Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 December tsa. 5
UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Mbali Yatsopano pa Msonkhano wa Mkati mwa Wiki
Kuyambila mu January 2018, pa misonkhano ya mkati mwa wiki tizikambilananso mfundo zounikila, na zithunzi zocokela mu Baibo yophunzilila ya pa intaneti ya Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika (nwtsty), imene pakali pano tilibe m’Cinyanja. Mosakayikila, mbali yatsopanoyi izikuthandizani kwambili pokonzekela misonkhano. Koma maka-maka, idzakuthandizani kumuyandikila kwambili Yehova, Atate wathu wacikondi.