Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 4/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Baibulo—Buku Lomwe Linalembedwa Kuti Limvetsetsedwe
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Kodi Mulungu Amalankhula Nafe Motani?
    Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Kusamvetsa Zinthu Kukhoza Kutipweteketsa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kuphunzitsidwa ndi Mulungu?
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 4/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi N’zotheka Kumvetsa Bwino Zimene Baibulo Limaphunzitsa?

Baibulo ndi Mawu a Mulungu. Lili ngati kalata yochokera kwa bambo wachikondi. (2 Timoteyo 3:16) M’Baibulo, Mulungu anatifotokozera zimene tingachite kuti tizimusangalatsa, chifukwa chake walola kuti padzikoli pakhale mavuto komanso zimene adzachitire anthu m’tsogolo. Koma aphunzitsi achipembedzo amapotoza zimene Baibulo limaphunzitsa ndipo izi zachititsa kuti anthu ambiri aziona kuti n’zosatheka kumvetsa bwino Baibulo.—Machitidwe 20:29, 30.

Yehova Mulungu amafuna kuti tidziwe zoona zokhudza iyeyo. N’chifukwa chake anatipatsa buku lonena za iye, lomwe ndi losavuta kumvetsa.—Werengani 1 Timoteyo 2:3, 4.

Kodi mungatani kuti muzilimvetsa bwino Baibulo?

Sikuti Yehova anangotipatsa Baibulo. Iye amatithandizanso kuti tilimvetse ndipo n’chifukwa chake anatumiza Yesu kuti adzatiphunzitse. (Luka 4:16-21) Yesu ankafotokoza kugwirizana kwa mavesi ndipo izi zinathandiza anthu kumvetsa Malemba.—Werengani Luka 24:27, 32, 45.

Yesu anakhazikitsa mpingo wachikhristu kuti upitirize kugwira ntchito imene anayambitsa. (Mateyu 28:19, 20) Masiku ano otsatira a Yesu enieni amathandiza anthu kumvetsa zimene Baibulo limaphunzitsa zokhudza Mulungu. Ngati mukufuna kumvetsa zimene Baibulo limaphunzitsa, a Mboni za Yehova ndi okonzeka kukuthandizani.—Werengani Machitidwe 8:30, 31.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena