LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • es25 masa. 98-108
  • October

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • October
  • Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
  • Tumitu
  • Citatu, October 1
  • Cinayi, October 2
  • Cisanu, October 3
  • Ciŵelu, October 4
  • Sondo, October 5
  • Mande, October 6
  • Ciŵili, October 7
  • Citatu, October 8
  • Cinayi, October 9
  • Cisanu, October 10
  • Ciŵelu, October 11
  • Sondo, October 12
  • Mande, October 13
  • Ciŵili, October 14
  • Citatu, October 15
  • Cinayi, October 16
  • Cisanu, October 17
  • Ciŵelu, October 18
  • Sondo, October 19
  • Mande, October 20
  • Ciŵili, October 21
  • Citatu, October 22
  • Cinayi, October 23
  • Cisanu, October 24
  • Ciŵelu, October 25
  • Sondo, October 26
  • Mande, October 27
  • Ciŵili, October 28
  • Citatu, October 29
  • Cinayi, October 30
  • Cisanu, October 31
Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
es25 masa. 98-108

October

Citatu, October 1

Nzelu yocokela kumwamba . . . ndi yokonzeka kumvela.​—Yak. 3:17.

Kodi kukhala womvela kumakuvutani? Davide nayenso, zinali kumuvuta nthawi zina. Ndiye cifukwa cake anapemphela kuti: “Ndipatseni mtima wofunitsitsa kukumvelani.” (Sal. 51:12) Davide anali kukonda Yehova. Ngakhale n’telo, nthawi zina Davide zinali kumuvuta kuonetsa mtima womvela, ndipo ni mmenenso zilili kwa ise. Cifukwa ciyani? Coyamba, cifukwa cakuti tinatengela mzimu wa kusamvela kwa makolo athu. Caciŵili, Satana amayesetsa kutinyengelela kuti tipandukile Yehova mmene iye anacitila. (2 Akor. 11:3) Cacitatu, tikukhala m’dziko mmene khalidwe la kupanduka lili paliponse, ndipo “mpweya umenewu, kapena kuti kaganizidwe kameneka, tsopano kakugwila nchito mwa ana osamvela.” (Aef. 2:2) Tiyenela kucita zonse zothekha kuti tilimbane na ucimo, Satana, komanso dziko, kuti timvele Yehova komanso aja amene wapatsa ulamulilo. w23.10 6 ¶1

Cinayi, October 2

Iwe wasunga vinyo wabwino mpaka nthawi ino.​—Yoh. 2:10.

Kodi tiphunzilapo ciyani pa cozizwitsa ca Yesu cosandutsa madzi kukhala vinyo? Kukhala odzicepetsa. Yesu sanadzitame pa cozizwitsaco ayi. Ndipo sanadzitamepo pa zonse zimene anali kucita. M’malo mwake, nthawi zonse anali kudzicepetsa mwa kupeleka ulemu na ulemelelo kwa Atate wake. (Yoh. 5:19, 30; 8:28) Tikatengela citsanzo ca Yesu mwa kukhala odzicepetsa, sitidzadzitama pa zilizonse tingakwanitse kucita. Tisadzitame ayi, koma tidzitamandile kuti Mulungu wathu ni wabwino, ndipo tili na mwayi wom’tumikila. (Yer. 9:23, 24) Tizim’patsa ulemelelo wake. Ndi iko komwe, n’ciyani cabwino cimene tingakwanitse kucita popanda thandizo la Yehova? (1 Akor. 1:26-31) Ngati tikhala odzicepetsa, sitidzafuna kudzipezela ulemu pa zabwino zimene tacitila ena. Timakhutila kudziŵa kuti Yehova amaona komanso amayamikila zimene timacita. (Yelekezelani na Mateyu 6:2-4; Aheb. 13:16) Ndithudi, timakondweletsa Yehova tikamatengela Yesu poonetsa kudzicepetsa.​—1 Pet. 5:6. w23.04 4 ¶9; 5 ¶11-12

Cisanu, October 3

Musamaganizile zofuna zanu zokha, koma muziganizilanso zofuna za ena.​—Afil. 2:4.

Mouzilidwa na mzimu woyela, mtumwi Paulo analimbikitsa Akhristu kuti aziganizila zofuna za ena. Kodi tingatsatile motani uphungu umenewu pa misonkhano? Mwa kukumbukila kuti nawonso abale na alongo athu amafuna kupelekapo ndemanga. Ganizilani izi. Mukamaceza na mabwenzi anu, kodi mungamalankhule kwambili moti anzanuwo n’kusoŵa mpata wakuti alankhulepo? Ayi simungatelo. Mumafuna kuti nawonso azilankhulapo. Mofananamo, pamisonkhano tiyenela kusiyilako ena mpata wopelekapo ndemanga. Ndipo njila yabwino koposa yolimbikitsila abale na alongo athu, ni kuwapatsa mpata woonetsa cikhulupililo cawo. (1 Akor. 10:24) Ndemanga zathu zizikhala zazifupi, kuti ena azikhalanso na mpata wopelekapo ndemanga. Ngakhale popeleka ndemanga yaifupi, pewani kukamba mfundo zambili. Musacite kukombelatu mfundo zonse m’ndime, moti ena n’kusoŵa ndemanga yopelekapo. w23.04 22-23 ¶11-13

Ciŵelu, October 4

Ndimacita zinthu zonse cifukwa ca uthenga wabwino, kuti ndilalikile uthengawu kwa anthu ena.​—1 Akor. 9:23.

Zinthu zikasintha pa umoyo wathu, kuthandizabe ena n’kofunika kwambili, maka-maka mwa kulalikila. Tizikhala ololela pa utumiki wathu. Timakumana na anthu a zikhulupililo na maganizo osiyana-siyana, komanso ocokela kosiyana-siyana. Mtumwi Paulo anali wololela, ndipo tingatengeleko citsanzo cake. Yesu anaika Paulo kukhala ‘mtumwi wotumidwa kwa mitundu ina.’ (Aroma 11:13) Pa utumiki wake umenewo, Paulo analalikila kwa Ayuda, Agiriki, anthu ophunzila, alimi osauka, anyanchito a boma, komanso mafumu. Kuti awafike pa mtima anthu onsewo, Paulo ‘anakhala zinthu zonse kwa anthu osiyanasiyana.’ (1 Akor. 9:19-22) Poganizila cikhalidwe na zikhulupililo za anthu amene anali kuwalalikila, mtumwi Paulo anasintha njila yolalikila. Nafenso tingakhale alaliki ogwila mtima tikamakhala okonzeka kusintha ulaliki wathu kuti ugwilizane na munthu amene tapeza. w23.07 23 ¶11-12

Sondo, October 5

Kapolo wa Ambuye sayenela kukangana ndi anthu. Koma ayenela kukhala wodekha kwa onse.​—2 Tim. 2:24.

Munthu akakhala wofatsa sindiye kuti ni wofooka. Zimafuna mphamvu kuti munthu akhalebe wodekha akaputidwa. Kufatsa ni ‘khalidwe limene munthu amakhala nalo mothandizidwa na mzimu woyela.’ (Agal. 5:22, 23) Liwu la Cigiriki lomasulidwa kuti “kufatsa” nthawi zina anali kuliseŵenzetsa pofotokoza za hachi yakuchile imene yayamba kuwetedwa. Hachiyo imakhala yodekha koma imakhalabe yamphamvu. Nanga ife tingakulitse bwanji khalidwe la kufatsa, koma pa nthawi imodzimodzi n’kukhalanso olimba? Izi sizingatheke mwa mphamvu zathu zokha. Koma zingatheke mwa kupempha mzimu wa Mulungu kuti utithandize kukulitsa khalidwe limeneli. Pali umboni woonetsa kuti zimenezi n’zotheka. Mboni zambili zimayankha mofatsa anthu akaziputa. Kutelo kwathandiza anthu kukhala na kaonedwe kabwino ka gulu lathu.​—2 Tim 2:24, 25. w23.09 15 ¶3

Mande, October 6

Ndinkapempha . . . ndipo Yehova wandipatsa zimene ndinapempha.​—1 Sam. 1:27.

M’masomphenya ocititsa cidwi, mtumwi Yohane anaona akulu 24 akulambila Yehova kumwamba. Iwo anatamanda Mulungu poona kuti ni woyenela kulandila “ulemelelo, ulemu ndi mphamvu.” (Chiv. 4:10, 11) Angelo okhulupilika nawonso ali na zifukwa zambili zotamandila Yehova na kum’lemekeza. Iwo amakhala naye kumwamba, ndipo anafika pom’dziŵa bwino kwambili. Amaona makhalidwe ake mwa zocita zake. Conco, amasonkhezeledwa kum’tamanda. (Yobu 38:4-7) Nafenso tizitamanda Yehova m’mapemphelo athu, mwa kuchula zimene timakonda komanso zimene timayamikila zokhudza iye. Pamene muŵelenga na kuphunzila Baibo, muziyesa kupeza makhalidwe a Yehova amene amakukhudzani mtima. (Yobu 37:23; Aroma 11:33) Kenako, muuzeni Yehova mmene mumamvela za makhalidwe akewo. Tingam’tamandenso cifukwa amatithandiza, komanso amathandiza abale na alongo athu.​—1 Sam. 2:1, 2. w23.05 3-4 ¶6-7

Ciŵili, October 7

Mukhale ndi khalidwe logwilizana ndi zimene Yehova amafuna.​—Akol. 1:10.

Mu 1919, anthu a Mulungu anamasuka ku Babulo Wamkulu. M’caka cimeneco, “kapolo wokhulupilika komanso wanzelu” anaikidwa kuti athandize anthu oona mtima kuyenda pa “Msewu wa Ciyelo” wamakono. (Mat. 24:45-47; Yes. 35:8) Nchito yokonza msewu umenewo imene amuna okhulupilika anagwila kalelo, ikuthandiza anthu oyenda pa msewu waukuluwo kuti adziŵe zambili zokhudza colinga ca Yehova. (Miy. 4:18) Iwo amathanso kusintha umoyo wawo kuti ugwilizane na miyeso ya Yehova. Yehova sayembekezela anthu ake kupanga masinthidwe onse panthawi imodzi. M’malo mwake, iye wakhala akuyenga anthu ake pang’ono-pang’ono. Tonsefe tidzakhala okondwa panthawi imene zocita zathu zonse zizikondweletsa Mulungu wathu! Kucokela mu 1919, nchito yokonza “Msewu wa Ciyelo” yakhala ikucitika, kuti anthu ambili acoke m’Babulo Wamkulu. w23.05 17 ¶15; 19 ¶16

Citatu, October 8

Sindidzakusiyani.​—Aheb. 13:5.

Bungwe Lolamulila lakhala likuphunzitsa mwacindunji owathandiza m’makomiti awo osiyana-siyana. Abale othandiza amenewa akusenza maudindo akulu-akulu mokhulupilika. Iwo aphunzitsidwa bwino kuti apitilize kugwila nchito yosamalila nkhosa za Khristu. Odzozedwa akadzatha onse kutengedwa kupita kumwamba, cakumapeto kwa cisautso cacikulu, kulambila koyela kudzapitilizabe pano padziko lapansi. Ndife oyamikila kuti utsogoleli wa Khristu udzathandiza kuti olambila Mulungu adzapitilize kumulambila mokhulupilika. N’zoona kuti panthawiyo Gogi wa Magogi adzatiukila, amene ni mgwilizano wankhanza wa mitundu. (Ezek. 38:18-20) Koma kutiukila kwa kanthawi kumeneku sikudzapambana; sikudzalepeletsa anthu a Mulungu kulambila Yehova. Iye adzawapulumutsa ndithu! M’masomphenya, mtumwi Yohane anaona “khamu lalikulu” lomwe ni gulu la nkhosa zina za Khristu. Yohane anauzidwa kuti “khamu lalikulu” limeneli ‘latuluka m’cisautso cacikulu.’ (Chiv. 7:9, 14) Inde, iwo adzatetezedwa! w24.02 5-6 ¶13-14

Cinayi, October 9

Musazimitse moto wa mzimu.​—1 Ates. 5:19.

Kodi tingatani kuti tilandile mzimu woyela? Mwa kuupempha, kuŵelenga Mawu a Mulungu ouzilidwa, komanso kugwilizana na gulu limene amalitsogolela na mzimu wake. Tikatelo, timakhala na “makhalidwe amene mzimu woyela umatulutsa.” (Agal. 5:22, 23) Mulungu amapatsa mzimu wake anthu okhawo oganiza bwino, komanso a khalidwe loyela. Iye sangapitilize kutipatsa mzimu woyela ngati tikhalabe na maganizo oipa. (1 Ates. 4:7, 8) Kuti tizilandilabe mzimu woyela, tiyenela kupewa ‘kunyoza mawu aulosi.’ (1 Ates. 5:20) Pa lembali, liwu lakuti ‘ulosi’ litanthauza mauthenga ouzilidwa na mzimu wa Mulungu. Aphatikizapo onena za tsiku la Yehova komanso masiku athu ano. Sitikankhila tsikulo kutsogolo, poganiza kuti Aramagedo sidzabwela pamene tili moyo. M’malo mwake, timakhalabe na makhalidwe abwino, komanso kutangwanika na ‘nchito zosonyeza kuti ndife odzipeleka kwa Mulungu.’​—2 Pet. 3:11, 12. w23.06 12 ¶13-14

Cisanu, October 10

Kuopa Yehova ndi ciyambi ca nzelu.​—Miy. 9:10.

Pokhala Akhristu, kodi tiyenela kucita ciyani zithunzi zamalisece zikaonekela pa cipangizo cathu? Tisaziyang’ane ngakhale pang’ono! Cingatithandize kutelo ni kukumbukila kuti ubale wathu na Yehova ni wamtengo wapatali. Ndipo ngakhale zithunzi zimene si zamalisece kwenikweni zingadzutse cilakolako ca kugonana. N’cifukwa ciyani nazonso tiyenela kuzipewa? Cifukwa sitifuna ngakhale pang’ono kuganizila zocita zaciwelewele. (Mat. 5:28, 29) Mkulu wina ku Thailand dzina lake David anati: “Nimadzifunsa kuti: ‘Olo kuti zithunzi zimenezi si zamalisece kwenikweni, kodi Yehova angakondwele nikapitiliza kuziyang’ana?’ Funso ngati limeneli limanithandiza kucita mwanzelu.” Mantha oyenela oopa kukhumudwitsa Yehova, amatithandiza kucita mwanzelu. Mantha aumulungu otelo ndiwo “ciyambi ca nzelu.” w23.06 23 ¶12-13

Ciŵelu, October 11

Inu anthu anga, pitani mukalowe mʼzipinda zanu zamkati.​—Yes. 26:20.

“Zipinda zamkati” zingaimile mipingo yathu. Pa cisautso cacikulu, Yehova adzatiteteza tikapitilizabe kum’lambila pamodzi na Akhristu anzathu. Cotelo, tiyenela kuyesetsa pali pano kukulitsa cikondi pa abale na alongo athu. Cipulumutso cathu cingadzadalile cikondi cathu pa iwo. “Tsiku lalikulu la Yehova” lidzakhala nthawi yovuta kwa anthu. (Zef. 1:14, 15) Nawonso atumiki a Yehova adzakumana na mavuto. Koma tikakonzekela pali pano, tidzakhalabe odekha na kuthandiza anthu ena. Tidzatha kupilila mavuto alionse amene tingadzakumane nawo. Okhulupilila anzathu akadzakumana na mavuto, tidzawaonetsa cifundo popeleka thandizo lofunikila kwa iwo. Ndipo tikaphunzila kuonetsa cikondi abale na alongo athu pali pano, cidzakhala capafupi kudzagwilizana nawo kwambili pa nthawi zovuta m’tsogolomu. Pamapeto pake, Yehova adzatifupa potipatsa moyo wosatha m’dziko limene matsoka na masautso adzakhala mbili yakale.​—Yes. 65:17. w23.07 7 ¶16-17

Sondo, October 12

[Yehova] adzakupatsani mphamvu, adzakuthandizani kuti mukhalebe okhulupilika komanso adzakulimbitsani.​—1 Pet. 5:10.

Nthawi zambili Mawu a Mulungu amachula anthu okhulupilika kuti ni amphamvu. Koma ngakhale aja amene anali amphamvu kwambili si nthawi zonse pamene anali kudzimva telo. Nthawi zina Mfumu Davide anali kudzimva “wamphamvu ngati phili,” koma nthawi zina anali kudzimva wofooka ndipo anali “kucita mantha.” (Sal. 30:7) Ngakhale kuti Samisoni anali na mphamvu zapadela pamene mzimu wa Mulungu unali kugwila nchito pa iye, iye anazindikila kuti popanda mphamvu zocokela kwa Mulungu ‘angafooke ndi kukhala ngati anthu ena onse.’ (Ower. 14:5, 6; 16:17) Amuna okhulupilika amenewa anali olimba cifukwa Yehova ndiye anawapatsa mphamvu. Mtumwi Paulo anadziŵa kuti nayenso anafunikila mphamvu zocokela kwa Yehova. (2 Akor. 12:9, 10) Monga ambili a ife, mtumwi Paulo nayenso anali kulimbana na mavuto a thanzi. (Agal. 4:13, 14) Nthawi zina, zinalinso zovuta kuti acite coyenela. (Aroma 7:18, 19) Analinso kukhala na nkhawa pa zimene zidzamucitikila. (2 Akor. 1:8, 9) Komabe, pamene anali wofooka, m’pamene anali kukhala wamphamvu. Motani? Cifukwa Yehova anam’patsa mphamvu zimene anali kufunikila kuti apilile mavuto ake. w23.10 12 ¶1-2

Mande, October 13

Yehova amaona mumtima.​—1 Sam. 16:7.

Ngati nafenso nthawi zina timavutika na maganizo odziona wacabe-cabe, tizikumbukila kuti Yehova anatikokela kwa iye mwa kufuna kwake. (Yoh. 6:44) Amaona zabwino mwa ife, zimene ife sitingaone. Ndipo amaudziŵa bwino mtima wathu. (2 Mbiri 6:30) Conco tiyenela kukhulupilila akatiuza kuti ndife a mtengo wapatali. (1 Yoh. 3:19, 20) Ena a ife tisanaphunzile coonadi, tinacitapo zinthu zimene ngakhale pali pano timadziimba nazo mlandu. (1 Pet. 4:3) Ngakhale Akhristu okhulupilika amalimbanabe na zifooko. Kodi mtima wanu umakuimbani mlandu? Ngati n’telo, pezani cilimbikitso podziŵa kuti atumiki okhulupilika a Yehova amakumananso na vuto limeneli. Mwacitsanzo, mtumwi Paulo anadziona wolephela atakumbukila zophophonya zake. (Aroma 7:24) N’zoona kuti iye anali atalapa macimo ake na kubatizika. Ngakhale n’telo, ponena za iye mwini, anati anali “wamng’ono kwambili pa atumwi onse,” komanso kuti anali “wocimwa kwambili.”​—1 Akor. 15:9; 1 Tim. 1:15. w24.03 27 ¶5-6

Ciŵili, October 14

Iwo anasiya nyumba ya Yehova.​—2 Mbiri 24:18.

Phunzilo limodzi limene tingatengepo pa cisankho coipa ca Mfumu Yehoasi n’lakuti tiyenela kusankha mabwenzi amene amakonda Yehova, komanso amene amafuna kumukondweletsa. Mabwenzi aconco angatithandize kucita zinthu mwanzelu. Sitiyenela kusankha anthu a msinkhu wathu okha-okha kukhala mabwenzi athu. Kumbukilani kuti Yehoasi anali wamng’ono kwambili poyelekezela na mnzake Yehoyada. Ponena za mabwenzi anu, dzifunseni kuti: ‘Kodi amanithandiza kulimbikitsa cikhulupililo canga mwa Yehova? Kodi amanilimbikitsa kutsatila miyeso ya Yehova? Kodi amakonda kukamba za Yehova na coonadi cake ca mtengo wapatali? Kodi amalemekeza miyeso ya Mulungu? Kodi amangoniuza zonikomela m’khutu, kapena amalimba mtima na kuniwongolela nikalakwitsa?’ (Miy. 27:5, 6, 17) Kunena zoona, ngati mabwenzi anu sakonda Yehova, pezani ena. Koma ngati amakonda Yehova, akangamileni​—cifukwa adzakuthandizani ngako!​—Miy. 13:20. w23.09 9-10 ¶6-7

Citatu, October 15

Ine ndine Alefa ndi Omega.​—Chiv. 1:8

Cilembo ca Alefa n’coyamba mu alifabeti ya Cigiriki, pamene cilembo ca Omega n’cothela. Podzifotokoza kuti iye ni “Alefa komanso Omega,” Yehova akumveketsa mfundo yakuti akayamba kucita cinacake amapitilizabe mpaka atacimalizitsa. Yehova atalenga Adamu na Hava, anawauza kuti: “Mubelekane, muculuke, mudzaze dziko lapansi, ndipo muliyang’anile.” (Gen. 1:28) Pa nthawi imeneyo, zinali ngati Yehova akunena kuti “Alefa.” Anafotokoza colinga cake momveka bwino. Nthawi inali kudzafika pamene ana angwilo komanso omvela a Adamu na Hava anali kudzadzaza dziko lapansi na kulisandutsa kukhala Paradaiso. Pa nthawi yam’tsogolo imeneyo, tinganene kuti Yehova adzati “Omega.” Atamaliza kulenga “kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse za mmenemo,” Yehova anapeleka citsimikizo. Yehova anatsimikizila kuti adzakwanilitsa colinga cake kwa mtundu wa anthu komanso dziko lapansi. Colinga cake cinali kudzakwanilitsidwa kumapeto kwa tsiku la 7.​—Gen. 2:1-3. w23.11 5 ¶13-14

Cinayi, October 16

Konzani njila ya Yehova! Mulungu wathu mukonzeleni msewu wowongoka wodutsa mʼcipululu.​—Yes. 40:3.

Ulendo wocoka ku Babulo kupita ku Isiraeli unali kutenga miyezi inayi. Ulendowo unali na zovuta zake, koma Yehova analonjeza kuti adzacotsa zovutazo zimene zikanawalepheletsa kubwelela kwawo. Ayuda okhulupilika anadziŵa kuti akabwelela ku Isiraeli, adzapeza madalitso oculuka kuposa zimene angasiye ku Babulo. Dalitso lalikulu kwambili linali lokhudza kulambila kwawo. Kunalibe kacisi wa Yehova ku Babulo. Kunalibenso guwa la nsembe limene Aisiraeli akanapelekelapo nsembe malinga na Cilamulo ca Mose. Komanso kunalibe ansembe olinganizidwa owathandiza kupeleka nsembezo. Kuwonjezela apo, anthu a Yehova anali kukhala pakati pa anthu ambili amene sanali kulemekeza Yehova kapena miyeso yake. Conco, Ayuda masauzande amene anali kuopa Yehova, anali kuyembekezela mwacidwi kubwelela ku dziko lawo kuti akabwezeletse kulambila koyela. w23.05 14-15 ¶3-4

Cisanu, October 17

Pitilizani kuyenda ngati ana a kuwala.​—Aef. 5:8.

Timafunikila thandizo la mzimu wa Mulungu kuti tipitilize kucita zinthu “ngati ana a kuwala.” Cifukwa ciyani? Cifukwa si copepuka kukhalabe woyela m’dziko lino lodzala na makhalidwe oipa. (1 Ates. 4:3-5, 7, 8) Mzimu woyela ungatithandize kugonjetsa maganizo a m’dzikoli amene amasemphana na kaganizidwe ka Mulungu. Mzimuwo ungatithandizenso kubala cipatso “ciliconse cabwino ndi ciliconse colungama.” (Aef. 5:9) Njila imodzi imene tingalandile mzimu woyela ni kuupempha. Yesu ananena kuti Yehova “adzapeleka mowolowa manja mzimu woyela kwa amene akumupempha.” (Luka 11:13) Timalandilanso mzimu woyela tikamatamanda Yehova capamodzi pa misonkhano yathu. (Aef. 5:19, 20) Cisonkhezelo cabwino cimene mzimu woyela umakhala naco pa ife cimatithandiza kukhala na umoyo wokondweletsa Mulungu. w24.03 23-24 ¶13-15

Ciŵelu, October 18

Pitilizani kupempha ndipo adzakupatsani. Pitilizani kufunafuna ndipo mudzapeza. Pitilizani kugogoda ndipo adzakutsegulilani.​—Luka 11:9.

Kodi mufunika kukulitsa kuleza mtima? Ngati n’telo, ipempheleleni nkhaniyo. Kuleza mtima ni cipatso cimene mzimu woyela umabala. (Agal. 5:22, 23) Conco, tiyenela kupempha mzimu woyela wa Yehova kuti utithandize kukulitsa cipatso cimeneci. Kuleza mtima kwathu kukakhala pa mayeso, ‘tidzapemphabe’ mzimu woyela kuti utithandize kukhala oleza mtima. (Luka 11:13) Tingapemphenso Yehova kuti atithandize kuona zinthu mmene iye amazionela. Pambuyo popemphela, tiyenela kuyesetsa kukhala oleza mtima tsiku lililonse. Tikamapemphela kwambili kuti tikhale oleza mtima, na kuyesetsa kukhala otelo, khalidweli lidzazika mizu mumtima mwathu. Ndipo lidzakhala umunthu wathu. Zingakhalenso zothandiza kusinkhasinkha zitsanzo za m’Baibo. M’Baibo muli zitsanzo zambili za anthu amene anali oleza mtima. Tikamasinkhasinkha zitsanzo zimenezo, tidzaphunzila mmene tingaonetsele kuleza mtima. w23.08 22 ¶10-11

Sondo, October 19

Muponye maukonde anu kuti muphe nsomba.​—Luka 5:4.

Yesu anam’tsimikizila mtumwi Petulo kuti Yehova adzam’thandiza. Iye ataukitsidwa, anacitanso cozizwitsa kwa Petulo na atumwi anzake powathandiza kupha nsomba. (Yoh. 21:4-6) Mosakayikila, cozizwitsa cimeneci cinatsimikizila Petulo kuti Yehova adzasamalila zosoŵa zake zakuthupi. N’kutheka kuti mtumwiyu anakumbukila mawu a Yesu akuti Yehova adzasamalila anthu amene ‘apitiliza kufuna-funa Ufumu coyamba.’ (Mat. 6:33) Izi zinapangitsa Petulo kuika utumikila patsogolo m’malo mwa nchito yake ya usodzi. Iye molimba mtima analalikila pa Pentekosite mu 33 C.E., ndipo anthu masauzande analabadila uthenga wabwino. (Mac. 2:14, 37-41) Pambuyo pake, iye anathandiza Asamariya na anthu amitundu ina kuphunzila za Khristu na kum’tsatila. (Mac. 8:14-17; 10:44-48) Zoonadi, Yehova anam’gwilitsa nchito kwambili pokoka anthu a mitundu yonse kuti abwele mu mpingo. w23.09 20 ¶1; 23 ¶11

Mande, October 20

Ngati simundiuza zimene ndalota nʼkundimasulila, ndikudulani nthulinthuli.​—Dan. 2:5.

Patapita zaka pafupifupi ziŵili Ababulo atawononga Yerusalemu, Mfumu Nebukadinezara ya Babulo inalota maloto othetsa nzelu okhudza cifanizilo cacikulu. Inaopseza kuti idzapha amuna onse anzelu, kuphatikizapo Danieli, akalephela kuiuza zimene yalota komanso kumasulila kwake. (Dan. 2:3-5) Danieli anacitapo kanthu mwamsanga, cifukwa anthu ambili akanaphedwa. Iye “anapita kwa mfumu kukapempha kuti imupatse nthawi kuti adzamasulile maloto ake.” (Dan. 2:16) Izi zinafuna kulimba mtima na cikhulupililo. Baibo siionetsa kuti Danieli anamasulilapo maloto m’mbuyomo. Iye anapempha anzake atatu, kuti “apemphele kwa Mulungu wakumwamba kuti awacitile cifundo ndi kuwaululila cinsinsi cimeneci.” (Dan. 2:18) Yehova anayankha mapemphelo awo, moti anathandiza Danieli kumasulila maloto a Nebukadinezara. Conco, Danieli na anzakewo sanaphedwe. w23.08 3 ¶4

Ciŵili, October 21

Amene adzapilile mpaka pamapeto ndi amene adzapulumuke.​—Mat. 24:13.

Mapindu a kuleza mtima. Tikakhala oleza mtima, timakhala acimwemwe komanso odekha. Izi zimathandiza kuti tikhale na thanzi labwinopo. Tikamalezela mtima anthu ena, timakhala nawo pa ubale wabwino. Mpingo umakhala wogwilizana kwambili. Ndipo wina akatikhumudwitsa, kusakwiya msanga kumatithandiza kupewa kuikulitsa nkhaniyo. (Sal. 37:8; Miy. 14:29) Koma coposa zonse, timatengela Atate wathu wakumwamba, ndipo timamuyandikila kwambili. Kuleza mtima ni khalidwe labwino zedi! Ngakhale kuti nthawi zina kuleza mtima kumavuta, Yehova angatithandize kukulitsa khalidwe limeneli. Ndipo pamene tikuyembekezela moleza mtima dziko latsopano, sitikayikila olo pang’ono kuti “diso la Yehova limayangʼana anthu amene amamuopa, amene amayembekezela cikondi cake cokhulupilika.” (Sal. 33:18) Conde, tisaleke kuvala kuleza mtima. w23.08 22 ¶7; 25 ¶16-17

Citatu, October 22

Cikhulupililo pacokha, ngati cilibe nchito zake, ndi cakufa.​—Yak. 2:17.

Yakobo anafotokoza kuti munthu angakambe kuti ali na cikhulupililo. Koma kodi nchito zake zigwilizana na cikhulupililoco? (Yak. 2:1-5, 9) Yakobo anachulanso za munthu yemwe anaona “m’bale kapena mlongo ali waumphawi ndipo alibe cakudya cokwanila pa tsikulo,” koma sanapeleke thandizo lofunikila. Munthuyo angakambe kuti ali na cikhulupililo, koma cifukwa cakuti sanacionetse na zocita zake, cikhoza kukhala copanda pake. (Yak. 2:14-16) Yakobo anaseŵenzetsa Rahabi monga citsanzo ca munthu amene anaonetsa cikhulupililo mwa nchito zake. (Yakobo 2:25, 26) Iye anamva za Yehova, ndipo anadziŵa kuti anali kuthandizila Aisiraeli. (Yos. 2:9-11) Anaonetsa cikhulupililo mwa nchito zake​—anateteza azondi aŵili aciisiraeli amene miyoyo yawo inali pa ciopsezo. Mwa izi, mkazi wopanda ungwilo ameneyu, komanso yemwe sanali Mwisiraeli n’komwe, anaonedwa kukhala wolungama monga zinalili kwa Abulahamu. Nkhani ya Rahabi itionetsa kufunika kokhala na cikhulupililo coonetsedwa na nchito zake. w23.12 5-6 ¶12-13

Cinayi, October 23

Muzike mizu ndiponso mukhale okhazikika pamaziko.​—Aef. 3:17.

Kwa ife Akhristu kungomvetsa ziphunzitso zoyambilila za m’Baibo si kokwanila. Mwathandizo la mzimu woyela, ndife ofunitsitsa kudziŵa “ngakhale zinthu zozama za Mulungu.” (1 Akor. 2:9, 10) Pa phunzilo la inu mwini, bwanji osadziikila colinga cophunzila mfudo zozama za mawu a Mulungu kuti mumuyandikile kwambili Yehova? Mwacitsanzo, mungafufuze mmene Yehova anaonetsela cikondi kwa atumiki ake akale na kuona mmene izi zionetsela kuti amakukondani. Mungafufuze za dongosolo la kulambila Yehova m’nthawi ya Aisiraeli na kuliyelekezela na dongosolo la masiku ano. Kapena mungaŵelenge mozama maulosi amene Yesu anakwanilitsa ali padziko lapansi. Mungapeze cimwemwe pophunzila nkhani zimenezi poseŵenzetsa Buku Lofufuzila Nkhani la Mboni za Yehova. Kucita phunzilo la Baibo la inu mwini mozama kudzalimbikitsa cikhulupililo canu na kukuthandizani ‘kum’dziŵadi Mulungu.’ Miy. 2:4, 5. w23.10 18-19 ¶3-5

Cisanu, October 24

Muzikondana kwambili cifukwa cikondi cimakwilila macimo oculuka.​—1 Pet. 4:8.

Mawu amene mtumwi Petulo anaseŵenzetsa akuti “kwambili” amatanthauza “kufutukula.” Mbali yaciŵili ya vesiyi ionetsa zimene zingacitike ngati timakondana kwambili. Timatha kukwilila macimo a abale. Tiyelekeze motele: Timagwila cikondi na manja aŵili monga nsalu imene ingatambasuke. Timaitambasula mpaka itaphimba, osati imodzi kapena aŵili, koma “macimo oculuka.” “Kuphimba” kutanthauza kukhululuka. Monga momwe nsalu ingaphimbile kusaoneka bwino kwa zinthu, cikondi naconso cimaphimba zifooko komanso kupanda ungwilo kwa ena. Cikondi cathu pa ena ciyenela kukhala cacikulu kuti tikwanitse kukhululukila zophophonya za okhulupilila anzathu, ngakhale kuti nthawi zina sicopepuka kutelo. (Akol. 3:13) Tikakwanitsa kukhululukila ena timaonetsa kuti cikondi cathu pa iwo n’colimba, ndiponso kuti tifuna kukondweletsa Yehova. w23.11 11-12 ¶13-15

Ciŵelu, October 25

Safani anayamba kuŵelengela mfumu bukulo.​—2 Mbiri 34:18.

Atakula, Mfumu Yosiya anayamba nchito yokonzanso kacisi. Nchitoyo ili mkati, “anapeza buku la Cilamulo ca Yehova lopelekedwa kudzela mwa Mose.” Atamva bukulo likuŵelengedwa, Yosiya anacitapo kanthu mwa kuyamba kutsatila zimene anali kuŵelenga m’bukulo. (2 Mbiri 34:14, 19-21) Kodi mumafuna kuŵelenga Baibo tsiku lililonse? Ngati munayamba kale, kodi zikuyenda bwanji? Kodi mumasungako mavesi ena amene angakuthandizeni pacanu? Ali na zaka ngati 39, Yosiya anapanga cisankho colakwika cimene cinam’tayitsa moyo wake. Anadzidalila m’malo modalila Yehova kuti amutsogolele. (2 Mbiri 35:20-25) Tiphunzilapo ciyani? Kaya tili na zaka zingati, kapena takhala tikuphunzila Baibo kwa nthawi yaitali bwanji, sitiyenela kuleka kumufuna-funa Yehova. Izi ziphatikizapo kupempha citsogozo cake nthawi zonse, kuphunzila Mawu ake, na kugwilitsa nchito ulangizi wa Akhristu okhwima. Tikamatelo, tidzapewa kupanga zisankho zolakwika, ndipo tidzakhala osangalala.​—Yak. 1:25. w23.09 12 ¶15-16

Sondo, October 26

Mulungu amatsutsa odzikuza, koma odzicepetsa amawasonyeza kukoma mtima kwake kwakukulu.​—Yak. 4:6.

Baibo imachula akazi ambili amene anali kum’konda Yehova na kum’tumikila. Iwo anali “ocita zinthu mosapitilila malile” komanso “okhulupilika m’zinthu zonse.” (1 Tim. 3:11) Kuwonjezela apo, alongo acitsikana angapeze zitsanzo zabwino za alongo okhwima mwauzimu zimene angatengele mumpingo mwawo. Inu alongo acitsikana, ganizilani zitsanzo za alongo okhwima mwauzimu amene mungatengeleko. Onani makhalidwe osililika amene ali nawo ndiyeno ganizilani mmene mungayaonetsele. Kudzicepetsa ni khalidwe lofunika kuti munthu akhale Mkhristu wokhwima. Mkazi akakhala wodzicepetsa, amasangalala na ubwenzi wabwino na Yehova komanso na anthu ena. Mwacitsanzo, mkazi wokonda Yehova amasankha kucilikiza lamulo la umutu limene Atate wake wakumwamba anakhazikitsa. (1 Akor. 11:3) Mfundo imeneyi imagwila nchito mumpingo komanso m’banja. w23.12 18-19 ¶3-5

Mande, October 27

Amuna azikonda akazi awo ngati mmene amakondela matupi awo.​—Aef. 5:28.

Yehova amayembekezela mwamuna kumukonda mkazi wake na kumusamalila kuthupi komanso kuuzimu. Kukhala oganiza bwino, kulemekeza akazi, komanso kukhala wodalilika, kungakuthandizeni mukadzakwatila. Mukakwatila, mungakhale tate. Mungaphunzile ciyani kwa Yehova pa nkhani yokhala tate wabwino? (Aef. 6:4) Yehova anauza mwana wake Yesu pa anthu kuti amamukonda komanso kuti amakondwela naye. (Mat. 3:17) Mukadzakhala tate muzikaonetsetsa kuti nthawi na nthawi mukuwatsimikizila ana anu kuti mumawakonda. Muzikawayamikila moona mtima pa zimene azikacita bwino. Atate amene amatengela citsanzo ca Yehova amathandiza ana awo kukhala Akhristu okhwima. Mungakonzekele pali pano udindo umenewu mwa kusamalila ena mwacikondi m’banja na mu mpingo komanso mwa kuwayamikila.​—Yoh. 15:9. w23.12 28-29 ¶17-18

Ciŵili, October 28

Mʼmasiku anu, [Yehova] adzacititsa kuti muzimva kuti ndinu otetezeka.​—Yes. 33:6.

Ngakhale kuti ndife atumiki okhulupilika a Yehova, nafenso timakumana na zovuta, komanso kudwala monga mmene zilili na anthu ena. Kuwonjezela apo, timafunikanso kupilila citsutso kapena mazunzo ocokela kwa anthu amene amadana na anthu a Mulungu. Ngakhale kuti Yehova satiteteza ku mavutowa, iye analonjeza kuti adzatithandiza. (Yes. 41:10) Na thandizo lake, tingakhalebe acimwemwe, kupanga zisankho zanzelu, komanso kukhalabe okhulupilika kwa iye ngakhale pomwe tikukumana na zinthu zovuta. Yehova analonjeza kutipatsa cimene Baibo imacha “mtendele wa Mulungu.” (Afil. 4:6, 7) Mtendele umenewu umatithandiza kukhala odekha, komanso a bata mu mtima cifukwa cokhala pa ubale wa mtengo wapatali na iye. Mtendele umenewu “anthu sangathe kuumvetsa”; ndipo ni wapadela kwambili kuposa mmene tingaganizile. Kodi munakhalapo wodekha pambuyo popemphela kwa Yehova mocokela pansi pa mtima? Munamva conco cifukwa iye anakupatsani “mtendele wa Mulungu.” w24.01 20 ¶2; 21 ¶4

Citatu, October 29

Moyo wanga utamande Yehova. Ciliconse ca mkati mwanga, citamande dzina lake loyela.​—Sal. 103:1.

Kukonda Mulungu kumasonkhezela anthu okhulupilika kulemekeza dzina lake na mtima wonse. Mfumu Davide anadziŵa kuti kutamanda dzina la Yehova kunali kutamanda Yehova iye mwini. Dzina la Yehova limaphatikizapo mbili yake. Limatikumbutsa za makhalidwe ake abwino, komanso zocita zake zocititsa cidwi. Davide anaona dzina la Atate wake kukhala loyela, ndipo analitamanda. Anacita zimenezi na ‘ciliconse ca mkati mwake’​—kutanthauza kuti na mtima wake wonse. Mofananamo, Alevi anatsogolela pa nchito yotamanda Yehova. Iwo anavomeleza modzicepetsa kuti mawu awo sakanakwanitsa kupeleka citamando coyenela kupatulika kwa dzinalo. (Neh. 9:5) Mosakaikila, mawu odzicepetsa acitamando amenewa, anakondweletsa mtima wa Yehova. w24.02 9 ¶6

Cinayi, October 30

Mulimonse mmene tapitila patsogolo, tiyeni tipitilize kupita patsogolo pocita zomwe tikucitazo.​—Afil. 3:16.

Mukalephela kukwanilitsa colinga cimene simukanacikwanitsa, Yehova sadzakuonani kuti ndinu wolephela. (2 Akor. 8:12) Mukalephelako nthawi zina, tengam’poni phunzilo Baibo imati: “Mulungu si wosalungama woti angaiŵale nchito yanu.” (Aheb. 6:10) Conco inunso musamaiŵale. Muziganizila zimene mwakwanilitsapo kale, monga kupalana ubwenzi na Yehova, kuuzako ena za iye, kapena kubatizika. Ngati munakwanilitsa zolinga zanu zauzimu kumbuyoku, n’zotheka kukwanilitsanso zolinga zimene muli nazo palipano. Mwa thandizo la Yehova, n’zotheka kukwanilitsa zolinga zanu. Pamene muyesetsa kukwanilitsa zolinga zanu, muzisangalala poona mmene Yehova akukuthandizilani kukwanilitsa colinga canu. (2 Akor. 4:7) Mukapanda kutopa, mudzalandila madalitso osaneneka.​—Agal. 6:9. w23.05 31 ¶16-18

Cisanu, October 31

Atatewo amakukondani cifukwa munandikonda ndipo mwakhulupilila kuti ine ndinabwela monga nthumwi ya Mulungu.​—Yoh 16:27.

Yehova amafuna-funa mipata yoonetsa anthu kuti amawakonda, komanso kuti amakondwela nawo. Malemba amakamba nthawi ziŵili pomwe Iye anauza Yesu kuti ni Mwana wake wokondedwa, ndiponso kuti amakondwela naye. (Mat. 3:17; 17:5) Kodi mungakonde kumva Yehova akukuuzani kuti amakondwela nanu? Yehova sakamba nafe mwacindunji masiku ano, koma amatelo kupitila m’Mawu ake. Timamva mawu a Yehova otitsimikizila kuti amakondwela nafe tikaŵelenga mawu a Yesu opezeka m’Mauthenga Abwino. Yesu anatengela bwino kwambili makhalidwe a Atate wake. Cotelo, tikamaŵelenga mawu a Yesu oonetsa kuti anali kuwakonda otsatila ake opanda ungwilo koma okhulupilika, zimakhala ngati tikumumva Yehova akutiuza mawu amenewo. (Yoh. 15:9, 15) Kukumana na mavuto si umboni wakuti Mulungu analeka kukondwela nafe. M’malo mwake, kumatipatsa mwayi woonetsa kuzama kwa cikondi cathu pa Mulungu, komanso kukula kwa cidalilo cathu mwa iye.​—Yak. 1:12. w24.03 28 ¶10-11

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani