LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w18 July tsa. 32
  • Mafunso Ocokela Kwa Oŵelenga

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mafunso Ocokela Kwa Oŵelenga
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Kusunga Mtendele na Ciyelo ca Mpingo
    Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
w18 July tsa. 32

Mafunso Ocokela Kwa Oŵelenga

Ngati mwamuna na mkazi osakwatilana anakhala m’nyumba imodzi usiku wonse popanda zifukwa zomveka, kodi lingakhale chimo lofunika komiti yaciweluzo?

Mamotoka aŵili awaimika panja usiku pa nyumba yogona

Inde, ngati palibe zifukwa zomveka zimene anacitila zimenezo, komiti yaciweluzo ingapangidwe cifukwa umenewo ni umboni wamphamvu woonetsa kuti anthuwo anacita ciwelewele.—1 Akor. 6:18.

Bungwe la akulu limapenda mosamala nkhaniyo kuti lidziŵe ngati komiti yaciweluzo ifunika kupangidwa. Mwacitsanzo: Kodi anthuwo ali pa cibwenzi? Kodi anapatsidwapo uphungu wokhudza mmene amacitila zinthu kwa wina na mnzake? Kodi n’zocitika zanji zimene zinapangitsa kuti akhale m’nyumba imodzi usiku wonse? Kodi zinali zocita kukonzekela? Kodi anacita mwadala, kapena panali zifukwa zomveka, monga zinthu zosayembekezeleka kapena zakugwa mwadzidzidzi zimene zinapangitsa kuti asacitile mwina koma kukhala m’nyumba imodzi usiku wonse? (Mlal. 9:11) Kodi anagona m’cipinda cimodzi kapena zosiyana? Popeza zocitika zimasiyana-siyana, pangakhalenso mfundo zina zimene akulu angapende.

Pambuyo pofufuza zeni-zeni zimene zinacitika, bungwe la akulu lidzaona ngati anthuwo ni ofunika kuwapangila komiti yaciweluzo kapena ayi.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani