Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 4/11 tsamba 3
  • Imfa Yovuta Kwambiri Kuiwala

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Imfa Yovuta Kwambiri Kuiwala
  • Galamukani!—2011
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Tingathandize Bwanji Mwana Yemwe Wachibale Wake Wamwalira?
    Galamukani!—2012
  • Mukamaona Kuti Simungathenso Kupirira
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2019
  • Kodi Ndingatani Ngati M’bale Wanga Wadzipha?
    Galamukani!—2008
  • “Ndasunga Chikhulupiriro”
    Nsanja ya Olonda—1994
Onani Zambiri
Galamukani!—2011
g 4/11 tsamba 3

Imfa Yovuta Kwambiri Kuiwala

Nicolle anali kamtsikana kathanzi. Koma tsiku lina madzulo anayamba kudandaula kuti mutu ukumupweteka, choncho makolo ake anamutengera kuchipatala. Madzulo a tsiku lotsatira madokotala akumuyeza, Nicolle anadwala mwadzidzidzi matenda a mtima. Atamuyezanso zinthu zina anapeza kuti mapapo ake, impso komanso mtima wake zinali ndi matenda. Pasanathe masiku awiri, Nicolle anamwalira. Pa nthawiyi n’kuti ali ndi zaka zitatu zokha.

ZIMAKHALA zopweteka kwambiri munthu amene timamukonda akamwalira. Ndipo nthawi zambiri zimavuta kuiwala. Mwachitsanzo, mayi ake a Nicolle, a Isabelle, anati: “Zimandivuta kuiwala imfa ya mwana wanga Nicolle. Zimandipweteka ndikakumbukira nthawi imene ndinkamunyamula m’manja komanso kumukumbatira. Ndimakumbukira kuti tsiku lililonse ankabwera kwa ine atatenga maluwa m’manja n’kundipatsa. Nthawi zonse ndimaganiza za Nicolle.”

Kodi nanunso muli ndi wachibale amene anamwalira? N’kutheka kuti mwana wanu, mkazi kapena mwamuna wanu, mchimwene kapena mchemwali wanu, kapenanso mnzanu wa pamtima anamwalira. Ngati ndi choncho, kodi mungatani kuti muiwale?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena