Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g03 2/8 tsamba 11
  • Osamangokhulupirira za M’maluŵa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Osamangokhulupirira za M’maluŵa
  • Galamukani!—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Tiyenera Kugwiritsa Ntchito Intaneti Mwanzeru
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kodi Kupeza Chibwenzi pa Intaneti Kungakhaledi Koopsa?
    Galamukani!—2005
  • Uthenga Wabwino pa Internet
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Ana Akamagwiritsa Ntchito Intaneti Zimene Makolo Angachite
    Galamukani!—2008
Onani Zambiri
Galamukani!—2003
g03 2/8 tsamba 11

Osamangokhulupirira za M’maluŵa

Kudziŵa zenizeni pa nkhani zosiyanasiyana n’kovuta kwambiri. Maboma ndiponso makampani akamanena zinthu amaphatikizamo timabodza. Nthaŵi zambiri, ofalitsa nkhani amalonjeza kuti azilemba nkhani zawo mosakondera koma satero. Nthaŵi zina madokotala safotokoza mavuto onse omwe angabuke chifukwa cha mankhwala omwe atipatsa. Kodi pali njira ina iliyonse yodziŵira zinthu zoti n’kuzikhulupirira?

Anthu ambiri anatama kubwera kwa Intaneti n’kumanena kuti ndiyo njira yodalirika yodziŵira zinthu zimene zikuchitika padziko lonse. Inde, zimenezi zingatheke ngati mukudziŵa mmene mungapezere zinthuzo pofufuza pa kompyuta. Nkhani ya mkonzi m’nyuzipepala ya The New York Times, inati: “Ubwino wa Intaneti ndi woti ingaphunzitse anthu ambiri mwamsanga kusiyana ndi njira ina iliyonse yofalitsira nkhani. Ndipo kuipa kwake n’koti ingapinimbitse bongo wa anthu mwamsanga kusiyana ndi njira ina iliyonse yofalitsira nkhani.”

Nkhani ya mkonziyo inanenanso kuti: “Popeza kuti Intaneti ndi yochititsa kaso, anthu osaidziŵa bwino amaikhulupirira kwambiri. Sadziŵa kuti kuipa kwake n’kofanana ndi dzenje la nyansi chifukwa pa Intaneti pamapezeka nkhani zilizonse n’zopanda umboni zomwe.” N’zomvetsa chisoni kuti monga momwe mkonzi wa nkhaniyi analembera, palibe njira iliyonse yochotserapo nkhani zachabechabezo.

Wina aliyense angalembe nkhani iliyonse m’magazini, kapenanso m’buku lopezeka pa Intaneti. Motero tizisamala ndiponso tiphunzire kuti tikamaŵerenga zinthu tisamangokhulupirira zilizonse, ndi za m’maluŵa zomwe. Aliyense amene amafuna kudziŵa zenizeni pa nkhani inayake ayenera kuonetsetsa kuti komwe kwachokera nkhaniyo n’kodalirika. Izi zingatenge nthaŵi ndithu. Koma tikatero ndiponso tikadziŵa zenizeni za nkhaniyo, maganizo athu sangakhale opotoka ndiponso sitingamakayikire pochita zinthu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena