Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 75
  • Anyamata Anai m’Babulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anyamata Anai m’Babulo
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Anyamata 4 Amene Anamvera Yehova
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Ayesedwa—Koma Akhulupirikabe kwa Yehova!
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Chikhulupiriro Chawo Chinapulumuka Chiyeso Choopsa
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Danieli
    Nsanja ya Olonda—2007
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 75

NKHANI 75

Anyamata Anai m’Babulo

MFUMU Nebukadinezara akutenga Aisrayeli onse ophunzira bwino kwambiri kumka nawo ku Babulo. Kenako mfumu ikusankha pakati pao anyamata okongola ndi ochenjera kopambana. Anai a amene’wa ndiwo anyamata mukuwaona apa’wa. Mmodzi’yo ndi Danieli, ndipo atatu ena’wo Ababulo akuwacha Sadrake, Mesake ndi Abedinego.

Nebukadinezara akulinganiza kuphunzitsa anyamata’wo kuti atumikire m’mphala yake. Pambuyo pa zaka zitatu za kuphunzitsidwa iye adzangosankhapo ochenjera kopambana onse kum’thandiza kuthetsa zobvuta. Mfumu ikufuna kuti anyamata’wo akhale amphamvu ndi athanzi m’kati mwa kuphunzitsidwa kwao. Chotero ikulamula kuti awapatse zakudya zabwino zofanana’zo zimene iye amadya ndi banja lake.

Taonani Danieli’yo. Kodi mukudziwa zimene akunena ndi mtumiki wamkulu wa mfumu’yo Asipenazi? Akumuuza kuti sakufuna kudya zakudya zabwino za pa gome la mfumu. Koma Asipenazi akudera nkhawa. ‘Mfumu ndiyo imene yanena zimene muzidya ndi kumwa,’ akutero. ‘Ndipo ngati simuoneka muli athanzi monga anyamata ena’wo, angandiphe.’

Chotero Danieli akumka kwa wom’yang’anira woikidwa ndi Asipenazi limodzi ndi mabwenzi ake atatu’wo. ‘Chonde tiyeseni kwa masiku 10,’ akutero. ‘Tipatseni zomera tidye ndi madzi timwe. Ndiyeno mutiyerekezere ndi anyamata ena odya chakudya cha mfumu, ndi kuona amene akuoneka bwino.’

Woyang’anira’yo akubvomereza kuchita izi. Pakutha kwa masiku 10, Danieli ndi anzake atatu’wo akuoneka kukhala athanzi kwambiri koposa anyamata ena onse’wo. Chotero woyang’anira’yo akuwalola kumangodya zomera m’malo mwa zimene mfumu imapereka.

Zitatha zaka zitatu anyamata’wo akutengeredwa kwa Nebukadinezara. Pambuyo pa kulankhula nawo onse, mfumu ikuona Danieli ndi mabwenzi ake atatu kukhala koposa onse. Chotero akuwatenga kum’thandiza m’mphala yake. Ndipo pali ponse pamene iyo ifunsa Danieli, Sadrake, Mesake ndi Abedinego mafunso kapena kuwapatsa chothetsa nzeru, iwo akudziwa nthawi 10 koposa ali yense wa ansembe ake kapena anzeru.

Danieli 1:1-21.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena