Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 100
  • Yesu m’Munda

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu m’Munda
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Kuperekedwa ndi Kugwidwa
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Khristu Anaperekedwa Kenako Anamangidwa
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Kuperekedwa ndi Kugwidwa
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Yesu Anamangidwa
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 100

NKHANI 100

Yesu m’Munda

ATACHOKA m’chipinda chapamwamba’cho, Yesu ndi atumwi ake akumka ku munda wa Getsemane. Iwo akhala akudza kuno nthawi zambiri. Yesu akuwauza kukhala maso ndi kupemphera. Ndiyeno akumka cha apo, nawerama pansi napemphera.

Kenako Yesu akudza kumene kuli atumwi ake. Kodi muganiza akuchitanji? Ali mtulo! Katatu Yesu akuwauza kuti ayenera kukhala maso, koma nthawi iri yonse imene akubwerera akuwapeza ali mtulo. ‘Kodi mungagone bwanji pa nthawi yonga ino?’ akutero Yesu pa nthawi yotsiriza imene iye akubwerera. ‘Nthawi yakwana yakuti ndiperekedwe kwa adani anga.’

Pa nthawi yomwe’yo phokoso la khamu lalikulu likumveka. Onani! Amuna’wo akudza ndi malupanga ndi zibonga! Ndipo anyamula nyali zowaunikira. Pofika pafupi, wina akutuluka m’khamu’lo nadza kwa Yesu. Akumpsyomsyona, monga momwe mukuonera pano. Munthu’yu ndiye Yudasi Isikariote! Kodi akupsompsyoneranji Yesu?

Yesu akum’funsa kuti: ‘Yudasi, kodi ukundipereka mwa kupsyompsyona? Inde, kupsyompsyona’ko ndiko chizindikiro. Kukudziwitsa amuna’wo kuti uyu ndiye Yesu, munthu amene iwo akufuna. Chotero adani’wo akudza nam’gwira. Koma Petro sakuwalola kutenga Yesu popanda nkhondo. Iye akusolola lupanga limene wadza nalo nakantha nalo munthu wokhala chifupi naye. Lupanga’lo langophonya mutu wa munthu’yo nalingodula khutu lakumanja. Koma Yesu akukhudza khutu la munthu’yo nalichiza.

Yesu akuuza Petro kuti: ‘Bwezera lupanga lako m’chimake. Kodi suganiza kuti ndingapemphe Atate wanga zikwi za angelo kudzandipulumutsa?’ Inde, angathe! Koma iye sakupempha Mulungu kutumiza angelo ali onse, chifukwa iye akudziwa kuti nthawi yakwana yakuti adani ake am’gwire. Chotero akuwalola kum’tenga. Tiyeni tione zimene zikuchitikira Yesu tsopano.

Mateyu 26:36-56; Luka 22:39-53; Yohane 18:1-12.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena