LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 December masa. 6-7
  • Chikondi Chenicheni

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Chikondi Chenicheni
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • 12 Zolinga
    Galamuka!—2018
  • Tetezani Cikwati Canu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Pezani Nzelu Zothandiza pa Umoyo pa JW.ORG
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 December masa. 6-7

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Chikondi Chenicheni

Colinga ca Yehova n’cakuti mgwilizano wa cikwati uzikhala kwa moyo wonse. (Gen. 2:22-24) Okwatilana angasankhe kusudzulana kokha ngati wina wacita cigololo. (Mal. 2:16; Mat. 19:9) Popeza Yehova amafuna kuti okwatilana azikhala acimwemwe, anapeleka mfundo zimene zingathandize Akhristu kusankha mwanzelu munthu womanga naye banja.—Mlal. 5:4-6.

MUTAMBILETU VIDIYO YAKUTI CHIKONDI CHENICHENI, KUTI MUKAYANKHE MAFUNSO AYA:

  • A Frank akukamba na mwana wawo, Liz

    N’cifukwa ciani uphungu wa m’bale Frank ndi mkazi wake Bonnie kwa mwana wawo Liz, unali wanzelu ndiponso wacikondi?

  • N’cifukwa ciani si canzelu kuganiza kuti mungam’sinthe munthu amene muli naye pa cibwenzi?

  • Ni malangizo anzelu ati amene m’bale Paul ndi mkazi wake anapatsa Liz?

  • Zack na Maggie ali pa msonkhano ya mpingo

    N’ciani cinayambitsa mavuto m’cikwati ca Zack na Maggie?

  • Liz na John ali pa msonkhano ya mpingo

    Kodi John na Liz anali na zolinga zauzimu ziti zofanana?

  • N’cifukwa ciani mufunika kudziŵa “munthu wobisika wamumtima” wa munthu wina musanapange naye lumbilo la cikwati? (1 Pet. 3:4)

  • Kodi cikondi ceni-ceni n’cotani? (1 Akor. 13:4-8)

N’kuti kumene Akhristu angapeze mfundo zina zokhudza kukhala pa cibwenzi?

  • Pa mavidiyo a pa JW Broadcasting a mutu wakuti Kukonzekera Kulowa M’banja (ku Chichewa)

  • Mu vidiyo ya pa JW.ORG yakuti Ndi Cikondi Ceni-ceni Kapena Kutengeka Maganizo Cabe?

  • M’buku lakuti Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, loyamba ndi laciŵili

  • Mu Buku Lofufuzila Nkhani la Mboni za Yehova (Pitani pa “Umoyo wa Banja,” kenako pa “Kukhala pa Cisumbali.”)

Nanga n’kuti kumene okwatilana angapeze malangizo othandiza?

  • Pa nkhani za pa JW.ORG m’Chichewa (Yendani pa ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > MALANGIZO OTHANDIZA BANJA LONSE.)

  • M’kabuku kakuti N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe

  • Book • M’buku lakuti Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja

  • Mu Buku Lofufuzila Nkhani la Mboni za Yehova (Pitani pa “Umoyo wa Banja,” kenako pa “Cikwati.”)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani