LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 September tsa. 7
  • Aphunzitseni Kutumikila Yehova Mosalekeza

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Aphunzitseni Kutumikila Yehova Mosalekeza
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Phunzitsani Atsopano
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Phunzilani kwa Ofalitsa Amene Atumikila Zaka Zambili
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Thandizani Maphunzilo Anu a Baibo Kuti Akakhale Ophunzila Obatizika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2021
  • Sukulu ya Ulaliki ya 2015 Idzatithandiza Kunola Luso Lathu Lophunzitsa
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 September tsa. 7

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Aphunzitseni Kutumikila Yehova Mosalekeza

Maumboni aonetsa kuti ofalitsa acatsopano akaphunzitsidwa kulalikila nthawi zonse, ndiponso mwacangu kucokela paciyambi, amadzakhala ofalitsa ocita bwino. (Miy. 22:6; Afil. 3:16) Munsimu muli malingalilo amene angakuthandizeni kuphunzitsa wophunzila wanu kukhala na ciyambi cabwino cokonda ulaliki:

  • Wophunzila wanu akangovomelezedwa kukhala wofalitsa, yambani kum’phunzitsa. (km 8/15 peji 1) M’thandizeni kuona kufunika kophatikiza ulaliki pa pulogilamu yake ya wiki iliyonse. (Afil. 1:10) Muzikamba zabwino zokhudza gawo lolalikilamo. (Afil. 4:8) M’limbikitseni kulalikilako na woyang’anila kagulu, na ofalitsa ena kuti atengeko maluso.—Miy. 1:5; km 10/12 peji 6 pala. 3

    M’bale athandiza wofalitsa watsopano kukonzekela ulaliki
  • Wophunzila wanu akabatizika, musaleke kum’limbikitsa na kum’phunzitsa ulaliki, maka-maka ngati sanatsilize kuphunzila buku lakuti “Khalanibe m’Cikondi.”—km 12/13 peji 7

    M’bale athandiza wofalitsa watsopano kukonzekela ulaliki
  • Polalikila na wofalitsa watsopano, muziseŵenzetsa ulaliki wosavuta. Pambuyo poona ulaliki wake, muyamikileni mocokela pansi pamtima. Pelekani malingalilo omuthandiza kukhala wofalitsa waluso.—km 5/10 peji 7

    Mwana na atate ŵake alalikila pamodzi
    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani