Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • th phunziro 5 tsamba 8
  • Kuwerenga Molondola

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuwerenga Molondola
  • Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Nkhani Yofanana
  • Kuŵerenga Molondola
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Chitani Khama pa Kuŵerenga
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Mmene Tingaŵerengere ndi Kukumbukira
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Bokosi la Mafunso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
Onani Zambiri
Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
th phunziro 5 tsamba 8

PHUNZIRO 5

Kuwerenga Molondola

Lemba

1 Timoteyo 4:13

MFUNDO YAIKULU: Muziwerenga momveka bwino komanso mosalakwitsa.

MMENE MUNGACHITIRE:

  • Muzikonzekera bwino. Muzidzifunsa kuti, N’chifukwa chiyani mawu amenewa analembedwa? Muziwerenga magulu a mawu osati kumangotchula liwu ndi liwu. Muzipewa kuwonjezera mawu, kudumpha mawu kapena kusemphanitsa mawu. Muzitsatira zizindikiro zonse za m’kalembedwe.

    Mfundo yothandiza

    Muzipempha mnzanu kuti azimvetsera pamene mukuwerenga ndipo azikuuzani pamene mwalakwitsa.

  • Muzitchula mawu alionse molondola. Ngati simukudziwa katchulidwe kabwino ka mawu, muyenera kufufuza, kumvetsera nkhani zojambulidwa kapena kufunsa anzanu omwe amadziwa bwino.

  • Muzilankhula momveka bwino. Kuti mawu anu azituluka bwino muyenera kukweza bwino mutu komanso kutsegula pakamwa mokwanira. Muzitchula mawu alionse momveka bwino.

    Mfundo yothandiza

    Koma sikuti muzitchula mawu mokokomeza mpaka kufika podabwitsa anthu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena