Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Ndiyenera Kubatizidwa?—Gawo 1: Tanthauzo la Kubatizidwa
    Zimene Achinyamata Amafunsa
    • Mnyamata akubatizidwa kumsonkhano wachigawo wa Mboni za Yehova.

      ZIMENE ACHINYAMATA AMADZIFUNSA

      Kodi Ndiyenera Kubatizidwa?—Gawo 1: Tanthauzo la Kubatizidwa

      Chaka chilichonse, achinyamata ambiri amene akukulira m’banja la Mboni za Yehova amabatizidwa. Kodi inuyo mukuganizira zobatizidwa? Ngati zili choncho, poyamba muyenera kumvetsa tanthauzo la kudzipereka kwa Mulungu komanso kubatizidwa.

      • Kodi kubatizidwa kumatanthauza chiyani?

      • Kodi kudzipereka kwa Mulungu kumatanthauza chiyani?

      • N’chifukwa chiyani kubatizidwa n’kofunika?

      • Zimene achinyamata anzanu amanena

      • Zimene anthu ena amanena komanso zoona zake za nkhaniyi

      Kodi kubatizidwa kumatanthauza chiyani?

      Mawu oti kubatizidwa omwe amapezeka m’Baibulo amatanthauza kumizidwa thupi lonse m’madzi osati kungowazidwa ndi madzi basi. Mawuwa amakhalanso ndi tanthauzo lophiphiritsa.

      • Kumizidwa m’madzi mukabatizidwa kumasonyeza kuti mwasiya kumangochita zimene zimakusangalatsani inuyo.

      • Kutulutsidwa m’madzi kumasonyeza kuti mwayamba moyo watsopano wochita zimene zimasangalatsa Mulungu.

      Mukabatizidwa mumasonyeza pa gulu kuti Yehova ali ndi ulamuliro wosankha zoyenera ndi zosayenera komanso kuti mwalonjeza kuchita zimene iye amafuna.

      Zoti muganizire: N’chifukwa chiyani mungafune kusonyeza pa gulu kuti mwalonjeza kumvera Yehova? Onani 1 Yohane 4:19 ndi Chivumbulutso 4:11.

      Kodi kudzipereka kwa Mulungu kumatanthauza chiyani?

      Musanabatizidwe muyenera kudzipereka kwa Yehova muli nokha. Kodi mungachite bwanji zimenezi?

      Muyenera kupemphera kwa Yehova muli nokha n’kumamuuza kuti mwalonjeza kudzamutumikira mpaka kalekale. Muyenera kumuuzanso kuti muzidzachita zimene iye amafuna zivute zitani mosatengera zimene anthu ena angasankhe kuchita.

      Mukabatizidwa mumasonyeza pa gulu zimene munachita panokha podzipereka kwa Mulungu. Mumasonyeza kwa anthu ena kuti mwasankha kuchita zimene Yehova amafuna m’malo mochita zofuna zanu.—Mateyu 16:24.

      Zoti muganizire: N’chifukwa chiyani moyo wanu umakhala wabwino kwambiri mukayamba kuchita zimene Yehova amafuna? Onani Yesaya 48:17, 18 ndi Aheberi 11:6.

      N’chifukwa chiyani kubatizidwa n’kofunika?

      Yesu ananena kuti ophunzira ake ayenera kubatizidwa. (Mateyu 28:19, 20) Choncho masiku anonso, Akhristu ayenera kubatizidwa. Baibulo limanena kuti munthu ayenera kubatizidwa kuti adzapulumuke.—1 Petulo 3:21.

      Koma muyenera kubatizidwa chifukwa chokonda Yehova ndi kuyamikira zimene iye amachita. Muyenera kukhala ndi mtima umene wolemba masalimo unali nawo polemba kuti: “Yehova ndidzamubwezera chiyani pa zabwino zonse zimene wandichitira? . . . Ndidzaitana pa dzina la Yehova. Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova.”—Salimo 116:12-14.

      Zoti muganizire: Kodi Yehova wakuchitirani zinthu zotani, nanga mungamubwezere bwanji? Onani Deuteronomo 10:12, 13 ndi Aroma 12:1.

      Zimene achinyamata anzanu amanena

      Mijin.

      “Mukadzipereka kwa Yehova mumamulonjeza zinazake ndipo kuchita zimenezi ndi nkhani yaikulu kwambiri. Koma munthu wodzipereka kwa Yehova amapeza madalitso ambiri. Zili choncho chifukwa Yehova angatisamalire bwino kwambiri kuposa mmene tingachitire.”—Mijin.

      Ember.

      “Yehova wasonyeza kale kuti amakukondani inuyo. Mukabatizidwa mudzasonyeza kuti mumamukonda kwambiri iyeyo. Kukhala wobatizidwa ndi mwayi waukulu komanso kumabweretsa madalitso ambiri.”—Ember.

      Julian.

      “Kusankha kudzipereka kwa Mulungu komanso kubatizidwa ndi chinthu chofunika kwambiri chimene mungasankhe pa moyo wanu. Koma simuyenera kuopa. Ngati mwakonzekera komanso mwasankha kuchita zimenezi pa zolinga zabwino, ndi chinthu chabwino kwambiri chimene mungasankhe pa moyo wanu wonse.”—Julian.

      Zimene anthu ena amanena komanso zoona zake za nkhaniyi

      ZIMENE ANTHU ENA AMANENA — Anthu aakulu okha ndi amene ali nzeru zokwanira kuti abatizidwe.

      ZOONA ZAKE — Munthu amasonyeza kuti ndi wanzeru osati chifukwa cha msinkhu wake koma chifukwa chakuti amakonda Yehova komanso ndi wofunitsitsa kumumvera. Ali aang’ono, Yosefe, Samueli ndi Yosiya anasonyeza kuti ndi anzeru. Masiku anonso, achinyamata ambiri akuchita zimenezi.

      Baibulo limati: “Mnyamata amadziwika ndi ntchito zake, ngati zochita zake zili zoyera ndiponso zowongoka.”—Miyambo 20:11.

      ZIMENE ANTHU ENA AMANENA — Ngati anzanu akubatizidwa, nanunso muyenera kubatizidwa.

      ZOONA ZAKE — Munthu ayenera kusankha yekha kudzipereka kwa Mulungu komanso kubatizidwa ndipo ayenera kusankha zimenezi ndi mtima wonse. Sikuti ayenera kuchita zimenezi chifukwa wafika pa msinkhu winawake ndipo ndi zimene anthu ena anachita kapena ndi zimene ena amayembekezera.

      Baibulo limati: “Anthu [a Mulungu] adzadzipereka mofunitsitsa.”—Salimo 110:3.

      ZIMENE ANTHU ENA AMANENA — Ngati simunabatizidwe, simungaimbidwe mlandu pa zimene mumachita.

      ZOONA ZAKE — Mumayankha mlandu kwa Yehova osati pambuyo pobatizidwa koma pambuyo podziwa zimene iye amaona kuti ndi zoyenera ndi zosayenera.

      Baibulo limati: “Ngati munthu akudziwa kuchita chabwino koma sakuchichita, akuchimwa.”—Yakobo 4:17.

      ZIMENE ZINGAKUTHANDIZENI: Ngati mumaopa udindo wokhala Mkhristu wobatizidwa, mungachite bwino kudzifufuza kuti mudziwe chifukwa chake mumaopa komanso zimene zingakuthandizeni kuchotsa manthawo. Ndi bwino kuwerenga Chaputala 37 m’buku la Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri.

      Mfundo zobwereza: N’chifukwa chiyani kubatizidwa n’kofunika?

      • Yesu ananena kuti ophunzira ake ayenera kubatizidwa.

      • Munthu ayenera kubatizidwa kuti adzapulumuke.

      • Ndi mwayi waukulu kwambiri kutumikira Yehova ngati Mkhristu wodzipereka kwa iye komanso wobatizidwa.

  • Kodi Ndiyenera Kubatizidwa?—Gawo 2: Kukonzekera Kubatizidwa
    Zimene Achinyamata Amafunsa
    • Mtsikana akufufuza mfundo zokhudza kubatizidwa pogwiritsa ntchito Baibulo komanso mabuku othandiza kuphunzira Baibulo.

      ZIMENE ACHINYAMATA AMADZIFUNSA

      Kodi Ndiyenera Kubatizidwa?—Gawo 2: Kukonzekera Kubatizidwa

      Ngati mukutsatira mfundo za m’Baibulo komanso mukuyesetsa kukhala pa ubwenzi wolimba ndi Mulungu, muyenera kuti mukuganiza zobatizidwa. Koma kodi mungadziwe bwanji ngati mwakonzeka kuchita zimenezi?a

      Zimene zili m’nkhaniyi

      • Kodi ndiyenera kudziwa zochuluka bwanji?

      • Kodi ndiyenera kuchita zotani?

      • Zimene achinyamata anzanu amanena

      Kodi ndiyenera kudziwa zochuluka bwanji?

      Ngati mukukonzekera kubatizidwa simuyenera kuloweza pamtima zinthu zambiri ngati mmene mungachitire pokonzekera mayeso akusukulu. Koma muyenera kugwiritsa ntchito mphamvu zanu za kuganiza kuti mudzitsimikizire zoti Baibulo limaphunzitsa mfundo zoona. (Aroma 12:1) Mwachitsanzo:

      • Kodi mumakhulupirira ndi mtima wonse kuti kuli Mulungu komanso ndi woyenera kumulambira?

        Baibulo limati: “Pakuti aliyense wofika kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti iye alikodi, ndi kuti amapereka mphoto kwa anthu omufunafuna ndi mtima wonse.”—Aheberi 11:6.

        Dzifunseni kuti: ‘N’chifukwa chiyani ndimakhulupirira kuti kuli Mulungu?’ (Aheberi 3:4) ‘N’chifukwa chiyani ndiyenera kumulambira?’—Chivumbulutso 4:11.

        Kodi mukufuna thandizo? Onani nkhani yakuti “Kodi Zinthu Zinachita Kulengedwa?—Gawo 1: N’chifukwa Chiyani Ndimakhulupirira Kuti Kuli Mulungu?”

      • Kodi mumakhulupirira ndi mtima wonse kuti mfundo za m’Baibulo ndi zochokera kwa Mulungu?

        Baibulo limati: “Malemba onse anauziridwa ndi Mulungu, ndipo ndi opindulitsa pa kuphunzitsa, kudzudzula, kuwongola zinthu ndi kulangiza m’chilungamo.”—2 Timoteyo 3:16.

        Dzifunseni kuti: ‘N’chifukwa chiyani sindikhulupirira kuti m’Baibulo muli maganizo a anthu basi?’—Yesaya 46:10; 1 Atesalonika 2:13.

        Kodi mukufuna thandizo? Onani nkhani yakuti “Kodi Baibulo Lingandithandize Bwanji?—Gawo 1: Kuganizira Mozama Mfundo za M’Baibulo”

      • Kodi mumakhulupirira ndi mtima wonse kuti Yehova akugwiritsa ntchito mpingo wa Chikhristu pokwaniritsa cholinga chake?

        Baibulo limati: “Kwa [Mulungu] kukhale ulemerero kudzera mwa mpingo ndi mwa Khristu Yesu, ku mibadwo yonse kwamuyaya.”—Aefeso 3:21.

        Dzifunseni kuti: ‘Kodi ndimaona kuti zimene ndimaphunzira kumisonkhano zimachokera kwa anthu kapena kwa Yehova?’ (Mateyu 24:45) ‘Kodi ndimapezeka pamisonkhano ngakhale pamene makolo anga sangathe (ngati amakulolani kupezeka)?’—Aheberi 10:24, 25.

        Kodi mukufuna thandizo? Onani nkhani yakuti “N’chifukwa Chiyani Ndiyenera Kupezeka Pamisonkhano ya pa Nyumba ya Ufumu?”

      Kodi ndiyenera kuchita zotani?

      Simuyenera kukhala munthu wangwiro kuti mubatizidwe. Komabe, muyenera kusonyeza kuti mumafunitsitsa ‘kupatuka pa zinthu zoipa ndi kuchita zabwino.’ (Salimo 34:14) Mwachitsanzo:

      • Kodi mumatsatira mfundo za Yehova pa moyo wanu?

        Baibulo limati: “Khalani ndi chikumbumtima chabwino.”—1 Petulo 3:16.

        Dzifunseni kuti: ‘Kodi ndimasonyeza bwanji kuti ndaphunzitsa “mphamvu zanga za kuzindikira kusiyanitsa choyenera ndi chosayenera”?’ (Aheberi 5:14) ‘Kodi pali nthawi zina pamene ndakana kuchita zinthu zoipa zimene anzanga ankafuna? Kodi ndimasankha kucheza ndi anthu amene amandilimbikitsa kuchita zabwino?’—Miyambo 13:20.

        Kodi mukufuna thandizo? Onani nkhani yakuti “Kodi Ndingaphunzitse Bwanji Chikumbumtima Changa?”

      • Kodi mumazindikira kuti muyenera kuyankha mlandu pa zimene mumachita?

        Baibulo limati: “Aliyense wa ife adzayankha yekha kwa Mulungu.”—Aroma 14:12.

        Dzifunseni kuti: ‘Kodi ndine woona mtima podzifufuza komanso pochita zinthu ndi anthu ena?’ (Aheberi 13:18) ‘Kodi ndimavomereza ndikalakwitsa zinthu kapena ndimakonda kuzibisa, apo ayi kuloza chala anthu ena?’—Miyambo 28:13.

        Kodi mukufuna thandizo? Onani nkhani yakuti “Kodi Ndizitani Ndikalakwitsa Zinazake?”

      • Kodi muli pa ubwenzi wolimba ndi Yehova?

        Baibulo limati: “Yandikirani Mulungu, ndipo iyenso adzakuyandikirani.”—Yakobo 4:8.

        Dzifunseni kuti: ‘Kodi ndikuchita zotani kuti ndilimbitse ubwenzi wanga ndi Yehova?’ Mwachitsanzo, ‘Kodi ndimawerenga Baibulo pafupipafupi?’ (Salimo 1:1, 2) ‘Kodi ndimakonda kupemphera?’ (1 Atesalonika 5:17) ‘Nanga kodi ndimanena zinthu zimene zili mumtima mwanga ndikamapemphera? Kodi anzanga ndi amene ndi anzakenso a Yehova?’—Salimo 15:1, 4.

        Kodi mukufuna thandizo? Onani nkhani yakuti “Kodi Baibulo Lingandithandize Bwanji?—Gawo 2: Zimene Mungachite Kuti Kuwerenga Baibulo Kuzikusangalatsani.”

      ZIMENE ZINGAKUTHANDIZENI: Kuti mukonzekere kubatizidwa, werengani chaputala 37 m’buku la Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri. Makamaka, onani zimene mungalembe patsamba 308 ndi 309.

      a Werengani nkhani yakuti “Kodi Ndiyenera Kubatizidwa?—Gawo 1,” yomwe ikufotokoza tanthauzo ndiponso kufunika kwa kudzipereka kwa Mulungu komanso kubatizidwa.

      Zimene achinyamata anzanu amanena

      Gabriella.

      “Kulemba mayankho a mafunso okhudza kubatizidwa m’buku la Zimene Achinyamata Amafunsa kunandithandiza kuona zinthu zimene ndiyenera kusintha ndisanabatizidwe. Kunandithandizanso kukhala ndi zolinga zimene ndinkafuna kukwaniritsa nditabatizidwa. Mukadzipereka kwa Yehova muli ndi udindo waukulu kwambiri koma mulinso ndi mwayi waukulu kuposa mwayi wina uliwonse.”—Gabriella.

      Caleb.

      “M’Baibulo, Timoteyo anauzidwa kuti: ‘Pitiriza kutsatira zimene unaphunzira ndi zimene unakhulupirira pambuyo pokhutira nazo.’” (2 Timoteyo 3:14) “Pezani nthawi yophunzira Mawu a Mulungu n’cholinga choti mukhulupirire ndi mtima wonse zimene Mawuwa amaphunzitsa. Mudzadzipereka kwa Yehova osati kwa anthu ena. Choncho mukamaganiza zobatizidwa, muyenera kuganizira kwambiri mmene Yehova amamvera.”—Caleb.

      Mfundo zobwereza: Kodi ndingakonzekere bwanji kubatizidwa?

      Fufuzani zimene mumakhulupirira. Kodi mumakhulupirira ndi mtima wonse kuti kuli Mulungu? Nanga kodi mumakhulupirira kuti ndi woyenera kumulambira? Kodi mumakhulupirira kuti Baibulo ndi Mawu ouziridwa a Mulungu komanso kuti iye amagwiritsa ntchito gulu lathu kuti azikwaniritsa cholinga chake?

      Fufuzani zimene mumachita. Kodi mumatsatira mfundo za Yehova pa moyo wanu? Kodi mumadziwa kuti mudzayankha mlandu pa zimene mumachita? Nanga kodi muli pa ubwenzi wolimba ndi Yehova?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena