LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 9/1 tsa. 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Kulambila Koona Mungakudziŵe Bwanji?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kodi Uthenga Wabwino Wonena za Cipembedzo ndi Uti?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kulambila Kumene Mulungu Amavomeleza
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Mmene Mungadziŵile Cipembedzo Coona
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 9/1 tsa. 16

Kuyankha Mafunso a M’baibulo

Kodi zipembedzo zonse zimalemekeza Mulungu?

Mukamamvetsela nkhani za padziko lonse, mwina mwaona kuti zinthu zoipa nthawi zina zimacitidwa m’dzina la cipembedzo. Zipembedzo zonse si zocokela kwa Mulungu woona. (Mateyu 7:15) Inde, anthu ambili asoceletsedwa.—Ŵelengani 1 Yohane 5:19.

Ngakhale zili conco, Mulungu amaona anthu oona mtima amene amakonda zabwino ndi coonadi. (Yohane 4:23) Mulungu akufuna kuti anthu otelo aphunzile coonadi ca Mau ake, Baibulo.—Ŵelengani 1 Timoteyo 2:3-5.

Kodi cipembedzo coona mungacidziŵe bwanji?

Yehova Mulungu akugwilizanitsa anthu ocokela m’zipembedzo zambili mwa kuwaphunzitsa coonadi komanso kukondana. (Mika 4:2, 3) Conco Akristu oona mungawadziwe mwa kuona mmene amaonetselana cikondi.—Ŵelengani Yohane 13:35.

Yehova Mulungu akugwilizanitsa anthu onse mwa kugwilitsila nchito kulambila koona.—Salimo 133:1.

Akristu oona amakhulupilila zimene Baibulo limanena ndipo amakhalanso moyo mogwilizana ndi zimene limanena. (2 Timoteyo 3:16) Iwo amalemekezanso dzina la Mulungu. (Salimo 83:18) Komanso amalengeza kuti Ufumu wa Mulungu ndiwo ciyembekezo cokha ca anthu. (Danieli 2:44) Iwo amatsatila citsanzo ca Yesu mwakuonetsa“kuwala” kwao ndipo zimenezi zimaonekela pamene acitila anansi ao zinthu zabwino. (Mateyu 5:16) Conco Akristu oona tingawadziŵe cifukwa ca cikondi cimene amaonetsa kwa anansi ao powacezela n’colinga cowauza uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu.—Ŵelengani Mateyu 24:14; Machitidwe 5:42; 20:20.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 15 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani