LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g20 na. 3 tsa. 3
  • Tsankho—Kodi Na Imwe Muli Nalo?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Tsankho—Kodi Na Imwe Muli Nalo?
  • Galamuka!—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Tikhale Amodzi, Monga Mmene Yehova na Yesu Alili Amodzi
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Onetsani Cikondi
    Galamuka!—2020
  • Maphunzilo Aumulungu Amagonjetsa Tsankho
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Dziŵani Zoona Zeni-zeni
    Galamuka!—2020
Onaninso Zina
Galamuka!—2020
g20 na. 3 tsa. 3
Anthu aŵili akuyenda moyang’anizana. Wina akuona kuti cithunzi-thunzi ca mnzake ni cocititsa mantha.

Tsankho Kodi Na Imwe Mungakhale Nalo?

Tsankho lili ngati matenda. Limawononga munthu amene ali nalo, ndipo nthawi zina munthu watsankho sazindikila kuti ali nalo.

Anthu amaonetsa tsankho kwa anthu cifukwa cosiyana dziko, mtundu, cinenelo, kapena cipembedzo. Enanso amaonetsa tsankho kwa anthu cifukwa si amuna kapena akazi anzawo, kapenanso cifukwa si olemela kapena osauka anzawo. Palinso ena amene amaona anthu molakwika cifukwa ca zaka zawo zakubadwa, maphunzilo awo, zilema zimene ali nazo, kapena cifukwa ca maonekedwe awo. Ngakhale n’telo, anthu otelo amadziona kuti alibe tsankho.

Kodi na imwe mungakhale na tsankho? Ambili a ife timakwanitsa kuona tsankho mwa ena. Koma cingakhale covuta kuzindikila kuti na ife tili nalo. Zoona n’zakuti tonsefe tiliko na tsankho pa mlingo winawake. Katswili wa cikhalidwe ca anthu, dzina lake David Williams anakamba kuti ngati anthu amauona molakwika mtundu winawake wa anthu, akakumana na munthu wocokela mu mtundu umenewo, “amacita naye zinthu mosiyanako, koma osazindikila ngakhale pang’ono kuti aonetsa tsankho.”

Mwacitsanzo, m’dziko lina ku Europe muli mtundu wina wocepa wa anthu. Ambili m’dzikolo sawakonda anthu ocokela mu mtundu umenewo. Jovica, amene akhala m’dzikolo, anati: “N’nali kuganiza kuti anthu onse a mtundu umenewo si abwino. Koma sin’nadziŵe kuti n’nali na tsankho, cifukwa n’nali kukhulupilila kuti ni mmenedi anthuwo alili.”

Maboma ambili amapanga malamulo oletsa kusankhana mitundu na makhalidwe ena atsankho. Ngakhale n’conco, khalidwe la tsankho likupitilizabe. Cifukwa ciani? Cifukwa malamulowo amangoletsa munthu kucita tsankho. Sangalamulile za m’maganizo na mumtima mwa munthu, mmene mumayambila tsankholo. Ndiye funso n’lakuti, kodi n’zothekadi kuthetsa tsankho? Kodi mankhwala othetsela tsankho aliko?

Nkhani zotsatila zifotokoza mfundo zisanu, zimene zathandiza anthu ambili kuthetsa tsankho mumtima na m’maganizo mwawo.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani