LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 March tsa. 7
  • Aisiraeli Anaiŵala Yehova

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Aisiraeli Anaiŵala Yehova
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Yehova Atumiza Yeremiya Kuti Akalalikile
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Yeremiya Sanaleke Kulankhula za Yehova
    Phunzitsani Ana Anu
  • Khalani Wolimba Mtima Monga Yeremiya
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 March tsa. 7

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | YEREMIYA 12-16

Aisiraeli Anaiŵala Yehova

Yeremiya anapatsiwa nchito yovuta imene inaonetsa kuti Yehova anali wotsimikiza kunyazitsa Ayuda onyada ndi ouma khosiwo powononga Yerusalemu wawo

Yeremiya anayenda kucokela ku Yerusalemu kupita ku Mtsinje wa Firate ndi kubwelelanso

Yeremiya anagula lamba wansalu

13:1, 2

  • Lamba wogwila m’ciuno anaimila ubale wolimba umene ukanakhalapo pakati pa Yehova na mtundu wa Aisiraeli

Yeremiya anatengela lamba uja ku mtsinje wa Firate

13:3-5

  • Kumeneko anabisa lambayo m’mphako ya cimwala na kubwelela ku Yerusalemu

Kenako, Yeremiya anabwelela ku mtsinje wa Firate kukatenga lambayo

13:6, 7

  • Lambayo anali atawonongeka

Yehova anafotokoza tanthauzo lake pambuyo pakuti Yeremiya wagwila nchito imene anapatsidwa

13:8-11

  • Kumvela na mtima wonse kumene Yeremiya anacita pankhani yooneka ngati yaing’ono kunathandiza kuti Yehova awafike pamtima anthu

KODI MUDZIŴA?

Msenga wocoka ku Yerusalemu kukafika ku Mtsinje wa Firate unali wa makilomita pafupi-fupi 500. Ulendo wonse wopita na kubwelela, Yeremiya anayenda msenga wa makilomita pafupi-fupi 2,000. Ayenela anayenda ulendowu kwa miyezi ingapo.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani