Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wcg mutu 8 tsamba 44-tsamba 47
  • Sanagonje Atakumana Ndi Mayesero

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sanagonje Atakumana Ndi Mayesero
  • Muziyenda Ndi Mulungu Molimba Mtima
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Zoti Mufufuze
  • Zomwe Tikuphunzirapo
  • Ganizirani Mfundo Yaikulu
  • Phunzirani Zambiri
  • Anali Bambo Wolimba Mtima
    Muziyenda Ndi Mulungu Molimba Mtima
  • Kapolo Amene Ankamvera Mulungu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • ‘Ndingachitirenji Choipa Chachikulu N’kuchimwira Mulungu?’
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Yehova Amatithandiza Kuti Zinthu Zizitiyendera Bwino
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Muziyenda Ndi Mulungu Molimba Mtima
wcg mutu 8 tsamba 44-tsamba 47

8 YOSEFE

Sanagonje Atakumana Ndi Mayesero

Losindikizidwa
Losindikizidwa

ALI wachinyamata, Yosefe ankakondedwa kwambiri ndi bambo ake (a Yakobo) komanso ndi Yehova Mulungu wake. Koma zimenezi sizikutanthauza kuti sanakumane ndi mavuto aliwonse. Azichimwene ake ankadana naye kwambiri. Chifukwa chakuti bambo ake ankamukonda komanso kumuchitira zinthu zina zapadera, azichimwene ake ankamuchitira nsanje. Yehova atamulotetsa maloto osonyeza kuti nthawi ina banja lawo lidzamugwadira, mkwiyo wa azichimwene ake unakula kwambiri.

Tsiku lina Yosefe ali ndi zaka pafupifupi 17, bambo ake anamutuma kuti akaone ngati azichimwene ake anali bwino ndipo ulendowu unali wamasiku angapo. Atafika, azichimwene ake anamugwira n’kumuponyera m’chitsime chopanda madzi. Iye anawachonderera koma sanamumvere chisoni. Kenako anaganiza zongomugulitsa kwa a malonda omwe ankadutsa ngakhale kuti poyamba anakambirana zoti amuphe. Kenako anakanamiza bambo awo kuti Yosefe wadyedwa ndi chilombo, ngakhale kuti anali atapita chakum’mwera ku Iguputo komwe anakagulitsidwa ngati kapolo kwa Potifara amene anali nduna m’boma la Farao.

Yosefe akanatha kutaya mtima. Koma anakhalabe wolimba mtima ndipo ankagwira ntchito mwakhama. Baibulo limati: “Yehova anali ndi mnyamatayo.” Iye anaonetsetsa kuti pa chilichonse chomwe Yosefe angachite, zinthu zizimuyendera bwino. Potifara anamupatsa udindo woyang’anira nyumba yake ndi zinthu zake zonse.

Panachitikanso nkhani ina yoopsa. “Yosefe anali wooneka bwino ndiponso wa thupi loumbika bwino” moti mkazi wa Potifara anayamba kumusirira. Iye anaonetsa poyera kuti ankamufuna mpaka anamuuza kuti: “Ugone nane.” Makolo ndi achibale a Yosefe anali kutali, ndiye kodi iye akanatani? Komanso anali kapolo wamba choncho mabwana akewo akanatha kumuchita chilichonse. Abwana ake aakazi akanatha kumuzunza kwambiri. Koma kodi Yosefe anakopeka n’kuchita zomwe mkaziyo ankafuna, kapena anakana?

Yosefe akuyenda m’nyumba ya Potifara atanyamula jagi yadothi ndipo akuyang’ana kutsogolo. Mkazi wa Potifara waima panja pa chipinda chake ndipo akumuyang’ana momukopa.

Kodi Yosefe anakwanitsa bwanji kukana kuchita zoipa ngakhale ankadziwa kuti mkazi wa Potifara akanatha kumuzunza?

Baibulo limati: “Ankakana.” Yosefe anauza mkaziyo kuti Potifara ankamukhulupirira kwambiri, choncho sakanamukhumudwitsa. Chochititsanso chidwi ndi choti Yosefe ananena kuti: “Ndingachitirenji choipa chachikulu chonchi nʼkuchimwira Mulungu?” Chifukwa chakuti Yosefe ankakonda kwambiri Yehova, analimba mtima n’kukana. Koma mkaziyo sanasiye kumuvutitsa. Ankamuuzabe “tsiku ndi tsiku” kuti agone naye. Tsiku lina antchito ena atatalikira, mkaziyo anagwira malaya a Yosefe n’kumuuza kuti: “Ugone nane basi!” Koma Yosefe anangovula malayawo n’kuthawa. Mkaziyo anasungabe malayawo kenako anadzamuonetsa Potifara n’kumuuza kuti Yosefe amafuna kumugwiririra. Potifara anakwiya kwambiri ndipo analamula kuti Yosefe atsekeredwe m’ndende.

Anatsekeredwa m’ndende yamdima ndipo kwakanthawi mapazi ake anamangidwa m’matangadza komanso anamuveka zitsulo m’khosi. (Sal. 105:​17, 18) Yosefe akanatayiratu chiyembekezo. Komabe, Yehova sanamusiye ndipo iyenso sanasiye kumudalira. Kundendeko, ankagwira ntchito mwakhama ndipo Yehova anamudalitsa. Pasanapite nthawi, woyang’anira ndende anamupatsa udindo waukulu. Iye anapitirizabe kupirira molimba mtima.

Chifukwa chakuti Yosefe anakhalabe wokhulupirika komanso wolimba mtima, Yehova ankamukonda kwambiri. Patapita nthawi, Mulungu analotetsa Farao maloto awiri onena zam’tsogolo ndipo Yosefe ndi amene anawamasulira. Iye anauza mfumuyo kuti malotowo akutanthauza kuti kudzakhala chakudya chambiri kwa zaka 7, komanso njala kwa zaka zinanso 7. Farao anasangalala n’kupatsa Yosefe udindo woonetsetsa kuti kuli chakudya chokwanira pokonzekera njalayo. Anamupatsanso udindo wokhala wachiwiri kwa iyeyo ndipo Yosefe anakwanitsa kupulumutsa anthu a ku Iguputo komanso banja lake lonse ku njala. Azichimwene ake atabwera kudzagula chakudya, mosadziwa anagwadira Yosefe. Maloto omwe analota ali mwana aja, anakwaniritsidwa. Patapita nthawi, azichimwene ake anasonyeza kuti anasintha n’kukhala anthu abwino. Mchimwene wawo amene ankadana naye poyamba, anawapulumutsa limodzi ndi bambo awo komanso m’badwo wobwera m’tsogolo. Izi zinatheka chifukwa Yosefe anali wolimba mtima komanso anapitirizabe kukhulupirira Yehova.

Werengani nkhaniyi m’Baibulo:

  • Genesis 37:​1-36; 39:​1-23; 41:1–45:28

Funso lokambirana:

Kodi Yosefe anasonyeza kulimba mtima m’njira ziti?

Zoti Mufufuze

  1. 1. N’chiyani chimatsimikizira kuti zomwe Baibulo limanena zokhudza moyo wa Yosefe ku Iguputo zinachitikadi? (g 11/10 15 ¶2)

  2. 2. Kodi Yosefe anadziwa bwanji kuti kuchita chigololo kunali “choipa chachikulu” kwa Yehova? (Gen. 39:9; w22.08 26 ¶2)

  3. 3. N’chifukwa chiyani Mulungu analola kuti Yosefe akhale nduna yaikulu ya Iguputo? (w96 5/1 11 ¶4-wcgr) A

    Yosefe, yemwe tsopano ndi nduna ku Iguputo, akuuza akapolo awiri zochita.

    Chithunzi A

  4. 4. N’chiyani chikusonyeza kuti Yosefe anali adakali ndi chikhulupiriro cholimba ngakhale pomwe anakwanitsa zaka 110? (Gen. 50:​25, 26; w07 6/1 28 ¶10-11) B

    Azibambo a Chiisiraeli anyamula bokosi lomwe muli mafupa a Yosefe ndipo akupita kukawaika m’manda m’Dziko Lolonjezedwa.

    Chithunzi B

Zomwe Tikuphunzirapo

  • Tikaona mmene Yosefe anachitira zinthu ndi azichimwene ake, tingaphunzire chiyani ngati Mkhristu mnzathu atatichitira zinthu zopanda chilungamo? (Gen. 45:​4, 5; 50:​19-21)

  • Yosefe anali wokhulupirika kwa Yehova ngakhale pamene anali kutali ndi kwawo. Kodi chitsanzo chake chingatithandize bwanji . . .

    • tikakhala kusukulu? C

      Mlongo wachitsikana akuchokera kusukulu ndipo akudutsa achinyamata omwe akusuta fodya. Achinyamatawo akumuyang’anitsitsa koma iye akungoyang’ana kutsogolo molimba mtima.

      Chithunzi C

    • tikakhala pa ulendo? D

      M’bale wachinyamata yemwenso ndi wokwatira, ali pa ulendo wokhudza za ntchito yake. Wafika kuhotelo kuti apeze malo ogona. Kumeneko wakumana ndi mtsikana wokongola yemwe si wa Mboni ndipo mtsikanayo akumuyang’anitsitsa.

      Chithunzi D

    • tikamagwiritsa ntchito foni kapena zipangizo zina? E

      M’bale wachinyamata wagona pabedi ndipo akuyang’ana pafoni yake.

      Chithunzi E

  • Kodi mungatsanzire bwanji kulimba mtima kwa Yosefe?

Ganizirani Mfundo Yaikulu

  • Kodi nkhaniyi yandiphunzitsa chiyani za Yehova?

  • Kodi nkhaniyi ikugwirizana bwanji ndi cholinga cha Yehova?

  • Kodi ndingakonde kudzamufunsa chiyani Yosefe akadzaukitsidwa?

Phunzirani Zambiri

Ngakhale kuti Yehova sanateteze Yosefe kuti asakumane ndi mayesero, anamuthandiza kuti akwanitse kuwapirira. Onani mmene angakuthandizireninso inuyo.

“Yehova Amatithandiza Kuti Zinthu Zizitiyendera Bwino” (w23.01 14-19)

Kodi ana angaphunzire chiyani kwa Yosefe anzawo akamawavutitsa?

Uzipilira Ngakhale Ena Akukuchitira Nkhanza (1:31)

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena