Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Mumadziwa Zotani pa Nkhani ya Fodya?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
    • Mutu 33

      Kodi Mumadziwa Zotani pa Nkhani ya Fodya?

      Onani zimene zalembedwa kumanjaku ndipo ikani chizindikiro ichi ✔ pa mawu amene akufotokoza zimene zimakuchititsani inuyo kufuna kusuta fodya.

      □ Ndimafuna kulawa

      □ Ndikufuna ndichepetse nkhawa

      □ Ndikufuna kuti anzanga asamandisale

      □ Ndikufuna ndichepetse thupi

      NGATI mwachonga pa bokosi lililonse patsamba 237, ndiye kuti mukufanana ndi achinyamata ena omwe amasuta fodya kapena amafuna atayamba kusuta.a Mwachitsanzo:

      Kufuna kulawa. “Ndinkafuna kudziwa kuti fodya amakoma bwanji ndiye tsiku lina mtsikana wina wa kusukulu kwathu atandigayira ndudu imodzi ndinalandira kenako n’kutuluka panja kukasuta.”​—Anatero Tracy.

      Kuchepetsa nkhawa komanso kufuna kuti anthu ena asamakusale. “Ana ambiri a kusukulu kwathu ankanena kuti kusuta kumawathandiza kuti asamakhale ndi nkhawa, ndiye nanenso ndikakhala ndi nkhawa ndinkalakalaka kusuta.”​—Anatero Nikki.

      Kuchepetsa thupi. “Atsikana ena amasuta kuti asanenepe. Njira imeneyi imaoneka yophweka poyerekeza ndi kuchepetsa zimene umadya.”​—Anatero Samantha.

      Koma musanayatse ndudu yanu, kaya mukuyamba kumene kapena mwakhala mukusuta m’mbuyomu, ndi bwino kuganiza kaye mofatsa. Musakhale ngati nsomba imene ikufuna kudya chinthu choti chili kumbedza. N’zoona kuti nsombayo idyadi chinthu chimene ikufunacho koma pamapeto pake ifa. M’malo mochita zimenezi, tsatirani malangizo a m’Baibulo ndipo muzigwiritsa ntchito “mphamvu zanu zotha kuganiza bwino.” (2 Petulo 3:1) Yankhani mafunso otsatirawa.

      Kodi Zimene Mumadziwa pa Nkhani ya Fodya N’zolondola?

      Chongani ziganizo zili m’munsizi kuti ndi zoona kapena zabodza.

      a. Kusuta kukhoza kuchepetsa nkhawa imene ndimakhala nayo.

      □ Zoona □ Zabodza

      b. Ndikamasuta palibe utsi umene umatsala m’thupi.

      □ Zoona □ Zabodza

      c. Panopa kusuta sikungasokoneze thanzi langa mpaka nditakalamba.

      □ Zoona □ Zabodza

      d. Kusuta kungachititse kuti anyamata kapena atsikana azindigomera.

      □ Zoona □ Zabodza

      e. Mavuto amene angabwere chifukwa chosuta adzakhudza ine ndekha.

      □ Zoona □ Zabodza

      f. Mulungu alibe nazo ntchito ngati nditayamba kusuta kapena ayi.

      □ Zoona □ Zabodza

      Mayankho

      a. Zabodza. Ngakhale kuti kusuta kumachepetsa pang’ono nkhawa imene munthu amakhala nayo akangosiya kusuta, asayansi apeza kuti kusuta kumawonjezera nkhawa.

      b. Zabodza. Kafukufuku amasonyeza kuti zinthu zambiri zimene zimakhala mu utsi wa fodya zimatsalira m’thupi.

      c. Zabodza. Ndi zoona kuti mavuto ambiri amawonjezeka ngati munthu wakhala akusuta kwa nthawi yaitali komabe pali mavuto ena amene amayamba kuonekera nthawi yomweyo. Anthu ena akangosuta ndudu imodzi amakomedwa moti safunanso kusiya. Kusuta kumapangitsanso kuti mapapo azikanika kukoka mpweya wokwanira mukamapuma komanso mukhoza kuyamba kudwala chifuwa chosatha. Khungu lanu likhoza kuyamba makwinya zomwe zingachititse kuti mukalambe msanga. Kusuta kukhoza kuchititsa kuti musamathe kugonana, muzikhala ndi mantha komanso kuti muzivutika maganizo.

      d. Zabodza. Katswiri wina wofufuza zinthu, dzina lake Lloyd Johnston, anapeza kuti “anyamata ndi atsikana ambiri sakopeka” ndi achinyamata amene amasuta.

      e. Zabodza. Chaka chilichonse, anthu ambiri amafa chifukwa cha utsi wochokera kwa munthu yemwe akusuta fodya. Utsiwo ukhoza kupha anthu a m’banja la munthu wosutayo ngakhalenso anzake.

      f. Zabodza. Amene amafuna kusangalatsa Mulungu sayenera kuchita “chinthu chilichonse choipitsa thupi.” (2 Akorinto 7:1) Palibe amene angatsutse zoti kusuta kumawononga thupi. Ngati mutasankha kuti muipitse thupi lanu komanso kuvulaza anthu ena chifukwa chosuta fodya, simungakhale bwenzi la Mulungu.​—Mateyu 22:39; Agalatiya 5:19-21.

      Zimene Mungayankhe Ngati Wina Atakunyengererani

      Ndiye kodi mungatani ngati winawake atakupatsani fodya kuti musute? Kuyankha mwachidule koma motsimikiza kukhoza kuthandiza. Mukhoza kumuyankha kuti “Pepani, sindimasuta.” Ngati munthuyo akukukakamizani kapenanso atayamba kukunenani, kumbukirani kuti kukana kusuta fodya ndi ufulu wanu. Mukhoza kumuuza kuti:

      ● “Ndimadziwa kuti fodya ndi woipa chifukwa akhoza kuwononga thanzi la munthu ndiye sindimasuta.”

      ● “Sindikufuna kufa msanga, ndili ndi zambiri zoti ndichite kutsogoloku.”

      ● “Kodi m’mesa ndili ndi ufulu wosankha zimene ndikufuna?”

      Koma mofanana ndi achinyamata amene afotokoza maganizo awo kumayambiriro kwa nkhaniyi, zikhoza kutheka kuti mtima wanu ndi umene ukulakalaka kwambiri kusuta fodya. Ngati zili choncho, kuganizira mafunso otsatirawa kukhoza kukuthandizani kulimbana ndi maganizo amenewa:

      ● ‘Kodi ndikasuta ndipindula chilichonse? Mwachitsanzo, ngati nditasuta n’cholinga choti anzanga asamandisale, kodi anzangawo angamandikondedi chabe chifukwa chakuti tonse timasuta? Ndipo kodi ndingafune kumagwirizana ndi anthu amene angasangalale kundiona ndikuwononga moyo wanga?’

      ● ‘Kodi ndingawononge ndalama zambiri bwanji pogula fodya komanso polipirira kuchipatala nditayamba kudwala naye? Komanso kodi ndingalole kuti anthu asiye kundilemekeza chifukwa chakuti ndimasuta?’

      ● ‘Kodi ndingalole kuwononga ubwenzi wanga ndi Mulungu chifukwa chosuta?’

      Koma kodi mungatani ngati munayamba kale kusuta ndipo mukukanika kusiya?

      Zimene Zingakuthandizeni Kuti Musiye

      1. Tsimikizani. Lembani zifukwa zimene mukusiyira ndipo muziona zimene mwalembazo pafupipafupi. Kukhala ndi cholinga choti Mulungu azikuonani kuti ndinu woyera kungakuthandizeni kwambiri kuti muziyesetsa kupewa kusuta.​—Aroma 12:1; Aefeso 4:17-19.

      2. Pemphani thandizo. Ngati mwakhala mukusuta mobisa, panopa ndi nthawi yabwino yoti muwauze ena kuti akuthandizeni. Auzeni anthu amene mwakhala mukuwabisirawo kuti mukufunitsitsa kusiya kusuta ndipo apempheni kuti akuthandizeni. Ngati mukufuna kutumikira Mulungu, m’pempheni kuti akuthandizeni.​—1 Yohane 5:14.

      3. Sankhani tsiku limene mukufuna kusiya. Mukamasankha tsiku loti mudzasiye kusuta, ndi bwino kusankha tsiku lakutsogolo kutatsala milungu iwiri kapena kucheperapo kuti lifike. Lembani detilo pakalendala yanu ndipo muuze abale anu komanso anzanu zoti mudzasiya kusuta pa tsiku limenelolo.

      4. Fufuzani ndi kutaya zinthu zonse zosafunika. Tsiku limene mwasankha kuti mudzasiye kusuta lisanafike, fufuzani mosamala kuchipinda kwanu, m’galimoto komanso m’zovala zanu ngati muli fodya aliyense wotsala. Mukamupeza m’tayeni ndipo tayaninso malaitala komanso zinthu zonse zimene mumagwiritsa ntchito posuta. Mungachite bwinonso kusiya zoyenda ndi machesi.

      5. Pezani njira yothetsera mavuto omwe amabwera mukangosiya kumene. Muzimwa madzi ambiri kapena juwisi komanso muzigona mokwanira. Musamaiwale kuti mavuto amene mungakumane nawo chifukwa chosiya kusuta ndi akanthawi chabe, pamene mapindu amene mungapeze adzakhalapo mpaka kalekale.

      6. Muzipewa zinthu zimene zingakupangitseni kufuna kusuta. Muzipewa kukhala pamalo kapena zochitika zimene zingakupangitseni kusuta. Zingakhalenso bwino ngati mutasiya kucheza ndi anthu amene amasuta.​—Miyambo 13:20.

      Musapusitsike Ndi Anthu Ena

      Chaka chilichonse, makampani ogulitsa fodya amawononga ndalama zambiri poitanira malonda awo. Kodi amafuna kukopa ndani kwenikweni? Kalata ina imene anthu ogwira ntchito pa kampani inayake ya fodya analemberana inali ndi mawu akuti: “Achinyamata a masiku ano akhoza kudzakhala makasitomala abwino a fodya. Choncho tikufunika kuyesetsa kuwakopa kuti ayambe kusuta.”

      Musalole kuti ndalama zanu zipite kwa anthu opanga fodya. Musakopeke ndi zochita zawo chifukwa iwowo komanso achinyamata anzanu amene amasuta samaganizira za moyo wanu. Choncho m’malo momvera zonena zawo, mungachite bwino kumvera malangizo a m’Baibulo kuti “zinthu zikuyendereni bwino.”​—Yesaya 48:17.

      M’MUTU WOTSATIRA

      Kodi anzanu amakunyengererani kuti mumwe mowa? Werengani nkhaniyi kuti mudziwe kufunika kokhala ndi malire a kuchuluka kwa mowa umene mungamwe.

      [Mawu a M’munsi]

      a Ngakhale kuti nkhaniyi ikufotokoza za anthu omwe amasuta, mavuto amene atchulidwa angachitikenso kwa munthu amene fodyayo amachita kutafuna.

      LEMBA

      “Tiyeni tidziyeretse ndipo tichotse chinthu chilichonse choipitsa thupi.”​—2 Akorinto 7:1.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      Ngati mwasiya kusuta, musamaganize kuti kusuta ndudu imodzi yokha si nkhani. Maganizo amenewa angachititse kuti muyambirenso.​—Yeremiya 17:9.

      KODI MUKUDZIWA . . . ?

      Munthu amene amagwiritsa ntchito fodya mosachita kusuta, mwachitsanzo kuchita kutafuna amakhala ndi poizoni wambiri m’thupi mwake wotchedwa nicotine kuposa munthu amene amachita kusuta. Kugwiritsa ntchito fodya mwa njira ngati imeneyi kukhoza kuchititsanso kuti poizoni woyambitsa khansa amene amapezeka mu fodya alowe m’thupi mwake ndipo akhoza kudwala khansa yapakhosi komanso yam’kamwa.

      ZOTI NDICHITE

      Ngati mnzanga wakusukulu atandinyengerera kuti ndisute fodya ndidzachita izi: ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pa nkhaniyi ․․․․․

      KODI INUYO MUKUGANIZA BWANJI?

      ● N’chifukwa chiyani n’zotheka munthu kulakalaka kuyamba kusuta ngakhale akudziwa kale mavuto ake?

      ● N’chiyani chikukupangitsani kuona kuti kusuta n’koopsa?

      [Mawu Otsindika patsamba 240]

      “Munthu wina akamandipatsa fodya, ndimangomwetulira n’kumuuza kuti, ‘Pepani, sindikufuna kudwala khansa.”​—Anatero Alana

      [Bokosi/​Chithunzi patsamba 241]

      Kodi N’zoona Kuti Chamba N’choipa?

      Ellen, yemwe amakhala ku Ireland, ananena kuti: “Anthu ena amanena kuti kusuta chamba kumathandiza kuti uiwaleko mavuto ndipo chamba sichiyambitsa mavuto alionse.” Kodi munamva anthu ena akunena zofanana ndi zimenezi? M’munsimu muli zinthu zabodza zimene anthu amanena pa nkhaniyi komanso zoona zake.

      Zomwe Ena Amanena. Chamba si choopsa.

      Zoona Zake. Zinthu zina zimene munthu wosuta chamba amadzavutika nazo mpaka kalekale ndi izi: Amaiwalaiwala, amavutika kuphunzira zinthu, thupi lake limakanika kulimbana ndi matenda komanso amuna ndi akazi omwe sakhala ndi mphamvu kuchipinda. Chamba chimachititsanso munthu kuvutika ndi nkhawa komanso mutu wake sugwira. Ana amene amabadwa kwa mayi amene amasuta chamba nthawi zambiri amakhala ovutitsa, amavutika kwambiri posankha zinthu komanso sakhala ndi chidwi pophunzira.

      Zomwe Ena Amanena. Utsi wa chamba si woopsa ngati utsi wa fodya.

      Zoona Zake. Tikayerekeza utsi wa fodya ndi utsi wa chamba, utsi wa chamba umawononga kwambiri m’mene mumadutsa mpweya komanso umakhala ndi poizoni wambiri yemwe amalowa m’magazi. Poizoni amene amapezeka mu ndudu 5 za chamba, ndi wochuluka mofanana ndi poizoni amene angapezeke mupaketi yonse ya fodya wamba.

      Zomwe Ena Amanena. Chamba sichivuta kusiya.

      Zoona Zake. Nthawi zambiri achinyamata amene amavutika maganizo amati akayamba kusuta chamba zimawavuta kuti asiye. Ena amavutika kusiya ngati akhala akusuta kwa nthawi yaitali. Kafukufuku amasonyezanso kuti achinyamata ambiri amene amasuta chamba, m’kupita kwa nthawi amayambanso kugwiritsa ntchito mankhwala ena osokoneza bongo, ngati cocaine, omwe amavuta kusiya.

      [Bokosi/​Chithunzi patsamba 244, 245]

      Thupi la Munthu Wosuta Fodya

      Yerekezerani zithunzi za anthu a thanzi omwe amasonyezedwa potsatsa malonda a fodya ndi zithunzi zomwe zikusonyeza zimene zimachitikadi m’thupi la munthu wosuta fodya.

      M’kamwa ndi pakhosi Umatha kudwala khansa

      [Chithunzi]

      Khansa ya palilime

      Mtima Mitsempha yodutsa magazi imayamba kulimba komanso kutsekeka, zomwe zimachititsa kuti mumtima musamafike mpweya wokwanira ndipo munthuyo akhoza kudwala matenda a mtima mosavuta

      [Chithunzi]

      Mtsempha woti wayamba kutsekeka

      Mapapo Fodya amawononga malo osungira mpweya m’mapapo, amatupitsa njira zimene mpweya umadutsa komanso n’zosavuta kuti munthuyo adwale khansa ya m’mapapo

      [Chithunzi]

      Mapapo a munthu wosuta fodya

      Ubongo N’zosavuta kuti munthu wosuta fodya adwale matenda opha ziwalo

      Khungu Munthu amakalamba msanga

      Mano amasintha mtundu

      M’mimba Fodya amayambitsa khansa

      Kapamba Fodya amayambitsa khansa

      Chikhodzodzo Fodya amayambitsa khansa

      Impso Fodya amayambitsa khansa

      [Chithunzi patsamba 239]

      Mofanana ndi nsomba imene imadya chinthu choti chili kumbedza, munthu amene amasuta amamva bwino kwa kanthawi koma pamapeto pake amakumana ndi mavuto oopsa

  • Kodi Kumwa Mowa Wambiri Kuli Ndi Vuto Lanji?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
    • Mutu 34

      Kodi Kumwa Mowa Wambiri Kuli Ndi Vuto Lanji?

      Kodi mungayankhe bwanji mafunso otsatirawa? Ikani chizindikiro ichi ✔ pamene pali yankho logwirizana ndi lanu.

      Kodi anzanu amamwa mowa kwambiri kapena amamwa mowa ngakhale kuti sanafike pa msinkhu woyenerera?

      □ Inde □ Ayi

      Kodi anzanu anayamba akunyengereranipo kuti mumwe mowa?

      □ Inde □ Ayi

      Kodi munayamba mwamwapo mowa wambiri?

      □ Inde □ Ayi

      KODI tingasiyanitse bwanji kumwa mowa ndi kumwa mowa wambiri? Anthu ena amanena kuti kumwa mowa wambiri ndi kumwa n’cholinga choti uledzere. Lipoti la bungwe lina la ku United States, linachita kutchula nambala ya mabotolo omwe munthu atamwa tinganene kuti wamwa mowa wambiri. (U.S. National Institute on Alcohol Abuse and Alcoholism) Linanena kuti “ngati mwamuna wamwa molumikiza mabotolo 5 kapena kuposa komanso ngati mkazi wamwa mabotolo 4 kapena kuposa,” ndiye kuti wamwa mowa wambiri.

      Ngati munayamba mwamwapo mowa wambiri kapena kumwa mowa musanafike msinkhu wovomerezeka ndi boma, dziwani kuti simuli nokha. Achinyamata ambiri amamwa mowa mopitirira muyezo.a Koma dzifunseni kuti, ‘Kodi ndikudziwa chimene chikundichititsa kuti ndiyambe mowa? Nanga ndikudziwa mavuto amene ndingakumane nawo ngati nditayamba mowa?’ Mwachitsanzo, kodi mungayankhe bwanji mafunso otsatirawa? Ikani chizindikiro ichi ✔ pamene pali yankho logwirizana ndi lanu, kenako ganizirani mayankho olondola omwe ali m’munsi mwakemo.

      a. Achinyamata amamwa chifukwa chakuti umawakomera.

      □ Zoona □ Zabodza

      b. Chifukwa chakuti achinyamata amakhala ndi mphamvu komanso thanzi labwino, sangakumane ndi mavuto ena amene anthu akuluakulu amakumana nawo chifukwa chomwa mowa wambiri.

      □ Zoona □ Zabodza

      c. Munthu sungafe chifukwa chomwa mowa wambiri.

      □ Zoona □ Zabodza

      d. Baibulo limaletsa kumwa mowa.

      □ Zoona □ Zabodza

      e. Vuto lokha limene ungakumane nalo ngati umamwa mowa wambiri ndi kudwaladwala basi.

      □ Zoona □ Zabodza

      a. Achinyamata amamwa chifukwa chakuti umawakomera. Yankho​—Zabodza. Pa kafukufuku amene anachitika ku Australia, anapeza kuti achinyamata 36 pa 100 alionse amene anafunsidwa, amamwa mowa n’cholinga choti asamaoneke otsalira pa nthawi ya zisangalalo. Pa kafukufuku wina amene anachitika ku United States anapeza kuti achinyamata 66 pa 100 alionse amamwa pongotengera anzawo. Komabe, achinyamata ambiri ananenanso kuti amamwa n’cholinga choti aiwale mavuto.

      b. Chifukwa chakuti achinyamata amakhala ndi mphamvu komanso thanzi labwino, sangakumane ndi mavuto ena amene anthu akuluakulu amakumana nawo chifukwa chomwa mowa wambiri. Yankho​—Zabodza. Magazini ina inanena kuti: “Kafukufuku amene wachitika posachedwapa akusonyeza kuti achinyamata amene amamwa mowa akuputa dala mavuto.” Kodi ananena zimenezi chifukwa chiyani? Chifukwa “achinyamata amene amamwa mowa kwambiri ubongo wawo sumagwira ntchito bwino.”​—Discover.

      Kumwa mowa kwa nthawi yaitali kumayambitsanso ziphuphu, kukalamba uli mwana, kunenepa kwambiri, kulephera kuchita zinthu ngati sunamwe mowa komanso kuyamba kugwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo. Kukhozanso kuwononga mitsempha, chiwindi ndiponso mtima.

      c. Munthu sungafe chifukwa chomwa mowa wambiri. Yankho​—Zabodza. Kumwa mowa kwambiri kumachititsa kuti muubongo musamafike mpweya wokwanira, zomwe zingachititse kuti ziwalo zina zisiye kugwira ntchito. Zizindikiro zake ndi kusanza, kukomoka ndiponso kuvutika kupuma. Nthawi zina munthu akhoza kufa.

      d. Baibulo limaletsa kumwa mowa. Yankho​—Zabodza. Baibulo silimaletsa kumwa mowa komanso silimaletsa achinyamata kusangalala. (Salimo 104:15; Mlaliki 10:19) Komabe, ngati mukufuna kumwa mowa muyenera kudikira mpaka mutafika msinkhu wovomerezeka ndi boma.​—Aroma 13:1.

      Koma Baibulo limaletsa kumwa mowa kwambiri. Lemba la Miyambo 20:1 limati: “Vinyo ndi wonyoza. Chakumwa choledzeretsa chimasokosera ndipo aliyense wosochera nacho alibe nzeru.” Mowa ukhoza kukupangitsani kuti muzichita zinthu zopanda nzeru. N’zoona kuti mukamayamba kumene kumwa mowa mumamva bwino, koma mukamwa wambiri ‘umaluma ngati njoka’ ndipo umakusiyirani mavuto ambiri.​—Miyambo 23:32.

      e. Vuto lokha limene ungakumane nalo ngati umamwa mowa wambiri ndi kudwadwala basi. Yankho​—Zabodza. Munthu ukaledzera n’zosavuta kuti anthu akuchite chipongwe, ngakhale kukugwiririra kumene. Komanso, mukhoza kuchita zinthu zosokoneza zomwe zikhoza kupweteketsa ena ndipo zimakhala zoti simungachite mutakhala kuti muli bwinobwino. Baibulo limachenjezanso kuti kumwa mowa kwambiri kumachititsanso ‘maso kuona zinthu zachilendo, ndipo mtima umalankhula zinthu zokhota.’ (Miyambo 23:33) Mwachidule tingati mungachite zinthu zodzichotsera ulemu. Mavuto ena angaphatikizepo kudana ndi anzanu, kulephera sukulu, kukanika kugwira bwino ntchito, kupalamula milandu yomwe ingakuipitsireni mbiri mpaka kalekale komanso kusauka.​—Miyambo 23:21.

      Koma kwenikweni ganizirani mmene kumwa mowa kwambiri kungasokonezere ubwenzi wanu ndi Yehova. Yehova Mulungu amafuna kuti muzimutumikira ndi ‘maganizo anu onse,’ osati kumutumikira maganizo anu atasokonezeka chifukwa chomwa mowa kwambiri. (Mateyu 22:37) Sikuti Mawu a Mulungu amangoletsa “kumwa vinyo mopitirira muyezo” kokha, amaletsanso “kumwa kwa mpikisano.” (1 Petulo 4:3) Choncho, kumwa mowa wambiri n’kosemphana ndi zimene Mlengi wathu amafuna komanso kungapangitse kuti musakhalenso pa ubwenzi wabwino ndi Mulungu.

      Kodi Inuyo Musankha Chiyani?

      Kodi inuyo mutengera zochita za anzanu omwe amamwa kwambiri mowa? Baibulo limati: “Kodi simukudziwa kuti ngati mudziperekabe kwa winawake monga akapolo kuti muzimumvera, mumakhala akapolo ake chifukwa chakuti mumamumvera?” (Aroma 6:16) Kodi mukufuna kukhala kapolo, kaya wa anzanu kapena wa mowa?

      Koma bwanji ngati muli kale ndi chizolowezi chomwa mowa wambiri? Uzani makolo anu mwamsanga kapena mnzanu wachikulire kuti akuthandizeni. Pempherani kwa Yehova Mulungu ndipo m’pempheni kuti akuthandizeni. Ndipotu iye ndi “thandizo lopezeka mosavuta pa nthawi ya masautso.” (Salimo 46:1) Popeza achinyamata ambiri amayamba kumwa kwambiri mowa chifukwa cha anzawo, mungachite bwino kusintha anthu amene mumacheza nawo.b Kusintha anthu ocheza nawo sikophweka koma Yehova akhoza kukuthandizani.

      M’MUTU WOTSATIRA

      N’zotheka kusiya kugwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo. Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zomwe zingakuthandizeni.

      [Mawu a M’munsi]

      a Onani bokosi lakuti, “Ndani Akuchita Zimenezi?” patsamba 249.

      b Kuti mumve zambiri, werengani Mutu 8 ndi 9 m’bukuli komanso Mutu 15, m’Buku Lachiwiri.

      LEMBA

      ‘Chidakwa . . . chidzasauka.’​—Miyambo 23:21.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      Ganizirani zifukwa zomwe zikukuchititsani kufuna kumwa mowa. Kenako ganizirani za zinthu zina zabwino zimene mungachite kuti musangalale.

      KODI MUKUDZIWA . . . ?

      Kafukufuku wina amene anachitika ku United States anapeza kuti, “mosiyana ndi achinyamata omwe samwa kwambiri mowa, achinyamata omwe amamwa kwambiri mowa sakonda kulowa m’kalasi, amachedwa kumaliza homuweki, amavulala komanso amawononga katundu.”

      ZOTI NDICHITE

      Ngati anzanga akufuna kuti timwe mowa mopitirira muyezo, ndingawauze kuti ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pa nkhaniyi ․․․․․

      KODI INUYO MUKUGANIZA BWANJI?

      ● N’chifukwa chiyani anzanu amafuna kuti anthu ena azimwa nawo mowa mopitirira malire?

      ● Kodi kumwa mowa kwambiri kungapangitse kuti anyamata kapena atsikana azikuonani kukongola? N’chifukwa chiyani mwayankha choncho?

      [Mawu Otsindika patsamba 250]

      “Anzanga akusukulu akamandipatsa mowa, ndimawauza kuti ndimatha kukhala wosangalala popanda mowa.”​—Anatero Mark

      [Bokosi patsamba 249]

      Ndani Akuchita Zimenezi?

      Mwana mmodzi pa 4 alionse akusekondale azaka 13 kapena 14, omwe anafunsidwa pa kafukufuku wina yemwe anachitika ku England, Scotland, ndi Wales, “ananena kuti anamwapo mabotolo a mowa oposa 5 nthawi imodzi.” Ndipo hafu ya achinyamata onse azaka 15 ndi 16 omwe anafunsidwa, ananena kuti nawonso anamwapo mowa wambiri chonchi. Dipatimenti ya zaumoyo wa anthu ya ku United States inafotokoza kuti, “achinyamata pafupifupi 10.4 miliyoni azaka zoyambira 12 mpaka 20 ananena kuti amamwa mowa. Pa gulu limeneli, achinyamata 5.1 miliyoni amamwa mowa wambiri ndipo 2.3 miliyoni ndi zidakwa chifukwa pa mwezi umodzi amapezeka kuti amwa mowa wambiri maulendo oposa 5.” Kafukufuku wina amene anachitika ku Australia anasonyeza kuti kawirikawiri atsikana ndi amene amamwa mowa wambiri kuposa anyamata chifukwa amamwa mabotolo 13 mpaka 30 nthawi imodzi.

      [Chithunzi patsamba 251]

      Mowa umatha kuluma ngati njoka

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena