LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 December tsa. 8
  • Dzikolo ‘Linameza Mtsinje’

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Dzikolo ‘Linameza Mtsinje’
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Alaliki a Ufumu Amapeleka Milandu Yao ku Khoti
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
  • Tizikumbukila Kupemphelela Akhiristu Anzathu Amene Akuzunzidwa
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Kucilikiza Boma la Mulungu Mokhulupilika
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
  • Tumikilani Yehova, Mulungu wa Ufulu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 December tsa. 8
Makalata ocokela ku bungwe la United Nations ovomeleza za kutulutsidwa m’ndende kwa Mboni za Yehova ku Korea, aikiwa patsogolo pa abale a ku Korea ovala vovala va ukaidi

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Dzikolo ‘Linameza Mtsinje’

Pa nthawi zosiyana-siyana m’mbili ya anthu, olamulila akhala akuthandiza anthu a Yehova. (Ezara 6:1-12; Esitere 8:10-13) Ngakhale masiku ano, timaona kuti “dziko” kapena kuti olamulila a dziko amaganizo abwino, amameza “mtsinje” wa cizunzo woyambitsidwa na “cinjoka,” cimene ni Satana Mdyelekezi. (Chiv. 12:16) Yehova, “Mulungu amene amatipulumutsa,” nthawi zina angaseŵenzetse olamulila kuti athandize anthu ake.—Sal. 68:20; Miy. 21:1.

Nanga bwanji ngati mwamangidwa cifukwa ca cikhulupililo canu? Musakayikile kuti Yehova akuona zimene zikukucitikilani. (Gen. 39:21-23; Sal. 105:17-20) Dziŵani kuti mudzadalitsidwa cifukwa ca cikhulupililo canu, komanso kuti kukhulupilika kwanu kumalimbikitsa abale padziko lonse.—Afil. 1:12-14; Chiv. 2:10.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI ABALE KU KOREA ATULUTSIDWA M’NDENDE, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • N’cifukwa ciani kwa zaka zambili abale athu masauzande ku South Korea anali kumangidwa?

  • Ni ziweluzo zotani zimene khoti linapeleka kuti ena mwa abale athu amasulidwe mwamsanga?

  • Tingawathandize bwanji abale athu pa dziko lonse amene amangidwa cifukwa ca cikhulupililo cawo?

  • Kodi ufulu umene tili nawo tingauseŵenzetse bwanji?

  • N’ndani amapangitsa kuti tiwine milandu ku khoti?

Ndende ya ku Korea, imene anali kusungilako Mboni za Yehova; makalata amene Mboni za Yehova zinatumiza ku ofesi ya Nthambi ya ku Korea, amene pambuyo pake anatumizidwa kwa abale amene anali m’ndende kumeneko; Tate na mwana akukumbatilana pamene aonananso

Kodi ufulu wanga nimauseŵenzetsa bwanji?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani