Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 115
  • Paradaiso Watsopano pa Dziko

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Paradaiso Watsopano pa Dziko
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • “Iwe Udzakhala ndi Ine m’Paradaiso”
    Kumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
  • Kodi Ndani Adzauka kwa Akufa? Nanga Adzakhala Kuti?
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • Kodi Chifuno cha Mulungu cha Dziko Lapansi N’chiyani?
    Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
  • “Tidzaonana M’Paradaiso”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 115

NKHANI 115

Paradaiso Watsopano pa Dziko

TAONANI mitengo yaitali, maluwa okongola ndi mapiri atali. Kodi pano si pokongola? Onani m’mene mbawala ikudyera m’manja mwa kamnyamata’ko. Onani mikango ndi akavalo aima uko pa dambo’wo. Kodi mungakonde kukhala m’nyumba yokhala pa malo otere?

Mulungu amafuna kuti mukhale ndi moyo kosatha pa dziko lapansi m’paradaiso. Samafuna kuti ali yense akhale ndi zopweteka ndi zowawa zimene anthu amabvutika nazo lero lino. Iri ndiro lonjezo la Baibulo kwa awo amene adzakhala ndi moyo m’paradaiso watsopano: ‘Mulungu adzakhala nawo. Sipadzakhala’nso imfa kapena kulira kapena chowawa. Zinthu zakale zapita.’

Yesu adzatsimikizira kuona kuti kusintha kodabwitsa’ku kwachitika. Kodi mukudziwa kuti zidzachitika liti? Inde, atachotsera dziko kuipa konse ndi anthu oipa. Pajatu, ali pa dziko lapansi Yesu anachiritsa matenda a mtundu uli wonse a anthu, ndipo iye anaukitsa’nso akufa. Anachita izi kusonyeza zimene adzachita pa dziko lonse akadzakhala Mfumu ya ufumu wa Mulungu.

Ganizirani m’mene kudzakhalira kodabwitsa m’paradaiso watsopano wa pa dziko lonse’yo! Yesu, ndi ena amene iye akuwasankha, adzalamulira ali kumwamba. Olamulira’wo adzasamalira ali yense pa dziko lapansi ndi kuona kuti iwo ali okondwa. Tiyeni tione chimene tifunikira kuchita kuti titsimikizire kuti Mulungu adzatipatsa moyo wosatha m’paradaiso wake watsopano.

Chibvumbulutso 21:3, 4; 5:9, 10; 14:1-3.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena