LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 August tsa. 3
  • Cilimikani Pamene Mapeto Ayandikila

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Cilimikani Pamene Mapeto Ayandikila
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Kulitsani Makhalidwe Aumulungu—Kulimba Mtima
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Kukhala Wolimba Mtima Sikovuta
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • ‘Limba Mtima, Ugwile Nchito Mwamphamvu’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
  • Nilimbitseni Mtima
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 August tsa. 3

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Cilimikani Pamene Mapeto Ayandikila

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Posacedwa, zocitika zocititsa mantha zidzatiika pa mayeso pankhani ya kulimba mtima kwathu na cidalilo cathu mwa Yehova kuposa kale lonse. Cisautso cacikulu cidzayamba na kuwonongedwa kwa cipembedzo conyenga. (Mat. 24:21; Chiv. 17:16, 17) Pa nthawi ya zocitika zimenezi, mwina tidzayamba kulalikila uthenga waciweluzo woŵaŵa. (Chiv. 16:21) Tidzaukilidwa na Gogi wa Magogi. (Ezek. 38:10-12, 14-16) Pofuna kuteteza anthu ake, Yehova adzabweletsa ‘nkhondo ya tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuyonse.’ (Chiv. 16:14, 16) Kuti tikhale olimba mtima kwambili poyembekezela zocitika za kutsogolo zimenezi, tifunika kukhala wokhulupilika pamene cikhulupililo cathu ciyesedwa pali pano.

MMENE TINGACITILE:

  • Molimba mtima sungani miyezo yapamwamba ya Yehova.—Yes. 5:20

  • Pitilizani kulambila pamodzi na Akhristu anzanu.—Aheb. 10:24, 25

  • Khalani okonzeka kumvela malangizo ocokela ku gulu la Yehova.—Aheb. 13:17

  • Sinkha-sinkhani mmene Yehova anapulumutsila anthu ake m’nthawi yakumbuyo.—2 Pet. 2:9

  • Pemphelani kwa Yehova, ndiponso mudalileni.—Sal. 112:7, 8

TAMBANI VIDIYO YAKUTI ZOCITIKA ZAM’TSOGOLO ZIMENE ZIDZAFUNA KULIMBA MTIMA—KAMBALI KAKE, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Zocitika Zam’tsogolo Zimene Zidzafuna Kulimba Mtima.’ Pa Nyumba ya Ufumu, mlongo akuyang’ana kutsogolo pambuyo powelenga cilengezo cofotokoza mpingo umene adzayamba kupita.

    Kodi ofalitsa anakumana na ciyeso cotani pankhani yakumvela pamene mpingo wawo unaphatikizidwa kumipingo ina?

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Zocitika Zam’tsogolo Zimene Zidzafuna Kulimba Mtima.’ Mlongo mmodzi-modziyo akambilana na alongo ena awili za kumpingo kumene adzayamba kupita.

    Kodi kulimba mtima na kumvela zigwilizana bwanji?

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Zocitika Zam’tsogolo Zimene Zidzafuna Kulimba Mtima.’ Wacicepele wada nkhawa pambuyo poona cithundzi coonetsa nkhondo ya aramagedo m’buku lakuti ‘Ufumu wa Mulungu Ukulamulila’

    N’cifukwa ciani kulimba mtima n’kofunika pamene Aramagedo ibwela?

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Zocitika Zam’tsogolo Zimene Zidzafuna Kulimba Mtima.’ Yehosafati pamodzi na anthu ena ocokela ku Yuda afika pa malo omenyela nkhonodo ndipo akupeza kuti palibe ngakhale mdani mmodzi amene ali moyo.

    Konzekelani pali pano zocitika za kutsogolo zimene zidzafuna kulimba mtima

    Ni nkhani iti m’Baibo imene ingatithandize kulimbitsa cikhulupililo cathu cakuti Yehova adzakwanitsa kutipulumutsa?—2 Mbiri 20:1-24

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani