LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 10/14 tsa. 2
  • Kufotokoza Zimene Timakhulupilila Zokhudza 1914

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kufotokoza Zimene Timakhulupilila Zokhudza 1914
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Nkhani Zothandiza mu Ulaliki
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Kodi Ufumu wa Mulungu Unayamba Liti Kulamulila? (Mbali 1)
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Ufumu wa Mulungu Ukulamulila Pali Pano!
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Umoyo Wabwino Koposa (The Best Life Ever)
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
Onaninso Zina
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 10/14 tsa. 2

LEMBA LA MWEZI: “LALIKILA MAU. LALIKILA MODZIPELEKA.”—2 Tim. 4:2.

Kufotokoza Zimene Timakhulupilila Zokhudza 1914

Malemba amatilimbikitsa ‘kukhala okonzeka kuyankha’ zimene timakhulupilila, “ndi mtima wofatsa ndiponso mwaulemu kwambili.” (1 Pet. 3:15) Kunena zoona, nthawi zina zingakhale zovuta kufotokoza mfundo zakuya za coonadi ca m’Baibulo, monga mfundo yokhudza mmene timadziŵila kuti Ufumu wa Mulungu unayamba kulamulila mu 1914. Pofuna kutithandiza kuyankha funso limeneli, pali nkhani ziŵili zimene zingatithandize za mutu wakuti, “Kukambilana Ndi Munthu Wina Nkhani za m’Baibulo—Kodi Ufumu wa Mulungu Unayamba Liti Kulamulila?” Nkhani zimenezi zipezeka m’magazini a Nsanja ya Mlonda amene tikugaŵila mu ulaliki m’miyezi ya October ndi November. Pamene muŵelenga nkhanizi, ganizilani mafunso otsatilaŵa ndi kuona mmene a Zulu, amene ndi wofalitsa m’nkhaniyo, anayambila makambilano ao.

Ndi motani mmene iye . . .

  • anayambila makambilano mwa kuyamikila munthu amene anali kuceza naye?—Mac. 17:22.

  • anaonetsela kudzicepetsa pofotokoza zimene amakhulupilila?—Mac. 14:15.

N’cifukwa ciani iye anacita bwino . . .

  • kuunikila mwacidule mfundo zimene akambilana asanapite pa mfundo ina?

  • kuyamba waima ndi kufunsa ngati mwininyumba anali kumvetsa zimene anali kukambilana?

  • kusafotokoza zambili pa nthawi imodzi?—Yoh. 16:12.

Tiyamikila kwambili Yehova ‘Mlangizi wathu Wamkulu’ potiphunzitsa mmene tingafotokozele bwino ziphunzitso zozama za coonadi ca m’Baibulo kwa amene ali ndi njala yakuuzimu.—Yes. 30:20.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani