Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 21:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Munthu aliyense mwa ana a Aroni wansembe, amene ali ndi chilema, asayandikire guwa lansembe kudzapereka nsembe yotentha ndi moto kwa Yehova.+ Iye ali ndi chilema. Asayandikire guwa lansembe kudzapereka mkate wa Mulungu wake.+

  • Numeri 16:40
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 40 Eleazara anachita izi kuti timalatato tikhale chikumbutso kwa ana a Isiraeli, kuti munthu aliyense amene si mbadwa+ ya Aroni asayandikire kwa Yehova+ kukafukiza nsembe. Anateronso kuti pasapezeke wina aliyense wochita zimene Kora limodzi ndi gulu lake+ anachita. Eleazara anachita zonse monga mmene Yehova anamuuzira kudzera kwa Mose.

  • Numeri 18:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Aleviwo azichita utumiki wawo pachihema chokumanako, ndipo ndiwo amene azisenza zolakwa za anthuwo.+ Iwo asakhale ndi cholowa+ pakati pa ana a Isiraeli. Limeneli ndi lamulo mpaka kalekale m’mibadwo yanu yonse.

  • 2 Mbiri 26:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Kenako iwo anatsutsa mfumu Uziya+ n’kuiuza kuti: “Mfumu Uziya, si ntchito yanu+ kufukiza kwa Yehova koma ntchito yofukizayi ndi ya ansembe, ana a Aroni,+ amene anayeretsedwa. Tulukani m’nyumba yopatulikayi popeza mwachita zosakhulupirika, ndipo sizikubweretserani ulemerero uliwonse+ pamaso pa Yehova Mulungu.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena