Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wcg mutu 31 tsamba 142-tsamba 145
  • Kamtsikana Kanalankhula Molimba Mtima Kudziko la Eni

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kamtsikana Kanalankhula Molimba Mtima Kudziko la Eni
  • Muziyenda Ndi Mulungu Molimba Mtima
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Zoti Mufufuze
  • Zomwe Tikuphunzirapo
  • Ganizirani Mfundo Yaikulu
  • Phunzirani Zambiri
  • Kamtsikana Kanathandiza Mkulu wa Asilikali
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Ankafuna Kuthandiza Ena
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Buthu Limene Linalankhula Molimba Mtima
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Mtsikana Athandiza Ngwazi
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Onani Zambiri
Muziyenda Ndi Mulungu Molimba Mtima
wcg mutu 31 tsamba 142-tsamba 145

31 KAMTSIKANA KA KU ISIRAELI

Kamtsikana Kanalankhula Molimba Mtima Kudziko la Eni

Losindikizidwa
Losindikizidwa

PANALI kamtsikana kena ka ku Isiraeli komwe kanakhalapo ndi moyo pa nthawi ya Mfumu Yehoramu. Dzina lake silidziwika, koma tikudziwa zinthu zothandiza kwambiri zimene kanachita. Mfumuyi komanso anthu amene inkawalamulira anasiya kulambira Yehova mokhulupirika choncho Yehovayo analola kuti Asiriya azibwera kudzamenyana nawo. Tsiku lina Asiriya atabwera, anagwira kamtsikanako n’kupita nako kudziko lawo.

Kamtsikanaka kayenera kuti kanali ndi mantha. Nawonso anthu am’banja lake ayenera kuti anali ndi nkhawa. Kamtsikanaka kanakhala wantchito wa Namani ndi mkazi wake. Namani anali mkulu wa asilikali a Siriya. Mwanayu ayenera kuti anayesetsa kuti azolowere moyo watsopanowu. Koma pasanapite nthawi, anazindikira kuti anthu am’banjali sankasangalala chifukwa panali vuto. Namani anali ndi matenda oopsa akhate. Matendawa ankachititsa munthu kukhala ndi mabala oopsa ndipo nthawi zina sankachira.

Ngakhale kuti anali kapolo m’dziko la anthu osalambira Mulungu, anapitirizabe kusonyeza chifundo komanso kulimba mtima

Kamtsikanaka kanali kokoma mtima kwambiri. Ngakhale kuti kankadziwa zoti Namani anali mdani wa Aisiraeli, kanamvera chisoni Namaniyo ndiponso mkazi wake. Ndipo kankadziwa zoti akhoza kuchira. N’kutheka kuti makolo ake anamufotokozera kuti Yehova anathandiza mneneri wake Elisa kuti achite zinthu zodabwitsa. Koma kamtsikanaka sikankadziwa ngati Elisa anachiritsapo munthu wodwala khate m’mbuyomo. Komabe kankakhulupirira kuti Mulungu wake, Yehova, akhoza kupereka mphamvu kwa mneneri wake zochiritsira Namani.

Koma kodi kakanalimba mtima kuuza banjali zokhudza Yehova ngakhale kankadziwa kuti kuchita zimenezi kunali koopsa? Namani ankalambira mulungu wotchedwa Rimoni ndipo nthawi zonse ankatenga mfumu ya Siriya kupita kukachisi kukalambira mulunguyu. Zikuoneka kuti anthu a ku Siriya ankaona kuti mulunguyu ndi amene ankabweretsa mphepo yamkuntho komanso mabingu. Kodi Namani akanaganiza chiyani zokhudza Yehova, Mulungu wa kamtsikanaka? Kodi mwina akanaona kuti wanyozeka ndi mfundo yoti Yehova akhoza kukwanitsa kuchita zimene mulungu wake walephera kuchita? Kamtsikanaka kayenera kuti kanapemphera kwa Yehova kuti akathandize kulimba mtima. Kenako kanauza abwana ake aakazi kuti: “Abwanawa akanapita kwa mneneri amene ali ku Samariya, bwenzi atakawachiritsa khate lawo.”

Kamtsikana ka ku Isiraeli kaima kuseri kwa chipilala m’nyumba ya Namani wakhate ndipo kakusunzumira. Kakuyang’ana mwachidwi pamene mkazi wa Namani akulimbikitsa mwamuna wake.

Amenewa ndi mawu okhawa amene amapezeka m’Baibulo amene kamtsikanaka kanalankhula. Mawuwa angaoneke ochepa, koma anathandiza kwambiri. Vesi lotsatira limanena kuti Namani anapita kwa mfumu dzina lake Beni-hadadi kukaifotokozera zomwe kamtsikana kaja kananena. Kenako mfumuyo inatumiza Namani ku Isiraeli ndipo inam’patsira kalata kuti akapereke kwa Mfumu Yehoramu yopempha kuti Namaniyo achiritsidwe khate lake.

Namani atachoka, anthu am’banja lake ankayembekezera mwachidwi kuti aone zomwe zingamuchitikire. Kamtsikanako kayenera kuti kankapempha Yehova mobwerezabwereza kuti achitepo kanthu n’cholinga choti Namani adziwe zoti Yehova yekha ndi Mulungu woona. Panadutsa masiku angapo kapenanso mawiki, Namani asanabwere. Koma tsiku lina anatulukira. Tangoganizani mmene anthu am’banjali anasangalalira atamuona. Iye anali atachira. Thupi lake, lomwe linali ndi mabala lija, linali bwinobwino ndipo linali ngati la mnyamata.

Kamtsikanako kayenera kuti kankamvetsera mwachidwi pamene Namani ankafotokoza za ulendo wake. Iye anafotokoza mmene Elisa anamulandirira, mmene anayesedwera pa nkhani ya kudzichepetsa komanso kuti anakwiya. Anafotokozanso kuti atumiki ake ndi amene anamulimbikitsa kuti atsatire malangizo osavuta omwe mneneri Elisa anamuuza. Kenako anafotokoza kuti atakasamba maulendo 7 mumtsinje wa Yorodano, anachira. Koma zomwe zinasangalatsa kwambiri kamtsikanaka n’zakuti Namani atachira, nthawi yomweyo anayamba kulambira Yehova Mulungu.

Zonsezi zinatheka chifukwa kamtsikanaka kanalimba mtima n’kulankhula zokhudza Mulungu komanso mneneri wake. N’zoona kuti sitikudziwa dzina la kamtsikanayu, koma Yehova akulidziwa. Koma ngati tingatsanzire kulimba mtima kwake, Yehova akadzamuukitsa tidzamuona. Tangoganizirani mmene mudzasangalalire kukumana naye, kudziwa dzina lake komanso kumumva akufotokoza zinthu zina zokhudza nkhaniyi.

Werengani nkhaniyi m’Baibulo

  • 2 Mafumu 5:​1-19

Funso lokambirana:

Kodi kamtsikana ka ku Isiraeli kanasonyeza kulimba mtima m’njira ziti?

Zoti Mufufuze

  1. 1. N’chifukwa chiyani mwina kamtsikanaka kankachita mantha ndi Asiriya komanso kudabwa ndi zomwe ankachita? (w96 5/15 8 ¶3-wcgr) A

    Courtesy of Musée du Louvre, Paris

    Chithunzi A: Chidole cha ku Siriya wakale, chomwe mwina chinali mulungu wotchedwa Rimoni

  2. 2. Fotokozani zomwe zimachitikira munthu wakhate. (it “Khate” ¶3-5-wcgr)

  3. 3. N’chifukwa chiyani Elisa sanalandire mphatso ya Namani? (w05 8/1 9 ¶2)

  4. 4. N’chifukwa chiyani Elisa ankakhulupirira kuti Yehova adzakhululukira Namani chifukwa chogwadira mulungu wotchedwa Rimoni? (2 Maf. 5:​18, 19; w05 8/1 9 ¶3) B

    Namani ndi mfumu yachikulire ya ku Siriya agwada kutsogolo kwa guwa la nsembe. Mfumuyo yawerama n’kumalambira mulungu wake wabodza koma Namani sanawerame ndipo sakuyang’ana guwalo.

    Chithunzi B

Zomwe Tikuphunzirapo

  • Namani anali mkulu wa asilikali a Asiriya ndipo anapita kukamenyana ndi Aisiraeli. Komabe Yehova anamuchiritsa. Kodi zimenezi zikutiphunzitsa chiyani pa mfundo yoti Yehova ndi wachifundo komanso wopanda tsankho? C

    Mnyamata wa Mboni akulalikira mnzake wakusukulu m’basi. Mnzakeyo ali ndi tsitsi lalitali lomwe lafika kunkhope kwake ndipo wavala ndolo m’zikope, m’makutu ndi pamlomo.

    Chithunzi C

  • Kodi chitsanzo cha kamtsikana ka ku Isiraeli chakulimbikitsani bwanji kuti muzilalikira ngakhale pamene mukuchita mantha?

  • Kodi mungatsanzire kulimba mtima kwa kamtsikana ka ku Isiraeli m’njira zinanso ziti?

Ganizirani Mfundo Yaikulu

  • Kodi nkhaniyi yandiphunzitsa chiyani za Yehova?

  • Kodi nkhaniyi ikugwirizana bwanji ndi cholinga cha Yehova?

  • Kodi ndingakonde kudzakafunsa chiyani kamtsikana ka ku Isiraeli kakadzaukitsidwa?a

Phunzirani Zambiri

Popeza kamtsikana ka ku Isiraeli sikanatchulidwe dzina, kodi zimenezi zikusonyeza kuti Yehova ankakaona kuti ndi kosafunika?

“N’chifukwa Chiyani Anthu Ena Otchulidwa M’Baibulo Sanatchulidwe Mayina Awo?” (w13 8/1 10)

Onani mmene ana masiku ano angasonyezere kulimba mtima ngati kamtsikana ka ku Isiraeli.

Yehova Akuthandiza Kuti Ukhale Wolimba Mtima (11:59)

a Ngati mtsikanayu anakula n’kukhala munthu wamkulu, ndiye kuti adzaukitsidwa ali mzimayi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena