Ciŵelu, October 25
Safani anayamba kuŵelengela mfumu bukulo.—2 Mbiri 34:18.
Atakula, Mfumu Yosiya anayamba nchito yokonzanso kacisi. Nchitoyo ili mkati, “anapeza buku la Cilamulo ca Yehova lopelekedwa kudzela mwa Mose.” Atamva bukulo likuŵelengedwa, Yosiya anacitapo kanthu mwa kuyamba kutsatila zimene anali kuŵelenga m’bukulo. (2 Mbiri 34:14, 19-21) Kodi mumafuna kuŵelenga Baibo tsiku lililonse? Ngati munayamba kale, kodi zikuyenda bwanji? Kodi mumasungako mavesi ena amene angakuthandizeni pacanu? Ali na zaka ngati 39, Yosiya anapanga cisankho colakwika cimene cinam’tayitsa moyo wake. Anadzidalila m’malo modalila Yehova kuti amutsogolele. (2 Mbiri 35:20-25) Tiphunzilapo ciyani? Kaya tili na zaka zingati, kapena takhala tikuphunzila Baibo kwa nthawi yaitali bwanji, sitiyenela kuleka kumufuna-funa Yehova. Izi ziphatikizapo kupempha citsogozo cake nthawi zonse, kuphunzila Mawu ake, na kugwilitsa nchito ulangizi wa Akhristu okhwima. Tikamatelo, tidzapewa kupanga zisankho zolakwika, ndipo tidzakhala osangalala.—Yak. 1:25. w23.09 12 ¶15-16
Sondo, October 26
Mulungu amatsutsa odzikuza, koma odzicepetsa amawasonyeza kukoma mtima kwake kwakukulu.—Yak. 4:6.
Baibo imachula akazi ambili amene anali kum’konda Yehova na kum’tumikila. Iwo anali “ocita zinthu mosapitilila malile” komanso “okhulupilika m’zinthu zonse.” (1 Tim. 3:11) Kuwonjezela apo, alongo acitsikana angapeze zitsanzo zabwino za alongo okhwima mwauzimu zimene angatengele mumpingo mwawo. Inu alongo acitsikana, ganizilani zitsanzo za alongo okhwima mwauzimu amene mungatengeleko. Onani makhalidwe osililika amene ali nawo ndiyeno ganizilani mmene mungayaonetsele. Kudzicepetsa ni khalidwe lofunika kuti munthu akhale Mkhristu wokhwima. Mkazi akakhala wodzicepetsa, amasangalala na ubwenzi wabwino na Yehova komanso na anthu ena. Mwacitsanzo, mkazi wokonda Yehova amasankha kucilikiza lamulo la umutu limene Atate wake wakumwamba anakhazikitsa. (1 Akor. 11:3) Mfundo imeneyi imagwila nchito mumpingo komanso m’banja. w23.12 18-19 ¶3-5
Mande, October 27
Amuna azikonda akazi awo ngati mmene amakondela matupi awo.—Aef. 5:28.
Yehova amayembekezela mwamuna kumukonda mkazi wake na kumusamalila kuthupi komanso kuuzimu. Kukhala oganiza bwino, kulemekeza akazi, komanso kukhala wodalilika, kungakuthandizeni mukadzakwatila. Mukakwatila, mungakhale tate. Mungaphunzile ciyani kwa Yehova pa nkhani yokhala tate wabwino? (Aef. 6:4) Yehova anauza mwana wake Yesu pa anthu kuti amamukonda komanso kuti amakondwela naye. (Mat. 3:17) Mukadzakhala tate muzikaonetsetsa kuti nthawi na nthawi mukuwatsimikizila ana anu kuti mumawakonda. Muzikawayamikila moona mtima pa zimene azikacita bwino. Atate amene amatengela citsanzo ca Yehova amathandiza ana awo kukhala Akhristu okhwima. Mungakonzekele pali pano udindo umenewu mwa kusamalila ena mwacikondi m’banja na mu mpingo komanso mwa kuwayamikila.—Yoh. 15:9. w23.12 28-29 ¶17-18