Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 35
  • Yehova Apereka Malamulo Ake

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Apereka Malamulo Ake
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Analonjeza Kuti Azimvera Yehova
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Phunzirani Njira za Yehova
    Nsanja ya Olonda—2005
  • Chitsamba Choyaka Moto
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Mmene Moyo wa Mose Umakukhudzirani
    Galamukani!—2004
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 35

NKHANI 35

Yehova Apereka Malamulo Ake

PAFUPI-FUPI miyezi iwiri atatuluka mu Igupto, Aisrayeli akufika pa Phiri la Sinai, limene likuchedwa’nso Horebi. Ndi pa malo omwewa pamene Yehova analankhulapo ndi Mose m’chitsamba choyaka moto. Anthu anamanga mahema pano nakhalapo kwa kanthawi.

Anthu akuyembekezera pansipo, Mose akukwera m’phirimo. Pamwambapo, Yehova akuuza Mose kuti Iye akufuna kuti Aisrayeli amvere Iye ndi kukhala anthu Ake apadera. Pamene Mose akutsika, akuuza Aisrayeli zimene Yehova wanena. Anthu’wo akuti adzamvera Yehova, chifukwa akufuna kukhala anthu ake.

Yehova tsopano akuchita chinthu chodabwitsa. Akuchititsa pamwamba pa phiri’lo kuchita utsi, ndi mphezi. Iye akulankhula’nso ndi anthu’wo kuti: ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene anakutulutsani m’dziko la Igupto.’ Nawalamula kuti: ‘Musamalambira milungu ina koma ine ndekha.’

Iye akupatsa Aisrayeli malamulo ena asanu ndi anai. Anthu’wo akuopa kwambiri. Iwo akuuza Mose kuti: ‘Inu mulankhule nafe, chifukwa tiopa kuti ngati Mulungu alankhula nafe tingafe.’

Kenako Yehova akuuza Mose kuti: ‘Kwera ku phiri kuno. Ndidzakupatsa miyala iwiri yaphanthi-panthi imene ndalembapo malamulo amene ndikufuna kuti anthu awasunge.’ Chotero Mose akukwera’nso ku phiri. Akukhalako kwa mausana ndi mausiku 40.

Mulungu ali ndi malamulo ochuluka kwambiri kaamba ka anthu ake. Mose akulemba malamulo’wa. Mulungu akum’patsa’nso miyala iwiri’yo. Mulungu mwini walembapo malamulo 10 amene iye ananena ndi anthu onse. Iwo akuchedwa Malamulo Khumi.

Iwo ali malamulo ofunika. Chimodzi-modzi’nso malamulo ena ambiri’wo amene Mulungu anapatsa Israyeli. Limodzi la malamulo’wa ndiro: ‘Udzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, maganizo ako onse, moyo wako wonse ndi nyonga yako yonse.’ Lina ndiro: ‘Udzikonda mnansi wako monga momwe umadzikondera.’ Mwana wa Mulungu, Yesu Kristu, anati awa ndiwo malamulo awiri akulu kopambana amene Yehova anapatsa anthu ake Israyeli. Kenako tidzaphunzira zinthu zambiri ponena za Mwana wa Mulungu ndi ziphunzitso zake.

Eksodo 19:1-25; 20:1-21; 24:12-18; 31:18; Deuteronomo 6:4-6; Levitiko 19:18; Mateyu 22:36-40.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena