January 14-20
MACHITIDWE 23-24
Nyimbo 148 na Pemphelo
Mawu Oyamba (3 min. olo kucepelapo)
CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
‘Apatsidwa Mlandu Wakuti ni Wovutitsa Komanso Woukila Boma’: (10 min.)
Mac. 23:12, 16—Ciwembu cofuna kupha Paulo cinalepheleka (bt peji 191 pala. 5-6)
Mac. 24:2, 5, 6—Munthu wina wodziŵa kukamba wochedwa Teritulo ananeneza Paulo kwa Bwanamkubwa wa Roma (bt peji 192 pala. 10)
Mac. 24:10-21—Mwaulemu Paulo anadziteteza ndipo analalikila molimba mtima (bt mape. 193-194 mapa. 13-14)
Kufufuza Cuma ca Kuuzimu: (8 min.)
Mac. 23:6—N’cifukwa ciani Paulo anakamba kuti: “Ine ndine Mfarisi”? (“Ine ndine Mfarisi” nwtsty mfundo younikila)
Mac. 24:24, 27—Kodi Durusila anali ndani? (“Durusila” nwtsty mfundo younikila pa Mac. 24:24)
Kodi imwe pacanu, kuŵelenga Baibo kwa wiki ino kwakuphunzitsani ciani za Yehova?
Ni cuma ca kuuzimu cina citi cimene mwapeza pa kuŵelenga Baibo kwa wiki ino?
Kuŵelenga Baibo: (4 min. olo kucepelapo) Mac. 23:1-15 (th phunzilo 5)
CITANI KHAMA PA ULALIKI
Vidiyo ya Ulendo Woyamba: (4 min.) Tambitsani na kukambilana vidiyoyi.
Ulendo Woyamba: (2 min. olo kucepelapo) Seŵenzetsani makambilano acitsanzo. (th phunzilo 1)
Ulendo Woyamba: (3 min. olo kucepelapo) Mukayamba makambilano acitsanzo, mwininyumba akambe mawu ofala kwanuko amene anthu amakamba pokana kuwalalikila. Koma muyankheni mwaluso. (th phunzilo 2)
Ulendo Woyamba: (3 min. olo kucepelapo) Mukayamba makambilano acitsanzo, mwininyumba akambe mawu ofala kwanuko okanila ulaliki. Koma muyankheni mwaluso. (th phunzilo 3)
UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Lipoti la Caka ca Utumiki: (15 min.) Nkhani yokambiwa na mkulu. Pambuyo poŵelenga cilengezo cocokela ku ofesi ya nthambi cokhudza lipoti la caka ca utumiki, funsani mafunso ofalitsa amene anakonzekeletsedwa pasadakhale, kuti asimbe zocitika zolimbikitsa za mu ulaliki m’caka capita ca utumiki.
Phunzilo la Baibo la Mpingo: (30 min.) jy mutu 50
Kubwelelamo na Kuchulako za Wiki Yotsatila (3 min.)
Nyimbo 128 na Pemphelo