LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g20 na. 3 masa. 4-5
  • Dziŵani Zoona Zeni-zeni

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Dziŵani Zoona Zeni-zeni
  • Galamuka!—2020
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • Cifukwa Cake Zingakhale Zovuta
  • Mfundo ya m’Baibo
  • Kodi Kudziŵa Zoona Zeni-zeni Kumathandiza Bwanji?
  • Zimene Mungacite
  • Tsankho—Kodi Na Imwe Muli Nalo?
    Galamuka!—2020
  • Onetsani Cikondi
    Galamuka!—2020
  • Tikhale Amodzi, Monga Mmene Yehova na Yesu Alili Amodzi
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Anagonjetsa Tsankho
    Galamuka!—2020
Onaninso Zina
Galamuka!—2020
g20 na. 3 masa. 4-5
Amuna aŵili akufunsa mkazi mafunso oloŵela nchito pa fakitale yopangilapo mamotoka. Mkaziyo akuoneka wokhumudwa.

Dziŵani Zoona Zeni-Zeni

Cifukwa Cake Zingakhale Zovuta

Tsankho limayamba cifukwa cakuti munthu anamvela kapena kuuzidwa mfundo zabodza. Ganizilani zitsanzo izi:

  • Mabwana ena amakhulupilila kuti akazi sangakwanitse kugwila nchito zofuna luso lapadela, mphamvu zambili kapena kuganiza kwambili.

  • M’nthawi ya Europe wamakedzana, Ayuda anali kuwanamizila kuti anali kuthila poizoni m’zitsime na kuyambukiza anthu matenda. Mu ulamulilo wa Nazi, Ayuda anawanamizilanso. Koma panthawiyi anawanamizila kuti ndiwo anapangitsa mavuto azacuma m’dziko la Germany. Zocitika zonsezi zinapangitsa kuti Ayuda azisalidwa kwambili, ndipo zimenezi zimaonekela mpaka pano.

  • Anthu ambili amaganiza kuti munthu aliyense wolemala amakhala wosasangalala kapena wamkali.

Anthu amene amakhulupilila nkhambakamwa ngati zimenezi, angapeleke zitsanzo kapena mfundo zina zosadalilika zimene amati ni umboni wotsimikizila kuti maganizo awo ni olondola. Ndipo amaona kuti aliyense amene sagwilizana na maganizo awo ni wosadziŵa zinthu.

Mfundo ya m’Baibo

“Si bwino kuti munthu akhale wosadziwa zinthu.”—MIYAMBO 19:2.

Kodi Mfundo Imeneyi Itanthauza Ciani? Munthu amene sadziŵa zoona zeni-zeni, amapanga zosankha zolakwika. Ngati tikhulupilila mfundo zopanda umboni, tingayambe kuwaganizila molakwika anthu ena.

Kodi Baibo Imalimbikitsa Tsankho?

Anthu ena amakamba kuti Baibo imalimbikitsa tsankho. Koma kodi Baibo imakamba ciani kweni-kweni?

  • Anthu tonse tili pacibale: “Kucokela mwa munthu mmodzi [Mulungu] anapanga mtundu wonse wa anthu.”—Machitidwe 17:26.

  • Mulungu alibe tsankho: “Mulungu alibe tsankho. Iye amalandila munthu wocokela mu mtundu uliwonse, amene amamuopa ndi kucita cilungamo.”—Machitidwe 10:34, 35.

  • Mulungu amayang’ana mumtima, osati maonekedwe a munthu: “Munthu amaona zooneka ndi maso, koma Yehova amaona mmene mtima ulili.”—1 Samueli 16:7.a

a Baibo imakamba kuti dzina la Mulungu ni Yehova.

Kodi Kudziŵa Zoona Zeni-zeni Kumathandiza Bwanji?

Ngati tidziŵa zoona zeni-zeni ponena za anthu enaake, sitingathamangile kukhulupilila mabodza amene ena amakamba ponena za iwo. Ndipo tikadziŵa kuti zimene tinamva zokhudza gulu linalake la anthu n’zabodza, tingasinthe maganizo athu n’kuyamba kuwaona moyenela anthuwo.

Citsanzo ca Zocitika Zeni-Zeni: Jovica wa ku (Europe)

Jovica, amene tamugwilapo kale mawu m’magazini ino, anakamba kuti pamene anali kukula, kaŵili-kaŵili anali kumvela anthu akukamba zoipa ponena za anthu a mtundu winawake. Anali kumvelanso zimenezi m’manyuzi komanso m’mapulogilamu a pa TV. Iye anati: “Mumtima mwanga munadzazilatu tsankho. N’nafika poyamba kuwazonda anthu amenewo. Ndipo mumtima n’nali kuona kuti panali poyenela kumvela mwanjila imeneyo.”

“Koma pamene n’nagena usilikali, panalibenso kucitila mwina koma kuyamba kuseŵenza na kukhala na asilikali ocokela mu mtundu umenewo. M’kupita kwa nthawi, n’nawadziŵa bwino. N’nayamba ngakhale kuphunzila citundu cawo, komanso kumvetsela nyimbo za cikhalidwe cawo. N’nayambanso kukondwela kukhala nawo pamodzi, ndipo n’naleka kuwaona molakwika. Ngakhale n’conco, nidziŵa kuti nthawi zina maganizo a tsankho angabwele mumtima. Conco, nimapewa kumvetsela nyuzi zoipitsa anthu a mtundu umenewo. Nimapewanso kumvetsela na kutamba mafilimu na maseŵela okamba nthabwala zonyoza anthu amenewo. Nidziŵa kuti tsankho limayambitsa mkwiyo na cidani.”

Zimene Mungacite

  • Olo ena akambe kuti anthu a mtundu wakuti-wakuti ali na khalidwe linalake loipa, kumbukilani kuti si anthu onse a mtunduwo ali na khalidwe limenelo.

  • Kumbukilani kuti pangakhale zambili zimene simudziŵa ponena za anthu ena.

  • Fufuzani ku magwelo odalilika kuti mudziŵe zoona zeni-zeni.

Anagonjetsa cidani

Zithunzi: 1. Anthu aŵili akukambilana pamene akuyenda. 2. Mmodzi wa iwo akumwetulila pamene ali na anzake.

N’ciani cinathandiza Mluya na Myuda wina kugonjetsa tsankho limene anali nalo?

Tambani vidiyo yakuti Kodi Cikondi Cidzagonjetsa Liti Cidani? Fufuzani vidiyo imeneyi pa jw.org mwa kulemba mutu umenewu pa batani lofufuzila.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani