UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Dzikolo ‘Linameza Mtsinje’
Pa nthawi zosiyana-siyana m’mbili ya anthu, olamulila akhala akuthandiza anthu a Yehova. (Ezara 6:1-12; Esitere 8:10-13) Ngakhale masiku ano, timaona kuti “dziko” kapena kuti olamulila a dziko amaganizo abwino, amameza “mtsinje” wa cizunzo woyambitsidwa na “cinjoka,” cimene ni Satana Mdyelekezi. (Chiv. 12:16) Yehova, “Mulungu amene amatipulumutsa,” nthawi zina angaseŵenzetse olamulila kuti athandize anthu ake.—Sal. 68:20; Miy. 21:1.
Nanga bwanji ngati mwamangidwa cifukwa ca cikhulupililo canu? Musakayikile kuti Yehova akuona zimene zikukucitikilani. (Gen. 39:21-23; Sal. 105:17-20) Dziŵani kuti mudzadalitsidwa cifukwa ca cikhulupililo canu, komanso kuti kukhulupilika kwanu kumalimbikitsa abale padziko lonse.—Afil. 1:12-14; Chiv. 2:10.
TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI ABALE KU KOREA ATULUTSIDWA M’NDENDE, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:
N’cifukwa ciani kwa zaka zambili abale athu masauzande ku South Korea anali kumangidwa?
Ni ziweluzo zotani zimene khoti linapeleka kuti ena mwa abale athu amasulidwe mwamsanga?
Tingawathandize bwanji abale athu pa dziko lonse amene amangidwa cifukwa ca cikhulupililo cawo?
Kodi ufulu umene tili nawo tingauseŵenzetse bwanji?
N’ndani amapangitsa kuti tiwine milandu ku khoti?
Kodi ufulu wanga nimauseŵenzetsa bwanji?