Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g20 No. 1 tsamba 14-15
  • N’zotheka Kudzakhala ndi Moyo Wopanda Nkhawa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’zotheka Kudzakhala ndi Moyo Wopanda Nkhawa
  • Galamukani!—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Nkhani Zimene Zili M’magaziniyi
    Galamukani!—2020
  • Zimene Tingachite Kuti Tisamapanikizike Kwambiri
    Galamukani!—2010
  • Ufumu wa Mulungu Ukamadzalamulira “Padzakhala Mtendere Wochuluka”
    Galamukani!—2019
  • Kupanikizika Maganizo Kwabwino ndi Koipa
    Galamukani!—1998
Onani Zambiri
Galamukani!—2020
g20 No. 1 tsamba 14-15
Kamnyamata ndi bambo ake akulumphira m’madzi kunyanja ndipo mayi ndi mwana wamkazi akuonerera kumtunda.

MUNGATANI KUTI MUCHEPETSE NKHAWA?

N’zotheka Kudzakhala ndi Moyo Wopanda Nkhawa

Mfundo za m’Baibulo zingatithandize kuti tisamakhale ndi nkhawa zosafunikira kwenikweni. Ndi zoona kuti patokha sitingathetseretu zinthu zomwe zimatidetsa nkhawa. Koma Mulungu ali ndi mphamvu yochita zimenezi. Iye anasankha Yesu Khristu kuti adzatichotsere zinthu zonse zomwe zimatipangitsa kukhala ndi nkhawa. Posachedwapa, Yesu adzachita zinthu zambiri zodabwitsa padziko lonse kuposa zimene anachita m’mbuyomu. Mwachitsanzo, iye adzachita zotsatirazi:

ADZACHIRITSA ODWALA NGATI MMENE ANACHITIRA ALI PADZIKOLI.

“Anthu anamubweretsera onse amene anali . . . kuvutika ndi matenda komanso zowawa zamitundumitundu . . . ndipo iye anawachiritsa.”​—MATEYU 4:24.

ADZAPEREKA NYUMBA KOMANSO CHAKUDYA KWA ONSE.

“Iwo [olamuliridwa ndi Yesu] adzamanga nyumba n’kukhalamo. Adzabzala minda ya mpesa n’kudya zipatso zake. Sadzamanga wina n’kukhalamo. Sadzabzala wina n’kudya.”​—YESAYA 65:21, 22.

ULAMULIRO WAKE UDZABWERETSA MTENDERE NDI CHITETEZO PADZIKO LONSE.

“M’masiku ake, wolungama adzaphuka, ndipo padzakhala mtendere wochuluka kwa nthawi yonse pamene mwezi udzakhalepo. Ndipo adzakhala ndi anthu omugonjera kuchokera kunyanja kukafika kunyanja, komanso kuchokera ku mtsinje kukafika kumalekezero a dziko lapansi. . . . Ndipo adani ake adzabwira fumbi.”​—SALIMO 72:7-9.

ADZATHETSA ZOPANDA CHILUNGAMO.

“Adzamvera chisoni munthu wonyozeka ndi wosauka, ndipo adzapulumutsa miyoyo ya anthu osauka. Adzawombola miyoyo yawo ku chipsinjo ndi chiwawa.”​—SALIMO 72:13, 14.

ADZATHETSANSO MAVUTO NDI IMFA

“Imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulira, kapena kubuula, ngakhale kupweteka.”​—CHIVUMBULUTSO 21:4.

“NTHAWI ZOWAWITSA”

Mkonzi wamkulu wa nyuzipepala ya Gallup, a Mohamed S. Younis ananena kuti: “Anthu ambiri masiku ano ndi okhumudwa, ali ndi nkhawa kwambiri komanso akuvutika kuposa kale lonse.”

N’chifukwa chiyani anthu ambiri akuvutika ndi nkhawa chonchi? Baibulo limapereka yankho logwira mtima la funso limeneli. Pa 2 Timoteyo 3:1, pamati: “Masiku otsiriza zidzafika nthawi zowawitsa.” (Buku Lopatulika) Baibuloli limafotokoza chifukwa chake masikuwa adzakhale owawitsa kapena ovuta. Limanena kuti m’masiku amenewa anthu adzakhala ndi makhalidwe oipa monga kukonda ndalama, kudzitamandira, kukhala ndi maonekedwe achipembedzo, achiwembu, opanda chikondi chachibadwidwe komanso osadziletsa. (2 Timoteyo 3:2-5) Masiku otsirizawa adzatha Yesu Khristu akadzayamba kulamulira dziko lapansili monga Mfumu.​—Danieli 2:44.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena