LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 8
  • Vimphona Padziko Lapansi

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Vimphona Padziko Lapansi
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Cigumula ca Nowa—Ndani Anamvetsela? Ndani Sanamvetsele?
    Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
  • Mmene Angelo Angakuthandizileni
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Cigumula Cacikulu
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Cingalawa ca Nowa
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
Onaninso Zina
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 8

Nkhani 8

Vimphona Padziko Lapansi

NGATI waona munthu mutali wofika pamtenje wa nyumba abwela kwa iwe, kodi ungaganize ciani? Munthu ameneyo angakhale cimphona! Panthawi ina padziko lapansi panali vimphona. Baibo imakamba kuti Atate a vimphona vimenevi anali angelo amene anacokela kumwamba. Koma kodi zimenezi zinacitika bwanji?

Kumbukila kuti mngelo woipa, Satana, anali kupangitsa anthu kucita vinthu voipa. Anali kuyesa kunyengelela ngakhale angelo a Mulungu kuti nao azicita vinthu voipa. M’kupita kwa nthawi, ena mwa angelo amenewa anayamba kumvela Satana. Iwo anasiya nchito imene Mulungu anawapatsa kumwamba. Anabwela pano padziko lapansi ndi kuvala matupi aumunthu. Kodi udziŵa cimene anacitila zimenezi?

Baibo imakamba kuti, ana a Mulungu amenewa anakhumbila akazi okongola pano padziko lapansi, ndipo anafuna kuti azikhala nao. Conco anabwela padziko lapansi ndi kukwatila akazi amenewa. Baibo imakamba kuti cimene angelo awa anacita cinali cinthu coipa kwambili, cifukwa Mulungu anapanga angelo kuti azikhala kumwamba.

Pamene angelo ndi akazi ao anayamba kubala ana, ana ao anali kuoneka osiyana. Mwina poyamba sanali kuoneka osiyana kwambili ndi ana ena. Koma io anali kukulila-kulila ndi kukhala amphamvu kwambili, mpaka anakhala vimphona.

Vimphona vimenevi vinali voipa kwambili. Cifukwa cakuti vinali vikulu-vikulu ndiponso vamphamvu kwambili, vinali kuvutitsa ndi kuvulaza anthu. Vinali kukakamiza anthu kuti akhale oipa monga mmene vinalili.

Panthawi imeneyi Inoki anali anamwalila kale. Koma panali munthu wina wabwino padziko lapansi. Munthu ameneyu dzina lake anali Nowa. Nthawi zonse iye anali kucita zimene Mulungu anali kumuuza.

Tsiku lina Mulungu anauza Nowa kuti nthawi yakuti iye aononge anthu onse oipa yafika. Koma Mulungu anakamba kuti adzapulumutsa Nowa, banja lake, ndi nyama zambili zosiyana-siyana. Tiye tione mmene Mulungu anacitila zimenezi.

Genesis 6:1-8; Yuda 6.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani