Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 8/10 tsamba 11-31
  • Zoti Banja Likambirane

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zoti Banja Likambirane
  • Galamukani!—2010
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ndani Ankagwira Ntchito Imeneyi?
  • KODI MUKUDZIWA CHIYANI ZOKHUDZA MTUMWI ANDIREYA?
  • ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE
  • KUCHOKERA M’MAGAZINI INO
  • MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2010
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2010
  • Kodi Mungayankhe Bwanji?
    Galamukani!—2008
  • Kodi Mungayankhe Bwanji?
    Galamukani!—2008
Onani Zambiri
Galamukani!—2010
g 8/10 tsamba 11-31

Zoti Banja Likambirane

Kodi Ndani Ankagwira Ntchito Imeneyi?

1. Tchulani asodzi awiri amene anali ana a Zebedayo komanso atumwi a Yesu.

Lembani mayankho anu m’mizere ili m’munsiyi.

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Mateyo 4:21, 22.

․․․․․

2. Tchulani mayina a atumwi ena awiri omwe analinso asodzi.

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Mateyo 4:18.

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi n’chifukwa chiyani Yesu ananena kuti ophunzira ake adzakhala “asodzi a anthu”? (Mateyo 4:19) Kodi usodzi wa nsomba ndi wa anthu ukufanana bwanji komanso ukusiyana bwanji?

KODI MUKUDZIWA CHIYANI ZOKHUDZA MTUMWI ANDIREYA?

3. Asanayambe kutsatira Yesu, kodi Andireya anali wophunzira wa ndani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Maliko 1:4; Yohane 1:35-40.

․․․․․

4. Kodi Andireya anauza ndani za Yesu, ndipo zotsatira zake zinali zotani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Yohane 1:40-42.

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi kuuza abale anu zinthu zimene mukudziwa zokhudza Yesu kuli ndi ubwino wotani? Komabe, kodi abale anu ena angachite chiyani mutawauza zimenezi?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Mateyo 10:32-37.

ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE

Kodi mungathe kupeza zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

KUCHOKERA M’MAGAZINI INO

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 3 Kodi munthu wochenjera amasamalira chiyani? Miyambo 14:․․․

TSAMBA 8 Kodi Mulungu anadzipatsa dzina loti chiyani? Salmo 83:․․․

TSAMBA 20 Kodi angelo amene anachimwa chinawachitikira n’chiyani? Yuda:․․․

TSAMBA 26 Kodi n’chiyani chimachitika munthu ‘akamalimbikira mkwiyo’? Miyambo 30:․․․

● Mayankho ali patsamba 11

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Yakobe ndi Yohane.

2. Petulo ndi Andireya.

3. Yohane M’batizi.

4. M’bale wake Petulo, ndipo anadzakhala wophunzira wa Yesu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena