Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Ndingapeze Bwanji Anzanga Abwino?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
    • Mutu 8

      Kodi Ndingapeze Bwanji Anzanga Abwino?

      “Ndikakwiya ndimafuna munthu woti ndimuuze mmene ndikumvera. Ndikakhumudwa ndimafuna munthu woti andilimbikitse. Ndikasangalala ndimafuna munthu amene angasangalale nane. Ineyo ndimaona kuti munthu aliyense amafunika kukhala ndi anzake.”​—Anatero Brittany.

      PAMENE munali mwana munkafuna ana ena kuti muzisewera nawo. Koma panopo mumafuna mutakhala ndi mnzanu wapamtima, amene mukhoza kumacheza naye komanso kuchita naye zinthu limodzi.

      Komanso Baibulo limanena kuti “bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse, ndipo ilo ndi m’bale amene anabadwira kuti akuthandize pakagwa mavuto.” (Miyambo 17:17) Zimenezi zikusonyeza kuti mnzanu wapamtima amakhala wapadera kwambiri.

      Mfundo yofunika: Mukamakula mumafuna kukhala ndi anzanu omwe

      1. Ali ndi makhalidwe abwino

      2. Amatsatira mfundo zabwino pa moyo wawo

      3. Akhoza kukuthandizani kuchita zinthu zabwino

      Funso: Kodi mungapeze bwanji anzanu oti ali ndi zinthu zitatu zomwe tatchulazi? Tiyeni tikambirane chimodzi ndi chimodzi.

      Choyamba: Makhalidwe Abwino

      Zimene muyenera kudziwa. Sikuti aliyense amene amati ndi mnzanu amakhala mnzanu wapamtima, chifukwa ngakhale Baibulo limati: “Pali mabwenzi amene amafuna kuthyolana.” (Miyambo 18:24) Mwina mungaganize kuti lembali likukokomeza. Koma taganizirani izi: Kodi munakhalapo ndi mnzanu yemwe ankaoneka ngati amakukondani koma cholinga chake chinali choti angopeza zimene akufuna? Kapena munakhalapo ndi mnzanu woti ankakujedani kapena ankakakunenerani zinthu zabodza kwa anthu ena? Zimenezi zikhoza kukuchititsani kuti musamakhulupirirenso anzanu.a Ndiyetu nthawi zonse muzikumbukira kuti ndi bwino kukhala ndi anzanu ochepa odalirika kusiyana n’kukhala ndi anzanu ambiri koma osadalirika.

      Zimene mungachite. Muzicheza ndi anthu amakhalidwe omwe mungakonde kutengera.

      “Ndili ndi mnzanga, dzina lake Fiona. Aliyense amaona kuti ndi munthu wa makhalidwe abwino. Inenso ndimafuna kuti anthu aziona kuti ndine munthu wa makhalidwe abwino. Limeneli ndi khalidwe losiririka kwambiri.”​—Anatero Yvette, wazaka 17.

      Tachitani izi.

      1. Werengani Agalatiya 5:22, 23.

      2. Dzifunseni kuti, ‘Kodi anzanga ali ndi “makhalidwe amene mzimu woyera umatulutsa”?’

      3. Lembani m’munsimu mayina a anzanu amene mumacheza nawo kwambiri. Ndiyeno lembani khalidwe limene mnzanu aliyense amadziwika nalo.

      Dzina Khalidwe

      ․․․․․ ․․․․․

      Dziwani izi: Ngati anzanuwo amadziwika ndi makhalidwe oipa, pezani anzanu ena odziwika ndi makhalidwe abwino.

      Chachiwiri: Mfundo Zabwino Zimene Amatsatira

      Zimene muyenera kudziwa. Munthu akamafuna kupeza anzake ocheza nawo mwamsanga m’pamene amapeza anzake a makhalidwe oipa. Baibulo limanena kuti: “Wochita zinthu ndi anthu opusa adzapeza mavuto.” (Miyambo 13:20) Mawu akuti “anthu opusa” sakutanthauza anthu amene sakhoza kusukulu kapena anthu opanda nzeru. Mawu amenewa amanena za anthu amene satsatira mwadala mfundo za makhalidwe abwino. Anthu oterewa sangakhale anzanu abwino.

      Zimene mungachite. M’malo momangocheza ndi munthu wina aliyense, muzisankha anthu ocheza nawo. (Salimo 26:4) Koma zimenezi sizikutanthauza kuti muzichita zinthu mwatsankho. Pamene tikunena kuti muzisankha, tikutanthauza kuti muzitha kusiyanitsa “pakati pa munthu wolungama ndi woipa ndiponso pakati pa munthu amene akutumikira Mulungu ndi amene sanatumikirepo Mulungu.”​—Malaki 3:18.

      “Ndikuthokoza kwambiri makolo anga kuti anandithandiza kupeza anzanga amsinkhu wanga amene amakonda zinthu zauzimu.”​—Anatero Christopher, wazaka 13.

      Yankhani mafunso ali m’munsiwa:

      Kodi ndikakhala ndi anzanga ndimachita mantha kuti andikakamiza kuchita zinthu zimene ndikudziwa kuti n’zoipa?

      □ Inde

      □ Ayi

      Kodi sindifuna kupita ndi anzanga kunyumba chifukwa ndimaopa kuti makolo anga andiletsa kuti ndisamacheze nawo?

      □ Inde

      □ Ayi

      Dziwani izi: Ngati mwayankha kuti inde pa mafunso ali pamwambawa, pezani anzanu amene amatsatira mfundo za makhalidwe abwino, omwe ndi Akhristu a chitsanzo chabwino.

      Chachitatu: Kukuthandizani Kuchita Zinthu Zabwino

      Zimene muyenera kudziwa. Baibulo limati: “Kugwirizana ndi anthu oipa kumawononga makhalidwe abwino.” (1 Akorinto 15:33) Mtsikana wina, dzina lake Lauren, ananena kuti: “Anzanga akusukulu ankagwirizana nane ndikamachita zimene iwowo akufuna. Nthawi imeneyo ndinkasowa wocheza naye ndiye ndinkangochita zimene akufuna kuti ndipeze ocheza nawo.” Lauren anazindikira kuti ukamangotsatira mfundo za anthu ena, umangokhala ngati kachidole kawo ndipo amakuseweretsa mmene akufunira. Koma si mmene ziyenera kukhalira.

      Zimene mungachite. Siyani kucheza ndi anthu amene amakukakamizani kuti muzitsatira zimene iwowo amachita. N’zoona kuti mukachita zimenezi mukhoza kukhala ndi anzanu ochepa koma muzikhala osangalala. Ndipo mudzapeza anzanu abwino amene angakulimbikitseni kuchitanso zinthu zabwino.​—Aroma 12:2.

      “Mnzanga wapamtima, dzina lake Clint, amaganiza bwino ndipo ndi munthu wachifundo. Chifukwa chakuti ali ndi makhalidwe amenewa amandilimbikitsa kwambiri.”​—Anatero Jason, wazaka 21.

      Yankhani mafunso ali m’munsiwa:

      Kodi ndimasintha kavalidwe, mmene ndimalankhulira kapena kuchita zinthu zoipa pongofuna kusangalatsa anzanga?

      □ Inde

      □ Ayi

      Kodi ndimapita ndi anzanga kumalo okayikitsa amene pandekha sindikanapita?

      □ Inde

      □ Ayi

      Dziwani izi: Ngati mwayankha kuti inde pamafunso amenewa pemphani makolo anu kapena munthu wachikulire amene mumamudalira kuti akuthandizeni. Ngati ndinu wa Mboni za Yehova, mungapite kwa m’bale yemwe ndi mkulu ndipo muuzeni kuti akuthandizeni kusankha anzanu omwe angakulimbikitseni kuchita zabwino.

      WERENGANI ZAMBIRI PA NKHANIYI M’MUTU 9 M’BUKU LACHIWIRI

      M’MUTU WOTSATIRA

      Kodi mungatani kuti musamakopeke ndi mtima wanu kapena ndi zochita za anzanu?

      [Mawu a M’munsi]

      a Chifukwa chakuti ndife ochimwa aliyense amalakwitsa zinthu. (Aroma 3:23) Choncho, mnzanu akachita zinthu zokukhumudwitsani n’kupepesa kuchokera pansi pamtima, muzikumbukira mfundo yakuti: “Chikondi chimakwirira machimo ochuluka.”​—1 Petulo 4:8.

      LEMBA

      “Pali bwenzi limene limamatirira kuposa m’bale wako.”​—Miyambo 18:24.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      Ngati mumatsatira mfundo za makhalidwe abwino pa moyo wanu, mumayamba kugwirizana ndi anthu amene amatsatiranso mfundo zomwezo ndipo amakhala anzanu apamtima.

      KODI MUKUDZIWA . . . ?

      Mulungu alibe tsankho komabe amasankha anthu amene angakhale ‘alendo m’chihema chake.’​—Salimo 15:1-5.

      ZOTI NDICHITE

      Ndichita zotsatirazi kuti ndipeze anzanga abwino: ․․․․․

      Anthu ena, omwe ndi aakulu kwa ineyo, omwe ndikufuna ndizicheza nawo ndi ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pa nkhaniyi ․․․․․

      KODI INUYO MUKUGANIZA BWANJI?

      ● Kodi mumafuna kuti mnzanu azikhala ndi makhalidwe ati ndipo chifukwa chiyani?

      ● Kodi ndi makhalidwe ati amene mukufunika kusintha kuti mukhale munthu wabwino?

      [Mawu Otsindika patsamba 60]

      “Nthawi ina makolo anga anandiletsa kucheza ndi anzanga enaake. Ndinkangoona ngati palibenso anthu ena omwe ndingamacheze nawo kupatulapo anzangawo. Makolo anga anandilangiza ndipo nditaganizira kwambiri zimene anandiuzazo, ndinazindikira kuti pali anthu ambiri omwe akhoza kukhalanso anzanga.”​—Anatero Cole.

      [Bokosi patsamba 61]

      Tayesani kuchita izi

      Kambiranani ndi makolo anu. Afunseni kuti anali ndi anzawo otani ali msinkhu ngati wanuwo. Kodi panopa amadandaula kuti sanasankhe bwino anzawo ocheza nawo? Ngati amadandaula, amadandaula chifukwa chiyani? Afunseni zimene mungachite kuti mupewe mavuto amene iwowo anakumana nawo.

      Makolo anu azidziwa anzanu amene mumacheza nawo. Ngati simufuna kuti makolo anu azidziwa anzanu amene mumacheza nawo, dzifunseni kuti, ‘N’chifukwa chiyani?’ Kodi pali zinazake zomwe anzanuwo amachita zimene makolo anu sangasangalale nazo? Ngati zilipo, muyenera kusankhanso anzanu ocheza nawo.

      Muzimvetsera. Muzichita chidwi ndi zimene anzanu akuganiza, zimene zikuwachitikira komanso zimene zikuwadetsa nkhawa.​—Afilipi 2:4.

      Muzikhululuka. Musamayembekezere kuti anzanu azichita zinthu zolondola nthawi zonse, chifukwa “tonsefe timapunthwa nthawi zambiri.”​—Yakobo 3:2.

      Muzipatsako anzanu mpata. Simufunika kumangowakakamira anzanu kulikonse komwe ali. Mnzako weniweni amakhalapo nthawi iliyonse yomwe akufunikira.​—Mlaliki 4:9, 10.

      [Chithunzi patsamba 63]

      Munthu akamangotsatira zimene anzake amachita amakhala ngati kachidole kawo ndipo amangomuseweretsa mmene akufunira

  • Kodi Ndingatani Kuti Ndisamakopeke Ndi Zochita za Anzanga?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
    • Mutu 9

      Kodi Ndingatani Kuti Ndisamakopeke Ndi Zochita za Anzanga?

      Karen wangofika kumene kuphwando ndipo akuona anyamata awiri akubwera ndi zimajumbo zikuluzikulu ziwiri. Iye wadziwiratu zimene zili m’majumbomo chifukwa nthawi inayake anamva anyamatawo akukambirana kuti kuphwandoko kukakhala mowa wochita kusamba.

      Kenako Karen akumva mnzake, dzina lake Jessica, akumufunsa kuti: “Kodi iwe wangoti ndwii pamenepo bwanji?” Pamene Karen akutembenuka akuona kuti mnzakeyo wanyamula mabotolo awiri a mowa ongotsegula kumene. Jessica akum’patsa Karen botolo limodzilo n’kumuuza kuti: “Eko imwa, kumanjoyako nthawi zina. Si zoti ‘Ine sindimwa.’”

      Karen akufuna kukana koma akuona kuti n’zovuta. Jessica ndi mnzake komanso sakufuna kuti azimuona ngati samanjoyako nthawi zina. Komanso Karen amaona kuti Jessica ndi munthu wabwino. Ngati iyeyo akumwa ndiye kuti kumwa kulibe vuto lililonse. Karen akuganiza kuti: ‘Kumwa mowa kuli ndi vuto ngati? Ngati kuti ndikumwa mankhwala osokoneza bongo kapena ndikuchita uhule?’

      MUNTHU ukakhala wamng’ono umayesedwa ndi zinthu zosiyanasiyana zomwe zikhoza kukukopa ndipo nthawi zambiri ngati ndiwe mnyamata umayesedwa ndi atsikana pomwe atsikana amayesedwa ndi anyamata. Mnyamata wina wazaka 17, dzina lake Ramon, ananena kuti: “Atsikana akusukulu kwathu ndi okakamira kwambiri. Amakonda kukugwiragwira pongofuna kukuyesa ndipo ngati sungawaletse akhoza kukugwira posakhala bwino. Samakusiya ngakhale uwaletse.” Nayenso mtsikana wina wazaka 17, dzina lake Deanna, amakumananso ndi vuto lomweli. Iye ananena kuti: “Mnyamata wina anabwera n’kundikolekera m’khosi. Ndinam’menya pamkono ndi mphamvu n’kumuuza kuti: ‘Tandisiye iwe, bwanji kodi?’”

      N’kutheka kuti nanunso mumayesedwa ndi anzanu ndipo zimaoneka ngati kuyesedwako sikudzatha. Nthawi zina anthu amapitirizabe kukuyesa ngakhale utayesetsa kusonyeza kuti sukufuna kuchita zomwe akufunazo. Kodi inuyo mumayesedwa kawirikawiri? Kodi inuyo mumakopeka ndi zinthu zili m’munsizi?

      □ Kusuta fodya

      □ Kuonera zolaula

      □ Kumwa mowa

      □ Kufuna kugonana ndi munthu wina

      □ Kumwa mankhwala ozunguza bongo

      □ Zina ․․․․․

      Ngati mwaika chizindikiro ichi ✔ m’kabokosi kena kalikonse pamwambapa musaganize kuti n’zosatheka kukhala Mkhristu. Mukhoza kuphunzira kusatengeka ndi zochita za ena. Chimene chingakuthandizeni kuchita zimenezi ndi kuzindikira zimene zimachititsa kuti muzikopeka ndi zochita za ena. Tiyeni tione zinthu zitatu.

      1. Ndife ochimwa. Munthu aliyense wochimwa amafuna kuchita zinthu zoipa. Ngakhale mtumwi Paulo, yemwe anali Mkhristu wolimba, anavomereza mfundo imeneyi ponena kuti: “Pamene ndikufuna kuchita chinthu chabwino, choipa chimakhala chili ndi ine.” (Aroma 7:21) Choncho, ngakhale munthu amene amayesetsa kuchita zinthu zabwino nthawi zina amalimbana ndi “chilakolako cha thupi,” komanso “chilakolako cha maso.” (1 Yohane 2:16) Koma ngozi imakhalapo ngati munthu akungoganizira zinthu zoipazo chifukwa Baibulo limati: “Chilakolako chikatenga pakati, chimabala tchimo.”​—Yakobo 1:15.

      2. Anzanu komanso zinthu zina. Munthu ukhoza kukopeka kuchita zinthu zoipa kwina kulikonse. Mtsikana wina, dzina lake Trudy, ananena kuti: “Anthu amangokhalira kukamba nkhani zogonana, kaya ndi kusukulu ndiponso kuntchito. Ndipo akamazionetsa pa TV komanso m’mafilimu amazionetsa ngati ndi zinthu zosangalatsa kwambiri. Moti nthawi zambiri saonetsa mavuto amene munthu angakumane nawo.” Zimene zinachitikira Trudy zinamuthandiza kuzindikira kuti zochita za anthu ena komanso zimene timaonera, zikhoza kutikopa n’kuchita zoipa. Iye ananena kuti: “Ndili ndi zaka 16 ndinayamba chibwenzi ndi mnyamata wina ndipo ndinkaona kuti timakondana kwambiri. Mayi anga anandilangiza kuti ngati sindithetsa chibwenzicho nditenga mimba. Ndinadabwa kwambiri ndi zimene ananenazi. Koma patangotha miyezi iwiri, ndinapezeka kuti ndilidi ndi mimba.”

      3. “Zilakolako zaunyamata.” (2 Timoteyo 2:22) Zilakolako zaunyamata zingaphatikizepo chilichonse chomwe achinyamata amafuna monga kufuna kuti azikondedwa ndi anthu ena komanso kuti anthu ena aziwaona kuti ndi munthu wamkulu. Sikulakwa kufuna zinthu zimenezi koma ngati munthu sangasamale zikhoza kuchititsa kuti akopeke mosavuta. Mwachitsanzo, ngati mukufunitsitsa kuti anthu ena azikuonani kuti ndinu munthu wamkulu mukhoza kuyamba kunyalanyaza malangizo a makolo anu. Ndi zimene zinachitikira Steve ali ndi zaka 17. Iye ananena kuti: “Ndinasiya kutsatira malangizo a makolo anga ndipo ndinayamba kuchita zinthu zimene ankandiletsa. Ndinachita zonsezi nditangobatizidwa kumene.”

      Mmene Mungapewere Kuchita Zoipa

      Zinthu zitatu zimene tazitchula pamwambazi zimachititsa kuti anthu ambiri azikopeka kuchita zoipa. Komabe, n’zotheka kupewa kuchita zinthu zoipa. Kodi mungazipewe bwanji?

      ● Choyamba, zindikirani chinthu chimene chimakukopani kwambiri. (Mwina mwasankha kale pamwambapa.)

      ● Ndiyeno dzifunseni kuti: ‘Kodi ndimakopeka kwambiri ndikakhala ndili kuti?’ Ikani chizindikiro ichi ✔ m’kabokosi kamene kakusonyeza kumene mumakopeka kwambiri:

      □ Kusukulu

      □ Ndikakhala ndekha

      □ Kuntchito

      □ Malo ena ․․․․․

      Kudziwa malo amene mungakopeke mosavuta kungakuthandizeninso kupewa kuchita zoipa. Mwachitsanzo, taganizirani zimene tafotokoza kumayambiriro kwa nkhaniyi. Kodi n’chiyani chikanamuthandiza Karen kudziwa kuti kuphwandoko kukhoza kuchitika zinazake zoipa?

      ․․․․․

      Kodi Karen akanatani kuti asakopeke?

      ․․․․․

      ● Popeza mwazindikira zinthu zimene zikhoza kukukopani komanso nthawi imene mungakopeke, tsopano mukhoza kupeza njira yopewera vutolo. Chinthu choyamba chimene mungachite ndi kuganizira zimene mungachite kuti musamakopeke kwambiri kapenanso musamakopeke n’komwe. Lembani m’munsimu zimene mungachite.

      ․․․․․

      (Zitsanzo: Ngati nthawi zambiri anzanu a kusukulu amakukopani kuti musute fodya mukaweruka, mwina mungasinthe njira imene mumadutsa kuti musamakumane nawo. Ngati muli ndi foni ya intaneti ndipo mumalandira zithunzi zolaula, mwina mungaikemo mapulogalamu oti azitsekereza kuti zinthu zimenezo zisamabwere. Komanso mukamafufuza zinthu pa intaneti muzilemba zinthu zomwe mukufunazo momveka bwino.)

      N’zoona kuti simungapeweretu zinthu zonse zoipa. Mwina mukhoza kukumana ndi zinthu zokopa kwambiri pa nthawi imene simukuyembekezera. Kodi mungatani kuti musadzakopeke?

      Konzekerani

      Pamene Yesu ‘ankayesedwa ndi Satana’ anamuyankha mwamphamvu nthawi yomweyo. (Maliko 1:13) Anachita zimenezi chifukwa ankadziwa kale zimene ankayenera kuchita pa nkhaniyo komanso chifukwa chakuti anali atatsimikiza kale mumtima mwake kuti azimvera Atate wake nthawi zonse. (Yohane 8:28, 29) Yesu ananena kuchokera pansi pa mtima kuti: “Ndinatsika kuchokera kumwamba kudzachita chifuniro cha iye amene anandituma, osati chifuniro changa.”​—Yohane 6:38.

      Patsamba lotsatirali, lembani zifukwa ziwiri zokuchititsani kupewa chinthu chomwe chimakukopani nthawi zambiri. Lembaninso zinthu ziwiri zimene zingakuthandizeni kuti muzipewa chimene chimakukopanicho.

      Zifukwa:

      1 ․․․․․

      2 ․․․․․

      Zimene zingakuthandizeni:

      1 ․․․․․

      2 ․․․․․

      Muzikumbukira kuti nthawi iliyonse imene mwalolera kuchita zinthu zoipa, mumakhala kapolo wa mtima wanu. (Tito 3:3) Si bwino kulola kuti mtima wanu uzikulamulirani. Inuyo ndi amene muyenera kulamulira mtima wanuwo. (Akolose 3:5) Ndipo muziipempherera nkhani imeneyi.​—Mateyu 6:13.a

      WERENGANI ZAMBIRI PA NKHANIYI M’MUTU 15 M’BUKU LACHIWIRI

      M’MUTU WOTSATIRA

      Kodi mukumalephera kuchita zinthu mwachangu? Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zimene mungachite kuti mukhale ndi mphamvu komanso thanzi labwino

      [Mawu a M’munsi]

      a Werengani Mutu 33 ndi 34.

      LEMBA

      “Mulungu ndi wokhulupirika ndipo sadzalola kuti muyesedwe kufika pamene simungapirire, koma pamene mukukumana ndi mayeserowo iye adzapereka njira yopulumukira kuti muthe kuwapirira.”​—1 Akorinto 10:13.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      Onani bokosi limene lili patsamba 132 ndi 133, lomwe lili ndi mutu wakuti “Mmene mungakonzekerere” m’buku la Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri. Bokosili lingakuthandizeni kudziwa komanso kukonzekereratu zimene munganene ngati munthu wina atakunyengererani kuti muchite zoipa.

      KODI MUKUDZIWA . . . ?

      Mulungu ananeneratu kuti Yesu adzakhala wokhulupirika, koma zimenezi sizikutanthauza kuti Yesu analengedwa ngati loboti yomwe imangochita zinthu osaganiza. Yesu anali ndi ufulu wosankha zoyenera kuchita moti anakhala munthu wokhulupirika chifukwa choti anachita kusankha yekha osati chifukwa chakuti anam’panga kuti adzakhale wokhulupirika. N’chifukwa chake ankachita kupemphera akamayesedwa.​—Aheberi 5:7.

      ZOTI NDICHITE

      Ndizichita zotsatirazi kuti ndizilimba mtima kupewa kuchita zinthu zoipa: ․․․․․

      Malo, anthu komanso zochitika zimene ndiyenera kuzipewa: ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pa nkhaniyi ․․․․․

      KODI INUYO MUKUGANIZA BWANJI?

      ● Kodi zolengedwa zopanda uchimo zikhoza kukopedwa kuti zichite zinthu zoipa?​—Genesis 6:1-3; Yohane 8:44.

      ● Kodi anthu ena amakhudzidwa bwanji ngati simunakopeke kuti muchite zoipa?​—Miyambo 27:11; 1 Timoteyo 4:12.

      [Mawu Otsindika patsamba 68]

      “Chimene chimandithandiza kwambiri ndi kudziwa kuti Mulungu, yemwe ndi wamphamvu kwambiri m’chilengedwe chonsechi, ndi wokonzeka kundithandiza ndipo ndikhoza kumupempha nthawi iliyonse kuti andithandize.”​—Anatero Christopher

      [Bokosi/​Chithunzi patsamba 67]

      Ganizirani Izi

      Nthawi zonse muvi wa kampasi umaloza kumpoto. Koma ngati kampasiyo itayandikana ndi maginito, muviwo sumalozanso kumpoto. M’malomwake umaloza mbali imene kuli maginitowo.

      Chikumbumtima chanu chili ngati kampasi. Ngati munachiphunzitsa bwino chimakuthandizani kusankha zinthu mwanzeru. Koma kucheza ndi anthu oipa, n’kwamphamvu ngati maginito chifukwa kungakusokonezeni maganizo n’kuyamba kuchita zinthu zolakwika. Choncho, ndi bwino kuti muzipewa kukhala malo olakwika komanso kucheza ndi anthu omwe angakuchititseni kuti musamasankhe zinthu mwanzeru.—Miyambo 13:20.

      [Chithunzi patsamba 69]

      Mukalolera kuchita zinthu zoipa mumakhala kapolo wa mtima wanu

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena