LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 8/15 tsa. 1
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Phunzitsani Atsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Phunzitsani Atsopano
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Nkhani Zofanana
  • Atumiki a Uthenga Wabwino
    Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
  • Aphunzitseni Kutumikila Yehova Mosalekeza
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Pitilizani Kukhala Wacangu mu Utumiki
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Phunzilani kwa Ofalitsa Amene Atumikila Zaka Zambili
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
Onaninso Zina
Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
km 8/15 tsa. 1

Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Phunzitsani Atsopano

Cifukwa Cake Kuli Kofunika: Ophunzila a Yesu atsopano afunika kuphunzila ndi kusunga “zinthu zonse” zimene Yesu analamulila, kuphatikizapo kuphunzitsa ena coonadi. (Mat. 28:19, 20) Atsopano ambili avomelezedwa kuloŵa Sukulu ya Ulaliki ndipo mwina amacita ulaliki wamwai kwa a m’banja lao kapena kwa anzao. Iwo akamvetsetsa zimene akuphunzila ndi kuzindikila kuti Yehova afuna kuti anthu onse amve uthenga wabwino, amafunitsitsa kulalikila. (Aroma 10:13, 14) Atsopano akavomelezedwa kukhala ofalitsa osabatizidwa, afunika kuphunzitsidwa kuti asamadzikayikile pamene akuyesetsa kukula mwa kuuzimu.—Luka 6:40.

Mmene Tingacitile:

  • Thandizani wofalitsa watsopano kutenga zofalitsa zimene afuna kukagwilitsila nchito mu ulaliki. Muonetseni mmene mumalongela mabuku m’cola ca muulaliki, ndipo fotokozani colinga ca zofalitsa zimene mwanyamula

  • Capamodzi, sankhani ulaliki wacitsanzo mu Utumiki Wanthu wa Ufumu ndi kuyeseza ulalikiwo. Limbikitsani watsopanoyo kukamba ulaliki wacitsanzowo m’mau akeake. Mungayesezenso mitundu ya makambilano imene ili pa tsamba 82 m’buku la Sukulu ya Ulaliki imene ingagwile nchito m’dela lanu. Fotokonzani ubwino wa kuvala ndi kuzikongoletsa mwaulemu.—2 Akor. 6:3, 4.

  • M’phunzitseni zinthu zina zoonjezeleka.Muonetseni khadi la gawo ndi kumuuza molembela maina a anthu pa khadilo. M’phunzitseni mmene angaseŵezetsele webusaiti yathu ya jw.org ndi kabuku kakuti Uthenga Wabwino wa Anthu Amitundu Yonse mu ulaliki. Mulimbikitseni kukulitsa cidwi ca anthu amene wapeza.—1 Akor. 3:6

  • Khalani oleza mtima ndipo muzimuyamikila. (Miy. 25:11)Muzionetsa citsanzo cabwino. Khama lanu ndi kumuonetsa cidwi kumene mungacite kudzakhala ndi zotsatilapo zabwino mtsogolo.

Yesani Kucita Izi Mwezi Uno:

  • Pitani ndi wophunzila Baibulo wanu amene ndi wofalitsa watsopano mu ulaliki wa kunyumba ndi nyumba, kuulendo wobwelelako kapena ku phunzilo la Baibulo. Ngati mulibe phunzilo la Baibulo limene ndi wofalitsa watsopano, mungapemphe ofalitsa amene sanazoloŵele kugwila nchito yolalikila.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani