Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesu Anasankha Atumwi 12
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Yesu ali ndi atumwi ake 12

      MUTU 80

      Yesu Anasankha Atumwi 12

      Yesu atalalikira pafupifupi kwa chaka ndi hafu, ankafunika kusankha zinthu zina zofunika kwambiri. Anafunika kusankha anthu apadera oti azigwira nawo ntchito yolalikira. Anthuwa anafunikanso kuwaphunzitsa kuti adzathe kutsogolera mpingo wa Chikhristu iye akadzapita kumwamba. Yesu anaona kuti m’pofunika kuti Yehova amutsogolere posankha anthuwo. Choncho anapita kuphiri kwayekhayekha ndipo anapemphera usiku wonse. Kutacha, anaitana ophunzira ake ena ndipo anasankhapo anthu 12 oti akhale atumwi. Kodi ukukumbukira mayina awo? Anali Petulo, Andireya, Yakobo, Yohane, Filipo, Batolomeyo, Tomasi, Mateyu, Yakobo mwana wa Alifeyo, Tadeyo, Simoni ndi Yudasi Isikariyoti.

      Andireya, Petulo, Filipo, Yakobo

      Andireya, Petulo, Filipo, Yakobo

      Atumwi 12 amenewa ankayenda ndi Yesu. Kenako atawaphunzitsa, anayamba kumapita okha. Yehova anawapatsa mphamvu kuti azitha kutulutsa ziwanda komanso kuchiritsa odwala.

      Yohane, Mateyu, Batolomeyo, Tomasi

      Yohane, Mateyu, Batolomeyo, Tomasi

      Yesu ankaona kuti atumwi 12 amenewa ndi anzake ndipo ankawakhulupirira. Koma Afarisi ankaganiza kuti atumwiwo anali osaphunzira komanso anthu wamba. Komatu Yesu anawaphunzitsa kuti azigwira bwino ntchito yawo. Atumwiwo anakhalabe ndi Yesu pa nthawi yofunika kwambiri pa moyo wake. Mwachitsanzo, analipo Yesu atatsala pang’ono kuphedwa komanso ataukitsidwa. Mofanana ndi Yesu ambiri mwa atumwiwa anali ochokera ku Galileya. Ndipo ena anali okwatira.

      Yakobo mwana wa Alifeyo, Yudasi Isikariyoti, Tadeyo, Simoni

      Yakobo mwana wa Alifeyo, Yudasi Isikariyoti, Tadeyo, Simoni

      Koma atumwiwa sanali angwiro ngati ife tomwe ndipo ankalakwitsa zinthu zina. Pena ankalankhula asanaganize ndiponso ankasankha molakwika. Nthawi zinanso sankaleza mtima komanso ankakangana kuti wamkulu ndi ndani. Komabe atumwiwa anali anthu abwino ndipo ankakonda Yehova. Iwo ndi amene anali anthu oyamba kukhala mumpingo wa Chikhristu Yesu atapita kumwamba.

      “Ndakutchulani kuti anzanga, chifukwa ndakudziwitsani zinthu zonse zimene ndamva kwa Atate wanga.”​—Yohane 15:15

      Mafunso: Kodi Yesu anasankha anthu 12 ati kuti akhale atumwi ake? Kodi Yesu anatumiza atumwi ake kuti akagwire ntchito iti?

      Mateyu 10:1-10; Maliko 3:13-19; 10:35-40; Luka 6:12-16; Yohane 15:15; 20:24, 25; Machitidwe 2:7; 4:13; 1 Akorinto 9:5; Aefeso 2:20-22

  • Ulaliki wa Paphiri
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Yesu akulalikira paphiri kwa anthu ambiri

      MUTU 81

      Ulaliki wa Paphiri

      Yesu atasankha atumwi ake 12, anatsika m’phiri n’kupita pamalo amene panasonkhana anthu ambiri. Anthuwo anali ochokera ku Galileya, Yudeya, Turo, Sidoni, Siriya komanso kutsidya kwa mtsinje wa Yorodano. Anamubweretsera anthu odwala matenda osiyanasiyana komanso amene ankavutitsidwa ndi ziwanda. Yesu anawachiritsa onsewo. Kenako anakhala pansi n’kuyamba kuwaphunzitsa. Anafotokoza zimene munthu angachite ngati akufuna kuti Mulungu akhale mnzake. Yesu anatinso tiyenera kuzindikira kuti timafunika kutsogoleredwa ndi Yehova ndipo tiyenera kuphunzira za iye kuti tizimukonda. Koma ananena kuti sitingakonde Mulungu ngati sitikonda anzathu. Komanso tiyenera kuchitira zabwino aliyense, ngakhale adani athu.

      Yesu anati: ‘Kungokonda anzanu si kokwanira. Muyenera kukondanso adani anu komanso muzikhululuka kuchokera pansi pa mtima. Ngati wina wakulakwirani, muzipita kukakambirana naye n’kupepesana. Muzichitira anthu zimene mungafune kuti iwonso akuchitireni.’

      Yesu akulalikira paphiri kwa anthu ambiri

      Yesu anaperekanso malangizo abwino okhudza chuma. Iye anati: ‘Kukhala pa ubwenzi ndi Mulungu n’kofunika kwambiri kuposa kukhala ndi ndalama zambiri. Munthu angathe kukuberani ndalama koma sangakubereni ubwenzi wanu ndi Yehova. Siyani kudandaula kuti: “Mawa tidzadya chiyani, tidzamwa chiyani nanga tidzavala chiyani?” Ganizirani za mbalame. Mulungu amaonetsetsa kuti nthawi zonse zili ndi chakudya chokwanira. Kudandaula sikungapangitse kuti mukhale ndi moyo wautali. Musaiwale kuti Yehova amadziwa zimene mukufunikira.’

      Anthuwo anali asanamvepo munthu akulankhula ngati mmene Yesu ankalankhulira. Atsogoleri a chipembedzo anali asanawaphunzitsepo zimenezi. N’chifukwa chiyani Yesu ankatha kuphunzitsa bwino chonchi? Chifukwa choti zonse zimene ankaphunzitsa zinkachokera kwa Yehova.

      “Senzani goli langa ndipo lolani kuti ndikuphunzitseni, chifukwa ndine wofatsa ndi wodzichepetsa ndipo mudzatsitsimulidwa.”​—Mateyu 11:29

      Mafunso: Kodi tingatani kuti Mulungu akhale mnzathu? Kodi Mulungu amafuna kuti tizichitira anthu ena zinthu zotani?

      Mateyu 4:24, 25; 5:1-48; 6:19-34; 7:28, 29; Luka 6:17-31

Mabuku a Chichewa (1974-2026)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena