Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g17 No. 6 tsamba 3
  • Kodi Zinthu Padzikoli Zafika Poipa Kwambiri Kapena Ayi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Zinthu Padzikoli Zafika Poipa Kwambiri Kapena Ayi?
  • Galamukani!—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Asayansi Asunthira Kutsogolo Wotchi Yosonyeza Nthawi ya Kutha kwa Dziko—Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nkhani Zina
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2012
  • Zimene Anthu Amaganiza Zokhudza Kutha kwa Dziko
    Galamukani!—2012
  • Kodi Kuopa Nyukiliya Kwatha?
    Galamukani!—1999
Onani Zambiri
Galamukani!—2017
g17 No. 6 tsamba 3
Wotchi Yosonyeza Nthawi ya Kutha kwa Dziko

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI ZINTHU PADZIKOLI ZAFIKA POIPA KWAMBIRI

Kodi Zinthu Padzikoli Zafika Poipa Kwambiri Kapena Ayi?

PAMENE chaka cha 2017 chinkayamba, gulu la akatswiri a sayansi linapereka uthenga wochititsa mantha. M’mwezi wa January, a sayansiwa analengeza kuti dziko lapansili latsala pang’ono kutha. Akatswiriwa ali ndi wotchi yongoyerekezera yosonyeza nthawi imene yatsala kuti dzikoli lithe ndipo anasunthira kutsogolo muvi wa maminitsi wa wotchiyi ndi masekondi 30. Wotchiyi ataikokera, inayamba kusonyeza kuti kwatsala 2 minitsi ndi hafu kuti nthawi ikwane 12 koloko ya usiku yomwe amati ikuimira nthawi yomwe dzikoli lidzathe. Panopa nthawiyi imaoneka yaifupi kwambiri poyerekeza ndi mmene inkaonekera chikhazikitsireni wotchiyi zaka zoposa 60 zapitazo.

Akatswiri asayansiwa akuganiza kuti mu 2018 adzaonenso kuti nthawi yoti dzikoli lithe yayandikira bwanji. Koma kodi wotchiyo idzawathandizadi kudziwa kuti dzikoli litha liti? Inuyo mukuganiza bwanji? Kodi zinthu padzikoli zafikiratu poipa kwambiri? Mwina mukuona kuti funsoli ndi lovuta kuyankha. Koma si inu nokha, ngakhalenso akatswiri ali ndi maganizo osiyana pa nkhaniyi chifukwa si onse omwe amakhulupirira kuti nthawi ina dzikoli lidzatha.

Pali anthu enanso ambiri omwe amaona kuti zinthu zidzakhala bwino mtsogolo. Anthuwa amanena kuti pali umboni woti anthufe komanso dzikoli lidzakhalapobe mpaka kalekale. Amanenanso kuti pa nthawiyo moyo wa anthu udzakhala wabwino kwambiri. Kodi umboni wa anthuwa ndi womveka? Kodi zinthu padzikoli zafikadi poipa kwambiri?

Magazini ina inanena kuti: “Wotchi Yosonyeza Nthawi ya Kutha kwa Dziko ndi yongoyerekezera ndipo inapangidwa ndi akatswiri asayansi a m’mayiko osiyanasiyana. Akatswiriwa anapanga wotchiyi n’cholinga chofuna kusonyeza nthawi yomwe yatsala kuti dzikoli liwonongeke chifukwa cha zochita za anthu. Chinthu choyambirira chomwe amaona kuti chingadzawononge dzikoli ndi mabomba a nyukiliya. Palinso zinthu zina zomwe anthu amachita kaya mwadala kapena mosadziwa zomwe zikuika dzikoli komanso moyo wa anthu pangozi. Zinthuzi ndi monga kusintha kwa nyengo, njira zamakono za ulimi ndi zachipatala komanso luso la zopangapanga.”​—Bulletin of the Atomic Scientists.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena