chaka cha 50 C.E., mtumwi Paulo anali ku Korinto, kuchimake kwa malonda ndipo kunkapezeka Agiriki, Aroma komanso Ayuda ambiri.a Paulo sanapite ku Korinto kukachita malonda kapena kukafuna ntchito. Iye anapita kumeneko kukagwira ntchito yofunika kwambiri yochitira umboni za Ufumu wa Mulungu. Paulo ankafunikira malo okhala, koma anatsimikiza ndi mtima wonse kuti asalemetse anthu ena. Iye sanafune kuti anthu ena aziona kuti ndi wofunika kumuthandiza chifukwa cha utumiki umene ankachita. Kodi pamenepa iye anatani?

2 Paulo ankadziwa kupanga matenti. Ngakhale kuti kupanga matenti ndi ntchito yovuta, iye anali wofunitsitsa kugwira ntchitoyo kuti azipeza zinthu zofunika pa moyo wake. Kodi Paulo akanapeza ntchito mumzinda umenewu? Kodi akanapeza malo abwino okhala? Ngakhale kuti iye anafunika kupeza zinthu zimenezi, sananyalanyaze utumiki wake womwe unali ntchito yofunika kwambiri.

3 Zikuoneka kuti Paulo anakhala ku Korinto kwa kanthawi ndipo utumiki wake kumeneko unkayenda bwino kwambiri. Kodi tingaphunzire chiyani pa zimene Paulo anachita ku Korinto, zimene zingatithandize kuchitira umboni mokwanira za Ufumu wa Mulungu m’gawo lathu?

MZINDA WA KORINTO UNALI PAKATI PA NYANJA ZIWIRI

Mzinda wakale wa Korinto unali m’dera lina limene linali pakati pa dziko la Girisi ndi chilumba cha Peloponnese chimene chinali kum’mwera kwa Girisi. Malo oning’a kwambiri a derali anali osakwana makilomita 6, ndipo zimenezi zinachititsa kuti mzinda wa Korinto ukhale ndi madoko awiri. Pagombe la Korinto panali doko la Lekiyamu, pamene pankafikira ngalawa zopita ku Italy, ku Sisile ndi ku Spain. Pagombe la Saroniki, pankafikira ngalawa zopita komanso zochokera ku dera la Aegean, ku Asia Minor, ku Siriya ndi ku Iguputo.

Mphepo yamphamvu inkawomba pamagombe akum’mwera kwenikweni kwa chilumba cha Peloponnese ndipo zinali zoopsa kuti ngalawa zifike kumeneko. Choncho anthu oyenda pangalawa ankakonda kuima pa limodzi mwa madoko awiri a ku Korinto, ndipo katundu wawo ankadutsa pamtunda kenako n’kukafikanso padoko lina kumene ankamukwezanso m’ngalawa. Ngalawa zing’onozing’ono zinkakokedwa kudutsa pamtunda umene unali pakati pa nyanja ziwirizo. Choncho mzinda wa Korinto unali chimake cha malonda ndipo anthu ochita malondawo ankabwera mumzindawo kudzera panyanja komanso pamtunda. Malondawa anachititsa kuti mzindawu ukhale wolemera komanso munkachitika zinthu zambiri zoipa chifukwa chakuti munkabwera anthu osiyanasiyana.

M’nthawi ya mtumwi Paulo, mzinda wa Korinto unali likulu la dera la Akaya limene linkalamulidwa ndi Aroma ndipo kunali maofesi aboma ofunika kwambiri. Panali umboni woti mumzindawu munali zipembedzo zambiri chifukwa munali kachisi wa mfumu ya milungu yonse, akachisi a milungu yambirimbiri ya Agiriki ndiponso Aiguputo, komanso sunagoge wa Ayuda.​—Mac. 18:4.

Zaka ziwiri zilizonse, pachilumba china chapafupi ndi Korinto pankachitika mpikisano wa masewera osiyanasiyana umene unali wofunika kwambiri ndipo unkaposedwa ndi masewera a Olimpiki okha. Mtumwi Paulo ayenera kuti anali ku Korinto pamene masewerawo ankachitika mu 51 C.E. Choncho, buku lina limati: “N’zosadabwitsa kuti Paulo anagwiritsa ntchito kwa nthawi yoyamba chitsanzo cha mpikisano wothamanga m’kalata yake yopita ku Korinto.”​—1 Akor. 9:24-27.

“Anali Opanga Matenti” (Machitidwe 18:1-4)

4, 5. (a) Kodi Paulo ali ku Korinto ankakhala kuti, nanga ankagwira ntchito yanji? (b) Kodi Paulo ayenera kuti anaphunzira bwanji ntchito yopanga matenti?

4 Patapita kanthawi kuchokera pamene Paulo anafika ku Korinto, anakumana ndi banja lina la Chiyuda lodziwa kuchereza alendo la Akula ndi mkazi wake Purisila, kapena kuti Purisika. Banjali linasamukira ku Korinto chifukwa Mfumu Kalaudiyo inalamula “Ayuda onse kuti achoke ku Roma.” (Mac. 18:1, 2) Akula ndi Purisila analandira Paulo kuti azikhala naye kunyumba kwawo komanso kuti azigwira naye ntchito limodzi. Timawerenga kuti: “Popeza ntchito yawo inali imodzi, [Paulo] anakhala kunyumba kwawoko. Iwo ankagwirira ntchito limodzi, chifukwa onse anali opanga matenti.” (Mac. 18:3) Paulo anakhalabe kunyumba kwa anthu achifundo ndi odziwa kulandira alendo amenewa, pa nthawi yonse imene ankachita utumiki wake ku Korinto. Pamene Paulo ankakhala ndi Akula ndi Purisila, ayenera kuti analemba ena mwa makalata amene kenako anadzakhala mabuku a m’Baibulo.b

5 Kodi zinatheka bwanji kuti Paulo, munthu amene ‘anaphunzitsidwa ndi Gamaliyeli,’ akhalenso wodziwa ntchito yopanga matenti? (Mac. 22:3) Zikuoneka kuti Ayuda kalelo sankachita manyazi kuphunzitsa ana awo ntchito yamanja, ngakhale kuti anawo anachita maphunziro ena apamwamba. Paulo ayenera kuti anaphunzira ntchitoyi ali mwana, chifukwa anachokera ku Tariso m’dera la Kilikiya, limene linali lotchuka chifukwa chopanga nsalu yamtengo wapatali yopangira matenti. Kodi pankakhala ntchito yotani popanga matenti? Ankawomba nsalu, kudula ndi kusoka nsaluyo, yomwe inali yolimba ndipo ntchito yonseyi inali yowawa.

6, 7. (a) Kodi Paulo ankaiona bwanji ntchito yopanga matenti, nanga n’chiyani chikusonyeza kuti Akula ndi Purisila ankaionanso chimodzimodzi? (b) Kodi Akhristu masiku ano amatsanzira bwanji Paulo, Akula ndi Purisila?

6 Paulo sankaona ntchito yopanga matenti ngati yofunika kwambiri pa moyo wake. Iye ankagwira ntchito imeneyi kuti azipeza zofunika pa moyo wake n’kumalalikira uthenga wabwino ‘popanda ena kulipira.’ (2 Akor. 11:7) Kodi Akula ndi Purisila ankaiona bwanji ntchito yawoyi? Monga Akhristu, n’zodziwikiratu kuti iwo ankaona ntchito yawo ngati mmene Paulo ankaionera. Ndipotu pamene Paulo ankachoka ku Korinto mu 52 C.E., Akula ndi Purisila anasamuka n’kumutsatira ku Efeso, ndipo kumeneko mpingo unkasonkhana kunyumba kwawo. (1 Akor. 16:19) Patapita nthawi, anabwerera ku Roma ndipo kenako anapitanso ku Efeso. Banja lakhama limeneli linkaika patsogolo zinthu za Ufumu ndipo linadzipereka ndi mtima wonse kutumikira ena. Chifukwa cha zimenezi, “mipingo yonse ya anthu a mitundu ina” inawayamikira.​—Aroma 16:3-5; 2 Tim. 4:19.

7 Akhristu omwe amatumikira Mulungu mwakhama masiku ano, amatsanzira Paulo, Akula ndi Purisila ndipo amagwira ntchito molimbika kuti aliyense ‘asawalipirire kanthu kalikonse pofuna kuwathandiza.’ (1 Ates. 2:9) N’zosangalatsa kuti anthu ambiri amene amalalikira za Ufumu nthawi zonse amagwira maganyu kuti azitha kupeza zofunika pa moyo wawo pamene akugwira ntchito yofunika kwambiri yolalikirayi. Mofanana ndi Akula ndi Purisila, atumiki a Yehova ambiri amene amakonda kuchereza alendo amalandira oyang’anira madera kunyumba zawo. Choncho, anthu amene ‘amakhala ochereza’ amaona kuti amalimbikitsidwa akamachita zimenezi.​—Aroma 12:13.

MAKALATA OUZIRIDWA AMENE ANALIMBIKITSA AKHRISTU

Cha m’ma 50-52 C.E., mtumwi Paulo anakhala ku Korinto kwa miyezi yokwana 18, ndipo pa nthawiyi analemba makalata pafupifupi awiri amene anakhala m’gulu la mabuku a Malemba a Chigiriki. Makalata amenewa ndi Atesalonika Woyamba ndi Wachiwiri. N’kutheka kuti mtumwiyu analemba kalata yake yopita kwa Agalatiya pa nthawi yomweyi kapena patadutsa kanthawi kochepa.

Kalata Yoyamba Yopita kwa Atesalonika inali kalata yoyambirira imene Paulo analemba mouziridwa. Paulo anafika ku Tesalonika cha m’ma 50 C.E. pa ulendo wake wachiwiri wolalikira. Mpingo womwe unali utangoyamba kumene, unayamba kutsutsidwa ndipo zimenezi zinachititsa kuti Paulo ndi Sila achoke mumzindawo. (Mac. 17:1-10, 13) Podera nkhawa mpingowo, Paulo anayesa kawiri konse kuti abwerere mumzindawu koma “Satana anatchinga njira” yake. Choncho, Paulo anatumiza Timoteyo kuti akalimbikitse abalewo. Zikuoneka kuti chakumapeto kwa 50 C.E., Timoteyo anakumananso ndi Paulo ku Korinto ndipo anamuuza uthenga wolimbikitsa wonena za mpingo wa ku Tesalonika. Kenako Paulo analemba kalatayi.​—1 Ates. 2:17–3:7.

Kalata Yachiwiri Yopita kwa Atesalonika. N’kutheka kuti Paulo analemba kalatayi pasanapite nthawi yaitali atalemba kalata yoyamba, mwina cha m’ma 51 C.E. M’makalata onse awiri, Timoteyo ndi Silivano (amene amatchedwa Sila m’buku la Machitidwe) anapereka moni limodzi ndi Paulo, koma palibe umboni wosonyeza kuti anthu atatuwa anakhalanso limodzi, Paulo atachoka ku Korinto. (Mac. 18:5, 18; 1 Ates. 1:1; 2 Ates. 1:1) N’chifukwa chiyani Paulo analemba kalata imeneyi? Zikuoneka kuti iye anamva zambiri zokhudza mpingowu, mwina kuchokera kwa munthu amene anakapereka kalata yoyamba ija. Zimene anamvazo zinachititsa Paulo kuti ayamikire abalewo chifukwa cha chikondi ndiponso kupirira kwawo. Komanso iye anawachenjeza kuti apewe maganizo amene abale ena ku Tesalonika anali nawo akuti kukhalapo kwa Ambuye kunali kutsala pang’ono kuchitika pa nthawiyo.​—2 Ates. 1:3-12; 2:1, 2.

Kalata ya Paulo yopita kwa Agalatiya ikusonyeza kuti iye anali atawachezera kawiri konse asanawalembere kalatayi. Mu 47-48 C.E., Paulo ndi Baranaba anapita ku Antiokeya wa ku Pisidiya, Ikoniyo, Lusitara ndi ku Debe, ndipo madera onsewa anali m’chigawo cha Galatiya chimene chinkalamulidwa ndi Aroma. Mu 49 C.E., Paulo anapitanso kumeneku limodzi ndi Sila. (Mac. 13:1–14:23; 16:1-6) Paulo analemba kalata imeneyi chifukwa Ayuda olimbikitsa kwambiri miyambo yawo, amene ankamulonda m’mapazi, ankaphunzitsa kuti Akhristu ankafunika kudulidwa ndiponso kutsatira Chilamulo cha Mose. N’zosakayikitsa kuti Paulo analemba kalata yopita kwa Agalatiya atangomva kuti ayamba kuphunzitsidwa zinthu zabodzazi. Iye ayenera kuti analemba kalatayi ali ku Korinto, koma n’zothekanso kuti anailemba ali ku Efeso pa nthawi imene anaima kumeneko mwachidule pa ulendo wake wobwerera kapena wochokera ku Antiokeya wa ku Siriya.​—Mac. 18:18-23.

“Anthu Ambiri a ku Korinto . . . Anayamba Kukhulupirira” (Machitidwe 18:5-8)

8, 9. Kodi Paulo anachita chiyani anthu atayamba kumutsutsa pa ntchito yake yochitira umboni kwa Ayuda, ndipo zitatero anayamba kulalikira kuti?

8 Mfundo yakuti Paulo ankagwira ntchito yamanja kuti angopeza zosowa zake pamene ankachita utumiki inaonekera pamene Sila ndi Timoteyo anabwera kuchokera ku Makedoniya ndi mphatso zambiri. (2 Akor. 11:9) Nkhaniyi imati nthawi yomweyo, “Paulo anatanganidwa kwambiri ndi ntchito yolalikira mawu a Mulungu.” (Mac. 18:5) Komabe Ayuda ankamutsutsa akamagwira ntchito yake yolalikirayo. Posonyeza kuti iye alibe mlandu chifukwa choti anthuwo anakana okha uthenga wopulumutsa moyo wonena za Khristu, Paulo anakutumula zovala zake n’kuuza Ayuda otsutsawo kuti: “Magazi anu akhale pamutu panu. Ine ndilibe mlandu. Kuyambira panopa ndizipita kwa anthu a mitundu ina.”​—Mac. 18:6; Ezek. 3:18, 19.

9 Kodi Paulo anayamba kulalikira kuti? Munthu wina dzina lake Titiyo Yusito, amene mwina analowa Chiyuda, anali ndi nyumba yake pafupi ndi sunagoge ndipo analandira Paulo kunyumba kwake. Choncho Paulo anachoka mu sunagoge n’kupita kunyumba kwa Yusito. (Mac. 18:7) Paulo ankakhalabe kunyumba kwa Akula ndi Purisila pa nthawi yonse imene anali ku Korinto, koma akafuna kulalikira, ankapita kunyumba kwa Yusito.

10. N’chiyani chikusonyeza kuti Paulo sankangolalikira anthu a mitundu ina okha?

10 Pamene Paulo ananena kuti ‘azipita kwa anthu a mitundu ina,’ kodi ankatanthauza kuti iye sadzalalikiranso Myuda aliyense kapenanso munthu aliyense amene analowa Chiyuda ngakhale atachita chidwi ndi uthenga wabwino? Ayi, sankatanthauza zimenezo. Mwachitsanzo, “Kirisipo, mtsogoleri wa sunagoge, anakhulupirira Ambuye pamodzi ndi anthu onse a m’banja lake.” Zikuoneka kuti anthu ambiri ndithu amene ankasonkhana ndi Kirisipo m’sunagoge anakhalanso okhulupirira chifukwa Baibulo limati: “Anthu ambiri a ku Korinto, amene anamva uthenga wabwino, anayamba kukhulupirira n’kubatizidwa.” (Mac. 18:8) Choncho, mpingo wa Chikhristu umene unali utangoyamba kumene ku Korinto unayamba kusonkhana kunyumba kwa Titiyo Yusito. Ngati Luka analemba nkhani ya m’buku la Machitidwe mwandondomeko monga mwa nthawi zonse, ndiye kuti Ayuda kapena anthu amene analowa Chiyuda amenewo, anakhala Akhristu Paulo atakutumula kale zovala zake. Choncho nkhaniyi ikusonyezeratu kuti mtumwiyu sankaumirira mfundo imodzi koma ankasintha mogwirizana ndi mmene zinthu zilili.

11. Kodi a Mboni za Yehova masiku ano amatsanzira bwanji Paulo poyesetsa kuti alalikire anthu a m’matchalitchi amene amati ndi a Chikhristu?

11 M’mayiko ambiri masiku ano, matchalitchi amene amati ndi a Chikhristu ndi odziwika bwino ndipo anthu awo amatsatira mokhulupirika zimene amawaphunzitsa. M’mayiko ena, amishonale a matchalitchi amene amati ndi a Chikhristu akopa anthu ambiri. Anthu amene amati ndi Akhristu, nthawi zambiri amangotsatira miyambo ngati mmene ankachitira Ayuda a m’nthawi ya atumwi ku Korinto. Komabe, mofanana ndi Paulo, a Mboni za Yehovafe timachita khama kulalikira anthu oterowo kuti tiwathandize kudziwa Malemba molondola. Sititaya mtima ngakhale anthuwo azititsutsa kapena atsogoleri awo achipembedzo azitizunza. Pagulu la anthu “odzipereka potumikira Mulungu, koma sakumudziwa molondola,” pali anthu ambiri ofatsa amene tikufunika kuwafufuza ndi kuwapeza.​—Aroma 10:2.

“Ndili ndi Anthu Ambiri Mumzindawu” (Machitidwe 18:9-17)

12. Kodi Paulo analimbikitsidwa bwanji m’masomphenya?

12 Ngati Paulo anali ndi maganizo oti asapitirize utumiki wake ku Korinto, maganizowo ayenera kuti anasintha usiku umene Ambuye Yesu anaonekera kwa iye m’masomphenya ndi kumuuza kuti: “Usaope, pitiriza kulankhula. Usakhale chete, chifukwa ine ndili nawe. Palibe munthu amene adzakukhudze n’kukuvulaza, popeza ndili ndi anthu ambiri mumzindawu.” (Mac. 18:9, 10) Masomphenya amenewa anali olimbikitsa kwambiri. Ambuye anamutsimikizira Paulo kuti amuteteza ndiponso kuti mumzindawo munali anthu ambiri achidwi. Kodi Paulo anatani ataona masomphenyawo? Timawerenga kuti: “Anakhala kumeneko chaka ndi miyezi 6, akuwaphunzitsa mawu a Mulungu.”​—Mac. 18:11.

13. Kodi pamene Paulo ankayandikira mpando woweruzira milandu ayenera kuti ankaganizira chiyani, koma anali ndi chifukwa chotani chokhulupirira kuti zimenezo sizimuchitikira?

13 Paulo atakhala pafupifupi chaka chimodzi ku Korinto, panachitika zinthu zina zimene zinamutsimikizira kuti Ambuye apitiriza kumuthandiza. “Ayuda ananyamuka mogwirizana n’kuukira Paulo ndipo anamutengera kumpando woweruzira milandu.” (Mac. 18:12) Ena amaganiza kuti mpando woweruzira milandu umenewu unali pamalo okwera ndipo unapangidwa ndi miyala ya mabo ya buluu komanso yoyera. Mpandowo anaukongoletsa kwambiri ndipo uyenera kuti unali cha pakatikati pa msika wa ku Korinto. Patsogolo pa mpando umenewu panali malo aakulu ndithu pamene anthu ankatha kusonkhanapo. Zimene anthu ofufuza zinthu zakale anapeza zikusonyeza kuti mpando woweruzira milandu umenewu uyenera kuti unali pafupi ndi sunagoge ndipo zimenezi zikutanthauza kuti unalinso pafupi ndi nyumba ya Yusito. Pamene Paulo ankayandikira mpandowo ayenera kuti anakumbukira za kuponyedwa miyala kwa Sitefano, yemwe anali Mkhristu woyamba kuphedwa chifukwa cha chikhulupiriro chake. Paulo amene pa nthawiyo ankatchedwa kuti Saulo, “anavomereza zoti Sitefano aphedwe.” (Mac. 8:1) Kodi tsopano Paulo akumananso ndi zimenezo? Ayi, chifukwa analonjezedwa kuti: ‘Palibe munthu amene adzakuvulaze.’​—Mac. 18:10.

Galiyo akuthetsa mlandu wa Paulo pamaso pa anthu amene ankamuimba mlanduwo. Asilikali a Chiroma akukhazikitsa bata kwa gulu la anthu okwiya.

“Atatero anawauza kuti achoke kumpando woweruzira milanduwo.”​—Machitidwe 18:16

14, 15. (a) Kodi Ayuda ankaimba Paulo mlandu wotani, nanga n’chifukwa chiyani Galiyo anathetsa mlanduwo? (b) Kodi n’chiyani chinachitikira Sositene nanga ayenera kuti anatani patapita nthawi?

14 Kodi chinachitika n’chiyani Paulo atafika kumpando woweruzira milanduwo? Pampandowo panakhala woweruza wina dzina lake Galiyo, yemwe anali bwanamkubwa wa ku Akaya, ndipo anali mkulu wake wa Seneca, katswiri wa nzeru za anthu ku Roma. Ayuda anayamba kuimba mlandu Paulo kuti: “Munthu uyu akukopa anthu kuti azipembedza Mulungu m’njira yosemphana ndi chilamulo.” (Mac. 18:13) Ponena zimenezi, Ayudawo ankatanthauza kuti Paulo ankaphwanya malamulo pokopa anthu kuti akhale Akhristu. Koma Galiyo anaona kuti Paulo sanachite “cholakwa” kapena kupalamula “mlandu waukulu” uliwonse. (Mac. 18:14) Galiyo sankafuna kulowerera m’mikangano ya Ayuda. Choncho iye anathetsa mlanduwo Paulo asananene n’komwe chilichonse. Anthu amene ankaimba mlandu Paulowo anakwiya kwambiri ndipo anaphwetsera mkwiyo wawo pa Sositene, amene mwina anakhala mtsogoleri wa sunagoge m’malo mwa Kirisipo. Anthuwo anagwira Sositene “n’kuyamba kumumenya pafupi ndi mpando woweruzira milanduwo.”​—Mac. 18:17.

15 N’chifukwa chiyani Galiyo sanaletse khamu la anthulo kuti lisamenye Sositene? Mwina Galiyo ankaganiza kuti Sositene anali mtsogoleri wa gulu la anthu achiwawawo amene ankadana ndi Paulo ndipo anayeneradi kumenyedwa. Komabe, kaya zinali choncho kapena ayi, zikuoneka kuti zotsatira za nkhaniyi zinali zabwino. M’kalata yake yoyamba yopita kumpingo wa Korinto, imene inalembedwa patapita zaka zingapo chichitikireni zimenezi, Paulo anatchula munthu wina dzina lake Sositene kuti anali m’bale. (1 Akor. 1:1, 2) Kodi Sositene ameneyu anali yemwe uja amene anamenyedwa ku Korinto? Ngati analidi yemweyo, zimene zinamuchitikirazo ziyenera kuti zinamuthandiza kuyamba Chikhristu.

16. Kodi mawu a Ambuye akuti ‘pitiriza kulankhula, usakhale chete, chifukwa ine ndili nawe,’ amatithandiza bwanji pa utumiki wathu?

16 Kumbukirani kuti Ayuda anali atakana kale kumvetsera zimene Paulo ankalalikira pamene Ambuye Yesu anamutsimikizira m’masomphenya kuti: “Usaope, pitiriza kulankhula. Usakhale chete, chifukwa ine ndili nawe.” (Mac. 18:9, 10) Ifenso tiyenera kukumbukira mawu amenewa, makamaka anthu akamakana kumvetsera uthenga wathu. Musaiwale kuti Yehova amaona mmene mitima ilili ndipo amakokera anthu oona mtima kwa iye. (1 Sam. 16:7; Yoh. 6:44) Zimenezi zimatilimbikitsa kuti tizilalikira mwakhama. Chaka chilichonse anthu masauzande amabatizidwa, zomwe zikutanthauza kuti anthu mahandiredi amabatizidwa tsiku lililonse. Anthu amene amamvera lamulo lakuti “mukaphunzitse anthu a mitundu yonse kuti akhale ophunzira anga,” Yesu akuwatsimikizira kuti: “Ine ndili limodzi ndi inu masiku onse mpaka m’nyengo ya mapeto a nthawi ino.”​—Mat. 28:19, 20.

“Yehova Akalola” (Machitidwe 18:18-22)

17, 18. Kodi Paulo ayenera kuti ankaganizira chiyani pamene anali m’ngalawa yopita ku Efeso?

17 Sitikudziwa ngati mpingo wa ku Korinto unalowa m’nyengo ya mtendere chifukwa cha zimene Galiyo anachita kwa anthu amene ankatsutsa Paulo. Komabe, Paulo anakhala “kumeneko kwa masiku ndithu” asanatsanzikane ndi abale a ku Korinto. Chapakatikati pa chaka cha 52 C.E., iye anaganiza zokwera ngalawa kupita ku Siriya kuchokera padoko la Kenkereya, ulendo wokwana pafupifupi makilomita 11 kum’mawa kwa Korinto. Koma asanachoke ku Kenkereya, Paulo “anameta tsitsi lake . . . chifukwa cha lonjezo limene anachita.”c (Mac. 18:18) Kenako, iye ananyamuka limodzi ndi Akula ndi Purisila ndipo anawoloka nyanja ya Aegean kupita ku Efeso m’chigawo cha Asia Minor.

18 Paulo atakwera ngalawa kuchokera ku Kenkereya, ayenera kuti ankaganizira nthawi imene anakhala ku Korinto. Iye ankakumbukira zinthu zabwino zambiri zimene zinkamusangalatsa. Utumiki umene anachita kumeneko kwa miyezi 18 unakhala ndi zotsatirapo zabwino. Mpingo woyamba ku Korinto unakhazikitsidwa ndipo unkasonkhana kunyumba kwa Yusito. Ena mwa anthu amene anakhala Akhristu anali Yusito, Kirisipo ndi banja lake, komanso anthu ena ambiri. Paulo ankakonda kwambiri Akhristu atsopanowo, chifukwa ndi iyeyo amene anawathandiza kukhala Akhristu. Patapita nthawi, anawalembera kalata imene anawatchula kuti iwo anali ngati kalata yomuchitira umboni yolembedwa mumtima mwake. Ifenso timakonda anthu amene tinawathandiza kuti adziwe choonadi. Timalimbikitsidwa kwambiri tikaona anthu amenewa omwe ali ngati “makalata otichitira umboni.”​—2 Akor. 3:1-3.

19, 20. Kodi Paulo anachita chiyani atafika ku Efeso, nanga tingaphunzire chiyani kwa iye pamene tikuyesetsa kuchita zimene Mulungu amafuna?

19 Atangofika ku Efeso, Paulo anayamba kugwira ntchito yake yofunika. Iye “analowa m’sunagoge n’kuyamba kukambirana ndi Ayuda.” (Mac. 18:19) Pa nthawiyi, Paulo sanakhalitse ku Efeso moti ngakhale kuti abale anam’pempha kuti akhalitse, “iye sanalole.” Ndipo pamene ankatsanzikana ndi abale a ku Efeso, iye anawauza kuti: “Yehova akalola ndidzabweranso kudzakuonani.” (Mac. 18:20, 21) Mosakayikira, Paulo anazindikira kuti uthenga wabwino unafunika kulalikidwa kwambiri ku Efeso. Mtumwiyu anaganiza zobwereranso, koma anasankha kusiya nkhaniyi m’manja mwa Yehova. Chimenechitu ndi chitsanzo chabwino kwambiri chofunika kuti tizichikumbukira. Kuti Mulungu atithandize kukwaniritsa zolinga zathu zauzimu, tiziyamba ndi ifeyo kuchitapo kanthu. Komabe, nthawi zonse tiyenera kudalira malangizo a Yehova ndi kuyesetsa kuchita zinthu zogwirizana ndi zimene iye amafuna.​—Yak. 4:15.

20 Atasiyana ndi Akula ndi Purisila ku Efeso, Paulo anayamba ulendo wa panyanja ndipo anafika ku Kaisareya. Zikuoneka kuti iye “anapita” ku Yerusalemu kukapereka moni ku mpingo wa kumeneko. (Mac. 18:22) Kenako Paulo anapita kunyumba kwake ku Antiokeya wa ku Siriya. Iye anamaliza bwino kwambiri ulendo wake wachiwiri waumishonale. Koma kodi Paulo anakumana ndi zotani pa ulendo wake womaliza waumishonale?

LONJEZO LA PAULO

Lemba la Machitidwe 18:18 limanena kuti pamene Paulo anali ku Kenkereya, “anameta tsitsi lake . . . chifukwa cha lonjezo limene anachita.” Kodi lonjezo limeneli linali lotani?

Lonjezo ndi mawu amene munthu amauza Mulungu mwa kufuna kwake kuti adzachita zinazake, adzapereka nsembe, kapenanso ayamba kumutumikira m’njira inayake yapadera. Ena amaganiza kuti Paulo anameta tsitsi lake kuti akwaniritse lonjezo la Mnaziri. Komabe tisaiwale kuti mogwirizana ndi Malemba, Mnaziri amayenera kumeta tsitsi lake “pakhomo la chihema chokumanako,” akakwanitsa nthawi imene analonjeza kuti achita utumiki wapadera kwa Yehova. Choncho, zikuoneka kuti Mnaziri ankachita zimenezi ku Yerusalemu kokha, osati ku Kenkereya.​—Num. 6:5, 18.

Nkhani ya m’buku la Machitidwe sinena chilichonse za nthawi imene Paulo anachita lonjezo limeneli. N’kutheka kuti iye analonjeza zimenezi asanakhale n’komwe Mkhristu. Nkhaniyi sinenanso chilichonse ngati Paulo anapempha zinthu zapadera kwa Yehova. Buku lina limanena kuti Paulo anameta tsitsi lake ngati “chizindikiro chothokoza Mulungu chifukwa chomuteteza. Chitetezo chimenechi chinathandiza kuti [Paulo] amalize utumiki wake ku Korinto.”

a Onani bokosi lakuti “Mzinda wa Korinto Unali Pakati pa Nyanja Ziwiri.”

b Onani bokosi lakuti “Makalata Ouziridwa Amene Analimbikitsa Akhristu.”

c Onani bokosi lakuti “Lonjezo la Paulo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena