LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb23 September tsa. 15
  • Makolo—Thandizani Ana Anu Kupeza Nzelu ya Umulungu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Makolo—Thandizani Ana Anu Kupeza Nzelu ya Umulungu
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Seŵenzetsani Mfundo za m’Baibo Pothandiza Ana Anu Kuti Apambane
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Zisankho Zimene Zimaonetsa Kuti Timadalila Yehova
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Anthu a “Maganizo Abwino” Adzalola Kuphunzira Nao
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Kufuna-funa Nzelu mwa Kuŵelenga Baibo Tsiku Lililonse
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
mwb23 September tsa. 15
Mlongo akuthandiza ana ake kuyankhapo komanso kumvetsela pa misonkhano ya mpingo.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Makolo—Thandizani Ana Anu Kupeza Nzelu ya Umulungu

Imodzi mwa njila zabwino zimene makolo angathandizile ana awo kupeza nzelu za umulungu ni kuwathandiza kupindula na misonkhano yacikhristu. Zimene acicepele amaona, kumva, komanso kukamba m’ndemanga zawo pa misonkhano, zimawathandiza kuphunzila za Yehova komanso kukhala bwenzi lake la pamtima. (Deut. 31:​12, 13) Ngati ndinu kholo, mungam’thandize bwanji mwana wanu kuti azipindula kwambili na misonkhano?

  • Muziyesetsa kupezeka pa misonkhano ya pamaso-mpamaso.—Sal. 22:22

  • Pezani nthawi yokhala na maceza olimbikitsa pa Nyumba ya Ufumu misonkhano isanayambe kapena pambuyo pake.—Aheb. 10:25

  • Onetsetsani kuti aliyense m’banja ali naco cofalitsa cimene cikuphunzilidwa pa misonkhano, kaya ca pacipangizo kapena copulintidwa

  • Thandizani mwana wanu kukonzekela ndemanga m’mawu ake-ake.—Mat. 21:​15, 16

  • Muzikamba zinthu zolimbikitsa ponena za misonkhano komanso zimene timaphunzila

  • Thandizani ana anu kugwilako nchito yoyeletsa Nyumba ya Ufumu komanso kuceza na acikulile a mumpingo mwanu

• Kuthandiza ana kuyandikila Yehova ni nchito yaikulu, ndipo nthawi zina ingaoneke yolemetsa kwambili. Komabe, dziŵani kuti Yehova adzakuthandizani.—Yes. 40:29.

ONELELANI VIDIYO YAKUTI MAKOLO, DALILANI YEHOVA NA MPHAMVU ZAKE, KENAKO YANKHANI MAFUNSO AWA:

  • Kodi kukhala olema kunam’khudza bwanji Zack na mkazi wake Leah?

  • N’cifukwa ciyani makolo ayenela kuyang’ana kwa Yehova kuti awapatse mphamvu?

  • Kodi Zack na Leah anadalila Yehova m’njila ziti kuti awathandize?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani