Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 67
  • Yehosafati Adalira Yehova

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehosafati Adalira Yehova
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Anathandiza Mfumu Yehosafati
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kodi Mumatsatira ndi Mtima Wonse Zimene Zinalembedwa?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Muziona Ena Mmene Yehova Amawaonera
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Tizitumikira Yehova ndi Mtima Wathunthu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 67

NKHANI 67

Yehosafati Adalira Yehova

KODI mukudziwa amuna’wa ndi zimene iwo akuchita? Iwo akumka ku nkhondo, ndipo amuna ali patsogolo’wo akuyimba. Koma mungafunse kuti: ‘Nchifukwa ninji oyimba’wo alibe malupanga ndi mikondo zomenyera nkhondo?’ Tiyeni tione.

Yehosafati ndiye mfumu ya ufumu wa mafuko awiri wa Israyeli. Iye akukhala ndi moyo pa nthawi imodzi-modzi ndi Mfumu Ahabu ndi Yezebeli ya ufumu wakumpoto wa mafuko 10. Koma Yehosafati ndi mfumu yabwino, ndipo atate wake Asa anali’nso mfumu yabwino kwambiri. Kwa zaka zambiri anthu a ufumu wakumwela wa mafuko awiri analinkukhala bwino.

Komano kanthu kena kakuchitika kochititsa anthu’wo mantha. Amithenga akusimbira Yehosafati kuti: ‘Gulu la nkhondo lalikulu lochokera ku maiko a Moabu, Amoni, ndi Phiri la Seiri akudza kudzakuukirani.’ Aisrayeli ambiri akusonkhana pa Yerusalemu kudzafuna chithandizo cha Yehova. Akumka ku kachisi, kumene’ko Yehosafati akupemphera kuti: ‘O Yehova Mulungu wathu, sitikudziwa chochita. Tathedwa nzeru ndi gulu la nkhondo lalikulu’li. Tikuyang’ana kwa inu kaamba ka chithandizo.’

Yehova akumvetsera, ndipo akutuma mmodzi wa atumiki ake kuuza anthu’wo kuti: ‘Nkhondo’yi si yanu, koma ya Mulungu. Simudzamenya. Ingopenyani, muone m’mene Yehova adzakupulumutsirani.’

Tsono m’mawa mwake Yehosafati akuwauza kuti: ‘Dalirani Yehova!’ Ndiyeno akuika oyimba patsogolo pa ankhondo’wo, ndipo pamene akuguba akuyimba zitamando kwa Yehova. Kodi mukudziwa chimene chikuchitika poyandikira ku nkhondo’ko? Yehova akuchitititsa ankhondo a adani’wo kumenyana okha-okha. Pofika iwo, wankondo ali yense wa adani’wo wafa!

Kodi sikunali kwanzeru kwa Yehosafati kudalira Yehova? Tidzakhala anzeru tikadalira Yehova.

1 Mafumu 22:41-53; 2 Mbiri 20:1-30.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena