Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb16 tsamba 130
  • Anachita Upainiya Wapadera kwa Zaka 50

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anachita Upainiya Wapadera kwa Zaka 50
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mpainiya Amachita Chiyani?
    Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
  • Kutumikira ndi LIngaliro la Kufulumira kwa Nthaŵi
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Madalitso a Utumiki Waupainiya
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Apainiya Amapereka ndi Kulandira Madalitso
    Nsanja ya Olonda—1994
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
yb16 tsamba 130

INDONESIA

Anachita Upainiya Wapadera kwa Zaka 50

Alisten Lumare

  • CHAKA CHOBADWA 1927

  • CHAKA CHOBATIZIDWA 1962

  • MBIRI YAKE Poyamba anali mkulu wa apolisi koma anakhala mpainiya wapadera kwa zaka zoposa 50.

M’bale Alisten Lumare

MU 1964, ndinaikidwa kukhala mpainiya wapadera pachilumba cha Manokwari ku West Papua. Mpingo womwe unali pachilumbachi unkatsutsidwa kwambiri ndi atsogoleri achipembedzo. Nditangofika kumene, m’busa wina watchalitchi chachipulotesitanti anafika kunyumba kwanga atakwiya.

Iye anayankhula mwaukali kuti: “Ndigwetsa nyumba yakoyi komanso ndithetsa gulu la Mboni za Yehova ku Manokwari kuno.”

Chifukwa cha zimene ndinaphunzira ndili wapolisi, sindinachite mantha ndi zimene ananenazo. Ndinamuyankha mwaulemu ndipo ananyamuka n’kumapita.—1 Pet. 3:15.

Nthawi imeneyo ku Manokwari kunali ofalitsa 8 okha basi. Panopa padutsa zaka pafupifupi 50 ndipo tsopano kuli mipingo yokwana 7. M’chaka cha 2014, anthu oposa 1,200 anapezeka pamsonkhano womwe unachitika m’derali. Ndikaona mmene Yehova wathandizira anthu m’dera lakumudzi limeneli, ndimasangalala kwambiri.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena